< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
The preier of a pore man, whanne he was angwishid, and schedde out his speche bifore the Lord. Lord, here thou my preier; and my crie come to thee.
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
Turne not awei thi face fro me; in what euere dai Y am troblid, bowe doun thin eere to me. In what euere day Y schal inwardli clepe thee; here thou me swiftli.
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
For my daies han failid as smoke; and my boonus han dried vp as critouns.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
I am smytun as hei, and myn herte dried vp; for Y haue foryete to eete my breed.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Of the vois of my weilyng; my boon cleuede to my fleische.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
I am maad lijk a pellican of wildirnesse; Y am maad as a niyt crowe in an hous.
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
I wakide; and Y am maad as a solitarie sparowe in the roof.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Al dai myn enemyes dispisiden me; and thei that preisiden me sworen ayens me.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
For Y eet aschis as breed; and Y meddlide my drinke with weping.
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
Fro the face of the ire of thin indignacioun; for thou reisinge me hast hurtlid me doun.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
Mi daies boweden awei as a schadewe; and Y wexede drie as hei.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
But, Lord, thou dwellist with outen ende; and thi memorial in generacioun and in to generacioun.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Lord, thou risinge vp schalt haue merci on Sion; for the tyme `to haue merci therof cometh, for the tyme cometh.
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
For the stones therof plesiden thi seruauntis; and thei schulen haue merci on the lond therof.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
And, Lord, hethen men schulen drede thi name; and alle kingis of erthe schulen drede thi glori.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
For the Lord hath bildid Sion; and he schal be seen in his glorie.
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
He bihelde on the preier of meke men; and he dispiside not the preier of hem.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
Be these thingis writun in an othere generacioun; and the puple that schal be maad schal preise the Lord.
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
For he bihelde fro his hiye hooli place; the Lord lokide fro heuene in to erthe.
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
For to here the weilingis of feterid men; and for to vnbynde the sones of slayn men.
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
That thei telle in Sion the name of the Lord; and his preising in Jerusalem.
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
In gaderinge togidere puplis in to oon; and kingis, that thei serue the Lord.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
It answeride to hym in the weie of his vertu; Telle thou to me the fewnesse of my daies.
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
Ayenclepe thou not me in the myddil of my daies; thi yeris ben in generacioun and in to generacioun.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Lord, thou foundidist the erthe in the bigynnyng; and heuenes ben the werkis of thin hondis.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
Tho schulen perische, but thou dwellist perfitli; and alle schulen wexe eelde as a clooth. And thou schalt chaunge hem as an hiling, and tho schulen be chaungid;
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
but thou art the same thi silf, and thi yeeris schulen not faile.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
The sones of thi seruauntis schulen dwelle; and the seed of hem schal be dressid in to the world.

< Masalimo 102 >