< Masalimo 11 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Yehova ine ndimathawiramo. Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti, “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
Pour la fin, psaume de David. Je me confie dans le Seigneur: comment dites-vous à mon âme: Émigré sur la montagne comme un passereau?
2 Pakuti taona oyipa akunga mauta awo; ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta, pobisala pawo kuti alase olungama mtima.
Parce que voilà que les pécheurs ont tendu un arc; ils ont préparé leurs flèches dans un carquois, pour percer dans les ténèbres les hommes droits de cœur.
3 Tsono ngati maziko awonongeka, olungama angachite chiyani?”
Parce que, ce que vous avez établi, ils l’ont détruit; mais le juste, qu’a-t-il fait?
4 Yehova ali mʼNyumba yake yoyera; Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba. Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu; maso ake amawayesa.
Le Seigneur est dans son saint temple; le Seigneur, son trône est dans le ciel. Ses yeux observent le pauvre: ses paupières interrogent les enfants des hommes.
5 Yehova amayesa olungama, koma moyo wake umadana ndi oyipa, amene amakonda zachiwawa.
Le Seigneur interroge le juste et l’impie; mais celui qui aime l’iniquité hait son âme.
6 Iye adzakhuthulira pa oyipa makala amoto ndi sulufule woyaka; mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
Il fera pleuvoir sur les pécheurs des pièges; le feu, le soufre et le vent des tempêtes sont la part de leur calice.
7 Pakuti Yehova ndi wolungama, Iye amakonda chilungamo; ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.
Car le Seigneur est juste et il aime la justice: son visage a vu l’équité.

< Masalimo 11 >