< Masalimo 109 >

1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
Kumqondisi wokuhlabela. ElikaDavida. Ihubo. Oh Nkulunkulu, wena engikudumisayo, ungali ulokhu uthule,
2 pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
ngoba abantu ababi abalenkohliso bayivulile imilomo yabo bekhuluma ngami; bakhuluma bengigcona ngendimi zabo zamanga.
3 Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
Bangihonqolozela ngamazwi enzondo; bayangisukela nje kungelasizatho.
4 Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
Ukubathanda kwami bakuphindisela ngokungisola, kodwa ngingumuntu womkhuleko.
5 Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
Bangiphindisela okuhle ngokubi, langenzondo ukubathanda kwami.
6 Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
Bathi, “Khethani umuntu omubi ozamelana laye; ombeka icala kame kwesokunene sakhe.
7 Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
Nxa esethonisiswa kafunyanwe elecala, futhi sengathi imikhuleko yakhe ingamlahla.
8 Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Sengathi insuku zakhe zingabazilutshwana; kakube lomunye ozathatha isikhundla sakhe sobukhokheli.
9 Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
Sengathi abantwabakhe bangaba zintandane lomkakhe abe ngumfelokazi.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
Sengathi abantwabakhe bangaba zinzulane zeziceli; sengathi bangaxotshwa emizini yabo esingamanxiwa.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
Sengathi lowo aboleke kuye angamemuka konke alakho; sengathi labezizweni bangaphanga izithelo zamandla akhe.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
Akungabikhona omenzela umusa loba ozwela izintandane zakhe.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
Sengathi izizukulwane zakhe zingaphela, amabizo abo esulwe esizukulwaneni esilandelayo.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
Sengathi ububi bukayise bungakhunjulwa phambi kukaThixo, sengathi isono sikanina singacitshi lanini.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
Sengathi izono zabo zingahlala zisobala phambi kukaThixo, ukuze aphelise du ukukhunjulwa kwabo emhlabeni.
16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
Ngoba kazange akhumbule ukwenza umusa kodwa wabazingelela ukufa abayanga labaswelayo labadabukileyo enhliziyweni.
17 Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
Wayekuthanda ukwethesa isithuko, sengathi singehlela kuye. Wayengakuthandi ukubusisa sengathi kungaba khatshana laye.
18 Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
Wayevunula ukuthuka njengesigqoko; kwangena emzimbeni wakhe njengamanzi, emathanjeni akhe njengamafutha.
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
Sengathi kungaba njengengubo athandelwe ngayo njengebhanti abotshwe ngalo lanini.”
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
Sengathi lokhu kungaba yisijeziso sikaThixo kulabo abangethesa amacala, labo abakhuluma okubi ngami.
21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
Kodwa wena, Oh Thixo woBukhosi, ngenzela kuhle ngenxa yebizo lakho; ngenxa yokulunga kothando lwakho akungikhulule.
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
Ngoba ngingumyanga ngiyaswela, lenhliziyo yami ilimele ngaphakathi kwami.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
Ngiyafiphala njengethunzi lakusihlwa; ngiyaphetshulwa njengentethe.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
Amadolo ami asebuthakathaka ngokuzila ukudla; umzimba wami usuzacile usutshwabhene.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
Sengiyinto yokuhlekisa kulabo abangibeka amacala; bathi bengibona banyikinye amakhanda abo.
26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
Akungisize, Oh Thixo Nkulunkulu wami; ngisindisa ngokuya ngothando lwakho.
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
Kumele bakwazi ukuthi lokhu ngokwesandla sakho; wena, Oh Thixo, nguwe okwenzileyo.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
Bangangiqalekisa, kodwa wena uzabusisa; bathi bayahlasela bayangiswe, kodwa inceku yakho izathokoza.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
Abangivukelayo kabembeswe ihlazo bagoqelwe ngokuyangeka njengengubo.
30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
Ngomlomo wami ngizambabaza kakhulu uThixo; ngisemphakathini ngizamdumisa.
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.
Ngoba umi ngakwesokunene salowo oswelayo, ukusindisa impilo yakhe kulabo abamnikela ekufeni.

< Masalimo 109 >