< Miyambo 9 >
1 Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
La sagesse a construit sa maison. Elle a défini ses sept piliers.
2 Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
Elle a préparé sa viande. Elle a mélangé son vin. Elle a également mis sa table.
3 Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
Elle a envoyé ses servantes. Elle crie depuis les plus hauts lieux de la ville:
4 “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
« Celui qui est simple, qu'il se tourne ici! » Quant à celui qui est dépourvu d'intelligence, elle lui dit,
5 “Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
« Viens, mange un peu de mon pain, Buvez un peu du vin que j'ai mélangé!
6 Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
Abandonnez vos habitudes simples, et vivez. Marchez dans la voie de la compréhension. »
7 Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
Celui qui corrige un moqueur s'expose à être insulté. Celui qui réprouve un homme méchant s'expose à des abus.
8 Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
Ne réprimandez pas le moqueur, de peur qu'il ne vous haïsse. Réprimandez une personne sage, et elle vous aimera.
9 Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
Instruisez une personne sage, et elle sera encore plus sage. Enseignez à un juste, et il augmentera son savoir.
10 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
La crainte de Yahvé est le commencement de la sagesse. La connaissance du Saint est la compréhension.
11 Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
Car par moi vos jours seront multipliés. Les années de votre vie seront augmentées.
12 Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
Si tu es sage, tu l'es pour toi-même. Si vous vous moquez, vous seul le supporterez.
13 Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
La femme folle est bruyante, indiscipliné, et ne sait rien.
14 Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
Elle est assise à la porte de sa maison, sur un siège dans les hauts lieux de la ville,
15 kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
pour appeler ceux qui passent, qui vont droit sur leur chemin,
16 Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
« Celui qui est simple, qu'il se rende ici. » Quant à celui qui est dépourvu d'intelligence, elle lui dit,
17 “Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
« L'eau volée est douce. La nourriture mangée en secret est agréable. »
18 Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )
Mais il ne sait pas que les esprits des défunts sont là, que ses invités sont dans les profondeurs de Sheol. (Sheol )