< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Mudre izreke Salomona, sina Davidova, kralja izraelskog:
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
da se spozna mudrost i pouka, da se shvate razumne riječi;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
da se primi umna pouka, pravda i pravica i nepristranost;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
da se dade pamet neiskusnima, mladiću znanje i umijeće;
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
kad mudar čuje, da umnoži znanje, a razuman steče mudrije misli;
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
da razumije izreke i prispodobe, riječi mudraca i njihove zagonetke.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Strah je Gospodnji početak spoznaje, ali ludi preziru mudrost i pouku.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Poslušaj, sine moj, pouku oca svoga i ne odbacuj naputka svoje majke!
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Jer će ti biti ljupki vijenac na glavi i ogrlica oko tvoga vrata.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Sine moj, ako te grešnici mame, ne pristaj;
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
ako bi rekli: “Hodi s nama, da vrebamo krv, čekamo u zasjedi nevina ni za što;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
da ih progutamo žive kao carstvo smrti i cijele kao one koji silaze u grob; (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
naplijenit ćemo svakojaka blaga, napuniti svoje kuće plijenom;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
bacat ćeš s nama svoj ždrijeb, svi ćemo zajedno imati jednu kesu.”
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Sine moj, ne idi s njima na put, makni nogu od njihove staze.
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Jer na zlo trče svojim nogama i hite prolijevati krv.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Jer uzalud je razapinjati mrežu pred očima svima pticama.
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
A oni vrebaju vlastitu krv, postavljaju zasjedu svojemu životu.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Takva je sudba svih lakomih na ružan dobitak: on ih života stane.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Mudrost glasno uzvikuje na ulici, na trgovima diže svoj glas;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
propovijeda po bučnim uglovima, na otvorenim gradskim vratima govori svoje riječi:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
“Dokle ćete, vi glupi, ljubiti glupost i dokle će podsmjevačima biti milo podsmijevanje, i dokle će bezumnici mrziti znanje?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Poslušajte moju opomenu! Gle, svoj duh pred vas izlijevam, hoću vas poučiti svojim riječima.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Koliko sam vas zvala, a vi ste odbijali; pružala sam ruku, ali je nitko ne opazi.
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Nego ste odbacili svaki moj savjet i niste poslušali moje opomene;
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
zato ću se i ja smijati vašoj propasti, rugat ću se kad vas obuzme tjeskoba:
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
kad navali na vas strah kao nevrijeme i zgrabi vas propast kao vihor, kad navali na vas nevolja i muka.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Tada će me zvati, ali se ja neću odazvati; tražit će me, ali me neće naći.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Jer su mrzili spoznaju i nisu izabrali Gospodnjeg straha
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
niti su poslušali moj savjet, nego su prezreli svaku moju opomenu.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Zato će jesti plod svojeg vladanja i nasititi se vlastitih savjeta.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Jer glupe će ubiti njihovo odbijanje, a nemar će upropastiti bezumne.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
A tko sluša mene, bezbrižan ostaje i spokojno živi bez straha od zla.”

< Miyambo 1 >