< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
`Of Dauid. Mi soule, blesse thou the Lord; and alle thingis that ben with ynne me, blesse his hooli name.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Mi soule, blesse thou the Lord; and nyle thou foryete alle the yeldyngis of him.
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
Which doith merci to alle thi wickidnessis; which heelith alle thi sijknessis.
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
Which ayenbieth thi lijf fro deth; which corowneth thee in merci and merciful doyngis.
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
Which fillith thi desijr in goodis; thi yongthe schal be renulid as the yongthe of an egle.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
The Lord doynge mercies; and doom to alle men suffringe wrong.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
He made hise weies knowun to Moises; hise willis to the sones of Israel.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
The Lord is merciful doer, and merciful in wille; longe abidinge, and myche merciful.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
He schal not be wrooth with outen ende; and he schal not thretne with outen ende.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
He dide not to vs aftir oure synnes; nether he yeldide to vs aftir oure wickidnessis.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
For bi the hiynesse of heuene fro erthe; he made strong his merci on men dredynge hym.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
As myche as the eest is fer fro the west; he made fer oure wickidnessis fro vs.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
As a fadir hath merci on sones, the Lord hadde merci on men dredynge him;
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
for he knewe oure makyng.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
He bithouyte that we ben dust, a man is as hey; his dai schal flowre out so as a flour of the feeld.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
For the spirit schal passe in hym, and schal not abide; and schal no more knowe his place.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
But the merci of the Lord is fro with out bigynnyng, and til in to with outen ende; on men dredinge hym. And his riytfulnesse is in to the sones of sones;
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
to hem that kepen his testament. And ben myndeful of hise comaundementis; to do tho.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
The Lord hath maad redi his seete in heuene; and his rewme schal be lord of alle.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Aungels of the Lord, blesse ye the Lord; ye myyti in vertu, doynge his word, to here the vois of hise wordis.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Alle vertues of the Lord, blesse ye the Lord; ye mynystris of hym that doen his wille.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Alle werkis of the Lord, blesse ye the Lord, in ech place of his lordschipe; my soule, blesse thou the Lord.

< Masalimo 103 >