< Masalimo 11 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Yehova ine ndimathawiramo. Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti, “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
大衛的詩,交與伶長。 我是投靠耶和華; 你們怎麼對我說:你當像鳥飛往你的山去。
2 Pakuti taona oyipa akunga mauta awo; ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta, pobisala pawo kuti alase olungama mtima.
看哪,惡人彎弓,把箭搭在弦上, 要在暗中射那心裏正直的人。
3 Tsono ngati maziko awonongeka, olungama angachite chiyani?”
根基若毀壞, 義人還能做甚麼呢?
4 Yehova ali mʼNyumba yake yoyera; Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba. Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu; maso ake amawayesa.
耶和華在他的聖殿裏; 耶和華的寶座在天上; 他的慧眼察看世人。
5 Yehova amayesa olungama, koma moyo wake umadana ndi oyipa, amene amakonda zachiwawa.
耶和華試驗義人; 惟有惡人和喜愛強暴的人,他心裏恨惡。
6 Iye adzakhuthulira pa oyipa makala amoto ndi sulufule woyaka; mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
他要向惡人密布網羅; 有烈火、硫磺、熱風,作他們杯中的分。
7 Pakuti Yehova ndi wolungama, Iye amakonda chilungamo; ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.
因為耶和華是公義的,他喜愛公義; 正直人必得見他的面。