< Yesaya 42 >

1 “Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza, amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye. Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
« Voici mon serviteur, que je soutiens, mon élu, en qui mon âme se complaît: J'ai mis mon Esprit sur lui. Il apportera la justice aux nations.
2 Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu, kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
Il ne criera pas, ni élever la voix, ni qu'il soit entendu dans la rue.
3 Bango lophwanyika sadzalithyola, ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa. Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
Il ne brisera pas un roseau meurtri. Il n'éteindra pas une mèche qui brûle faiblement. Il rendra fidèlement la justice.
4 sadzafowoka kapena kukhumudwa mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi, ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
Il n'échouera pas et ne se découragera pas, jusqu'à ce qu'il ait établi la justice sur la terre, et les îles attendent sa loi. »
5 Yehova Mulungu amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika, amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka, amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo, ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
Dieu Yahvé, celui qui a créé les cieux et les a étendus, celui qui a étendu la terre et ce qui en sort, celui qui donne le souffle à son peuple et l'esprit à ceux qui y marchent, dit:
6 “Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama; ndikugwira dzanja ndipo ndidzakuteteza. Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
« Moi, Yahvé, je vous ai appelés dans la justice. Je te tiendrai la main. Je te garderai, et te faire une alliance pour le peuple, comme une lumière pour les nations,
7 Udzatsekula maso a anthu osaona, udzamasula anthu a mʼndende ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
pour ouvrir les yeux des aveugles, pour faire sortir les prisonniers du donjon, et ceux qui sont assis dans les ténèbres sortiront de la prison.
8 “Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo! Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense kapena matamando anga kwa mafano.
« Je suis Yahvé. C'est mon nom. Je ne donnerai pas ma gloire à un autre, ni mes louanges à des images gravées.
9 Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi, ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano; zinthuzo zisanaonekere Ine ndakudziwitsani.”
Voici, les premières choses sont arrivées et je déclare des choses nouvelles. Je vous en parle avant qu'elles n'arrivent. »
10 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi, inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo. Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
Chantez à Yahvé un chant nouveau, et ses louanges jusqu'aux extrémités de la terre, vous qui descendez à la mer, et tout ce qui s'y trouve, les îles et leurs habitants.
11 Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo; midzi ya Akedara ikondwere. Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe; afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
Que le désert et ses villes élèvent leurs voix, avec les villages que Kedar habite. Que les habitants de Sela chantent. Qu'ils crient du haut des montagnes!
12 Atamande Yehova ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
Qu'ils rendent gloire à Yahvé, et publier ses louanges dans les îles.
13 Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu, adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo; akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo ndipo adzagonjetsa adani ake.
Yahvé sortira comme un homme puissant. Il suscitera le zèle comme un homme de guerre. Il lancera un cri de guerre. Oui, il criera à haute voix. Il triomphera de ses ennemis.
14 Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
« J'ai gardé le silence pendant longtemps. J'ai été silencieux et je me suis retenu. Maintenant, je vais crier comme une femme en travail. Je vais souffler et haleter.
15 Ndidzawononga mapiri ndi zitunda ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse; ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba ndipo ndidzawumitsa maiwe.
Je détruirai les montagnes et les collines, et dessécher toutes leurs herbes. Je vais faire des îles des rivières, et assèchera les piscines.
16 Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe, ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo; ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala ndipo ndidzasalaza malo osalala. Zimenezi ndizo ndidzachite; sindidzawataya.
Je ferai venir les aveugles par un chemin qu'ils ne connaissent pas. Je les conduirai dans des sentiers qu'ils ne connaissent pas. Je rendrai les ténèbres légères devant eux, et les endroits tortueux sont droits. Je vais faire ces choses, et je ne les abandonnerai pas.
17 Koma onse amene amadalira mafano amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
« Ceux qui se confient aux images gravées, qui racontent des images en fusion, « Vous êtes nos dieux, seront retournés. Ils seront totalement déçus.
18 “Imvani, agonthi inu; yangʼanani osaona inu, kuti muone!
« Écoutez, sourds, et regarde, tu es aveugle, que vous pouvez voir.
19 Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi? Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma? Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano, kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
Qui est aveugle, sinon mon serviteur? Ou qui est aussi sourd que le messager que j'envoie? Qui est aussi aveugle que celui qui est en paix, et aussi aveugle que le serviteur de Yahvé?
20 Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale; makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
Tu vois beaucoup de choses, mais tu n'observes pas. Ses oreilles sont ouvertes, mais il n'écoute pas.
21 Chinamukomera Yehova chifukwa cha chilungamo chake, kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
Il a plu à Yahvé, à cause de sa justice, de magnifier la loi. et le rendre honorable.
22 Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo, onsewa anawakola mʼmaenje kapena akuwabisa mʼndende. Tsono asanduka chofunkha popanda wina wowapulumutsa kapena kunena kuti, “Abwezeni kwawo.”
Mais c'est un peuple volé et pillé. Ils sont tous coincés dans des trous, et ils sont cachés dans les prisons. Ils sont devenus des captifs, et personne ne les délivre, et un pillage, et personne ne dit: « Restaurez-les!
23 Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
Qui parmi vous prête l'oreille à cela? Qui écoutera et entendra pour le temps à venir?
24 Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha, ndi Israeli kwa anthu akuba? Kodi si Yehova, amene ife tamuchimwirayu? Pakuti sanathe kutsatira njira zake; ndipo sanamvere malangizo ake.
qui a donné Jacob comme butin, et Israël aux voleurs? N'est-ce pas Yahvé, celui contre qui nous avons péché? Car ils n'ont pas voulu marcher dans ses voies, et ils ont désobéi à sa loi.
25 Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.
Il a donc déversé sur lui l'ardeur de sa colère, et la force de la bataille. Ça l'a enflammé tout autour, mais il ne le savait pas. Ça l'a brûlé, mais il ne l'a pas pris à cœur. »

< Yesaya 42 >