< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Bongani uThixo, memezani ibizo lakhe; lizazise phakathi kwabantu izenzo zakhe
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Hlabelelani kuye, hlabelelani indumiso kuye; likhulume ngezenzo zakhe zonke ezimangalisayo.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Jabulani ebizweni lakhe elingcwele; kazithokoze inhliziyo zabo abamdingayo uThixo.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Dingani uThixo lamandla akhe, limdinge yena njalonjalo.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Khumbulani izenzo zakhe ezimangalisayo azenzayo, izimangaliso azenzayo, lezahlulelo azikhulumayo,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
lina zizukulwane zika-Abhrahama inceku yakhe, lina madodana kaJakhobe, abakhethiweyo bakhe.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
UnguThixo uNkulunkulu wethu; izahlulelo zakhe zisemhlabeni wonke.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
Uyasikhumbula isivumelwano sakhe nini lanini, ilizwi lomlayo wakhe, okwezizukulwane ezizinkulungwane,
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
isivumelwano asenza lo-Abhrahama, isifungo asifungayo ku-Isaka.
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
Wakuqinisa lokhu kuJakhobe kwaba yisimiso ku-Israyeli njengesivumelwano saphakade:
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
wathi “Ngizalinika ilizwe laseKhenani njengesabelo selifa lenu.”
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Kwathi besesebalutshwana, bebalutshwana kakhulu, beyizihambi kulo,
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
bezula kuzizwe ngezizwe besuka komunye umbuso besiya komunye.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
Kavumelanga loba ngubani ukubancindezela; wawakhuza amakhosi ngenxa yabo:
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
“Lingabathinti abagcotshiweyo bami; lingahlukuluzi abaphrofethi bami.”
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
Waletha indlala elizweni wachitha zonke iziphala zokudla;
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
wathumela indoda yabandulela uJosefa owathengiswa waba yisigqili.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
Bambhonxula inyawo zakhe ngezibopho, wabotshwa intamo ngezinsimbi,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
kwaze kwathi lokho ayekutsho ngaphambili kwagcwaliseka, kwaze kwathi ilizwi likaThixo latshengisa ukuthi wayeqinisile.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Inkosi yathumela ukuthi akhululwe, umbusi wezizwe wamkhulula.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
Wamenza umbusi wendlu yakhe, umbusi wakho konke okwakungokwakhe,
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
ukuqondisa amakhosana akhe njengokubona kwakhe lokufundisa abadala bakhe inhlakanipho.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Kwathi-ke u-Israyeli wayangena eGibhithe; uJakhobe wahlala njengowezizweni elizweni likaHamu.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
UThixo wenza abantu bakhe banda kakhulu; wabenza baba banengi kakhulu bandela izitha zabo,
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
kwathi inhliziyo zabo wazenza zazonda abantu bakhe, bakha amacebo amabi ngezinceku zakhe.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Wathuma uMosi inceku yakhe, lo-Aroni ayebakhethile.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
Benza iziboniso zakhe ezimangalisayo phakathi kwabo, izimanga zakhe elizweni likaHamu.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Wathumela umnyama wenza ilizwe laba mnyama kanti angithi babewahlamukele amazwi akhe?
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
Waguqula amanzi abo aba ligazi, okwenza inhlanzi zawo zafa.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Ilizwe labo lanyakazela ngamaxoxo, angena ezindlini zokulala ezababusi babo.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
Wakhuluma, kwavela umtshitshi wezibawu, lenswintila elizweni labo lonke.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Wenza izulu labo laba yisiqhotho, laba lombane elizweni labo lonke;
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
wacakazela phansi amavini abo lemikhiwa, waphundla izihlahla zelizwe labo.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
Wakhuluma zatheleka izintethe, izintethe ezingelakubalwa;
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
zadla yonke into eluhlaza elizweni labo, zadla izithelo zomhlabathi wabo.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
Ngemva kwalokho wasebulala amazibulo wonke elizweni labo, izithelo zokuqala zobulisa babo.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
Wamkhupha u-Israyeli, ethwele esisitheka isiliva legolide, kakwaba lamunye phakathi kwezizwana zabo owehlulwa yikufa.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
IGibhithe yathokoza ngokusuka kwabo, ngoba base bemesaba kubi u-Israyeli.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Wendlala iyezi lagubuzela, lomlilo ukukhanyisa ebusuku.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
Bacela wabalethela izagwaca, wabasuthisa ngesinkwa sasezulwini.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
Wavula ilitshe amanzi antshaza; njengomfula ageleza enkangala.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
Ngoba wakhumbula isithembiso sakhe esingcwele esaphiwa inceku yakhe u-Abhrahama.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
Wabakhupha abantu bakhe ngokuthokoza, abakhethiweyo bakhe ngenhlokomo yentokozo.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
Wabapha amazwe ezizwe, badla ilifa lalokho okwakuginqelwe ngabanye,
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
ukuze bagcine iziqondiso zakhe njalo balalele imithetho yakhe. Dumisani uThixo.

< Masalimo 105 >