< Masalimo 12 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
大衛的詩,交與伶長。調用第八。 耶和華啊,求你幫助,因虔誠人斷絕了; 世人中間的忠信人沒有了。
2 Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
人人向鄰舍說謊; 他們說話,是嘴唇油滑,心口不一。
3 Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
凡油滑的嘴唇和誇大的舌頭, 耶和華必要剪除。
4 Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
他們曾說:我們必能以舌頭得勝; 我們的嘴唇是我們自己的, 誰能作我們的主呢?
5 “Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
耶和華說:因為困苦人的冤屈 和貧窮人的歎息, 我現在要起來, 把他安置在他所切慕的穩妥之地。
6 Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
耶和華的言語是純淨的言語, 如同銀子在泥爐中煉過七次。
7 Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
耶和華啊,你必保護他們; 你必保佑他們永遠脫離這世代的人。
8 Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.
下流人在世人中升高, 就有惡人到處遊行。

< Masalimo 12 >