< Miyambo 7 >

1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
Mon fils, garde mes paroles. Portez mes commandements en vous.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Observez mes commandements et vivez! Garde mon enseignement comme la prunelle de tes yeux.
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Liez-les sur vos doigts. Écris-les sur la tablette de ton cœur.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Dis à la sagesse: « Tu es ma sœur. » Appelez la compréhension de votre parent,
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
afin qu'ils te préservent de la femme étrangère, de l'étrangère qui flatte avec ses mots.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
Car à la fenêtre de ma maison, J'ai regardé à travers mon treillis.
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
J'ai vu parmi les simples. J'ai discerné parmi les jeunes un jeune homme dépourvu d'intelligence,
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
passant dans la rue près de son coin, il a pris le chemin de sa maison,
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
au crépuscule, au soir du jour, au milieu de la nuit et dans l'obscurité.
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
Voici qu'une femme vint à sa rencontre, vêtue comme une prostituée, et avec une intention maligne.
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
Elle est bruyante et provocante. Ses pieds ne restent pas dans sa maison.
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
Maintenant elle est dans les rues, maintenant sur les places, et se cachant à chaque coin de rue.
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
Alors elle le saisit et l'embrassa. Avec un visage impudent, elle lui dit:
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
« Les sacrifices d'actions de grâces sont avec moi. Aujourd'hui, je me suis acquitté de mes vœux.
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
C'est pourquoi je suis sorti à ta rencontre, pour chercher assidûment ta face, et je t'ai trouvé.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
J'ai étendu ma couche avec des tapis de tapisserie, avec des tissus rayés de la laine d'Égypte.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
J'ai parfumé mon lit avec de la myrrhe, de l'aloès et de la cannelle.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Venez, prenons notre dose d'amour jusqu'au matin. Consolons-nous en aimant.
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
Car mon mari n'est pas à la maison. Il est parti pour un long voyage.
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
Il a pris avec lui un sac d'argent. Il reviendra à la maison à la pleine lune. »
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
Avec des paroles persuasives, elle l'a égaré. Avec la flatterie de ses lèvres, elle l'a séduit.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
Il la suivit immédiatement, comme un bœuf va à l'abattoir, comme un idiot qui se prend les pieds dans un nœud coulant.
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
Jusqu'à ce qu'une flèche lui transperce le foie, comme un oiseau qui se précipite vers le piège, et ne sait pas que ça va lui coûter la vie.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Maintenant donc, mes fils, écoutez-moi. Faites attention aux mots de ma bouche.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Ne laisse pas ton cœur se tourner vers ses voies. Ne vous égarez pas dans ses sentiers,
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
car elle a jeté de nombreux blessés. Oui, tous ses morts sont une puissante armée.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)
Sa maison est le chemin du séjour des morts, en descendant dans les chambres de la mort. (Sheol h7585)

< Miyambo 7 >