< Masalimo 14 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa; palibe amene amachita zabwino.
Рече безумник у срцу свом: Нема Бога; неваљали су, гадна су дела њихова; нема никога да добро твори.
2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi, kuyangʼana anthu onse kuti aone ngati alipo wina wanzeru, amene amafunafuna Mulungu.
Господ погледа с неба на синове човечије, да види има ли који разуман, тражи ли који Бога.
3 Onse atembenukira kumbali, onse pamodzi asanduka oyipa; palibe amene amachita zabwino, palibiretu ndi mmodzi yemwe.
Сви су зашли, сви се покварили, нема никога добро да твори, нема ни једног.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse? Akudya anthu anga ngati chakudya chawo ndipo satamanda Yehova?
Зар се неће опаметити који чине безакоње, једу народ мој као што једу хлеб, не призивају Господа?
5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu, pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
Онде ће задрхтати од страха; јер је Господ у роду праведном.
6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka, koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
Смејете се ономе што убоги ради; али Господ њега заклања.
7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni! Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake, Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!
Ко ће послати са Сиона помоћ Израиљу? Кад Господ поврати заробљени народ свој, онда ће се радовати Јаков и веселиће се Израиљ.

< Masalimo 14 >