< Yobu 15 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Alors, répondant, Eliphaz, le Thémanite, dit:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
Un sage répondra-t-il comme parlant en l’air, et remplira-t-il son cœur d’une chaleur ardente?
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
Tu reprends celui qui n’est pas égal à toi, et tu dis ce qui n’est pas avantageux.
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
Autant qu’il est en toi tu as anéanti la crainte de Dieu, et tu as détruit les prières devant Dieu.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
Car ton iniquité a instruit la bouche, et tu imites le langage des blasphémateurs.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Ta bouche te condamnera, et non pas moi, et tes lèvres te répondront.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
Est-ce toi qui es né le premier homme, et qui as été formé avant les collines?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Est-ce que tu as ouï le conseil de Dieu, et sa sagesse sera-telle inférieure à toi?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
Que sais-tu que nous ignorions? Que comprends-tu que nous ne sachions?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
Il est des vieillards et des anciens parmi nous, beaucoup plus vieux que tes pères.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Est-ce une chose considérable que Dieu te console? Mais tes paroles perverses l’en empêchent.
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Pourquoi ton cœur t’élève-t-il, et as-tu les yeux fixes, comme si tu pensais de grandes choses?
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
Pourquoi ton esprit s’enfle-t-il contre Dieu, pour que tu profères de ta bouche de tels discours?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
Qu’est-ce qu’un homme, pour qu’il soit sans tache et paraisse juste, étant né d’une femme?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Voilà que parmi ses saints personne n’est immuable, et les cieux ne sont pas purs en sa présence.
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
Combien plus abominable et inutile est un homme qui boit l’iniquité comme l’eau.
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
Je te le montrerai, écoute-moi: je te raconterai ce que j’ai vu.
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
Des sages le publient, et ils ne dissimulent pas ce qu’ils ont appris de leurs pères,
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
À qui seuls a été donnée cette terre, et aucun étranger n’a passé au milieu d’eux.
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
Durant tous ses jours, l’impie s’enorgueillit, et le nombre des années de sa tyrannie est incertain.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
Le bruit de la terreur est toujours à ses oreilles; et quoiqu’il y ait la paix, lui soupçonne toujours des embûches.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
Il ne croit pas qu’il puisse revenir des ténèbres à la lumière, il voit de tous côtés autour de lui un glaive.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
Quand il se remue pour chercher son pain, il sent que le jour des ténèbres est prêt en sa main.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
La tribulation l’épouvantera, et l’angoisse l’environnera comme un roi qui se prépare au combat.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
Car il a étendu contre Dieu sa main, et il s’est roidi contre le Tout-Puissant.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
Il a couru contre lui, la tête levée, et il s’est armé d’un cou inflexible.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
La graisse à couvert sa face, et l’embonpoint pend de ses côtés.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
Il a habité dans des villes désolées, dans des maisons désertes, qui ont été réduites en monceaux de ruines.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
Il ne s’enrichira point, et son bien ne subsistera pas, et il ne jettera pas ses racines dans la terre.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
Il ne sortira pas des ténèbres; une flamme desséchera ses rameaux, et il sera emporté par le souffle de sa bouche.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Trompé par une vaine erreur, il ne croira pas qu’il puisse être racheté à aucun prix.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Avant que ses jours soient accomplis, il périra; et ses mains se sécheront.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
Sa grappe sera frappée comme la vigne, qui l’est dans sa première fleur, et comme l’olivier qui laisse tomber sa fleur.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
Car tout ce qu’amasse un hypocrite est sans fruit, et un feu dévorera les tabernacles de ceux qui reçoivent volontiers des présents.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
Il a conçu la douleur et il a enfanté l’iniquité, et son cœur prépare des fourberies.