< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Aleluja! Zahvaljujte Jahvi jer je dobar, jer je vječna ljubav njegova!
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Neka rekne dom Izraelov: “Vječna je ljubav njegova!”
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Neka rekne dom Aronov: “Vječna je ljubav njegova!”
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Svi koji se Jahve boje neka reknu: “Vječna je ljubav njegova!”
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Iz tjeskobe Jahvu ja zazvah: on me usliša i oslobodi.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
Jahve je sa mnom i ja ne strahujem: što mi tko može?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
Jahve je sa mnom, pomoć moja, i zbunjene gledam dušmane.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Bolje se Jahvi uteći nego se uzdat' u čovjeka.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
Bolje se Jahvi uteći nego se uzdat' u mogućnike.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Pogani me okružiše: imenom ih Jahvinim uništih.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Opkoliše me odasvud: imenom ih Jahvinim uništih.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Opkoliše me poput pčela, ubod im žeže kao trnje zapaljeno: imenom ih Jahvinim uništih.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Gurahu me, gurahu, da me obore, ali mi Jahve pomože.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
Jahve je moja snaga i pjesma, on mi je spasitelj.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Čuj! Radost i spasenje odzvanja šatorima pravednika: Jahvina se proslavi desnica,
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
Jahvina me uzdigne desnica, Jahvina se proslavi desnica!
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
Ne, umrijeti neću nego živjeti i kazivat ću djela Jahvina.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
Kaznom teškom kaznio me Jahve, ali me smrti ne preda.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Otvorite mi širom vrata pravde: ući ću, Jahvi zahvalit'!
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
“Ovo su vrata Jahvina, na njih ulaze pravedni!”
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Zahvalit ću ti što si me uslišio i moj postao spasitelj.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
Kamen što ga odbaciše graditelji postade kamen zaglavni.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
Jahvino je to djelo: kakvo čudo u očima našim!
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
Ovo je dan što ga učini Jahve: kličimo i radujmo se njemu!
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
O Jahve, spasenje nam daj! Jahve, sreću nam daj!
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Blagoslovljen koji dolazi u imenu Jahvinu! Blagoslivljamo vas iz Doma Jahvina!
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
Obasjao nas Bog Jahve! Složite povorku s grančicama u ruci sve do rogova žrtvenika.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Ti si Bog moj - tebi zahvaljujem: Bože moj, tebe ja uzvisujem.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Zahvaljujte Jahvi jer je dobar, jer je vječna ljubav njegova!

< Masalimo 118 >