< Miyambo 6 >

1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
Mon fils, si tu es devenu la garantie de ton prochain, si vous avez frappé vos mains en gage pour un étranger,
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
vous êtes piégés par les mots de votre bouche; tu es pris au piège par les paroles de ta bouche.
3 Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
Fais-le maintenant, mon fils, et délivre-toi, puisque tu es tombé dans la main de ton voisin. Allez, humiliez-vous. Appuyez votre plaidoyer auprès de votre voisin.
4 Usagone tulo, usawodzere.
Ne laisse pas tes yeux s'endormir, ni le sommeil à vos paupières.
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
Libère-toi, comme une gazelle de la main du chasseur, comme un oiseau échappant au piège de l'oiseleur.
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
Va vers la fourmi, paresseux. Considérez ses manières, et soyez sage;
7 Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
qui n'ont ni chef, ni surveillant, ni dirigeant,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
lui fournit du pain en été, et recueille sa nourriture dans la moisson.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
Combien de temps vas-tu dormir, paresseux? Quand sortiras-tu de ton sommeil?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
Un peu de sommeil, un peu d'assoupissement, un petit pliage des mains pour dormir...
11 umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
ainsi votre pauvreté viendra comme un voleur, et votre rareté en tant qu'homme armé.
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
Un homme sans valeur, un homme d'iniquité, est celui qui marche avec une bouche perverse,
13 amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
qui cligne des yeux, qui fait des signes avec ses pieds, qui fait des gestes avec ses doigts,
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
dans le cœur duquel il y a de la perversité, qui invente continuellement le mal, qui sème toujours la discorde.
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
C'est pourquoi sa calamité viendra soudainement. Il sera brisé soudainement, et ce sans remède.
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
Il y a six choses que Yahvé déteste; oui, sept qui sont une abomination pour lui:
17 maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
des yeux arrogants, une langue mensongère, des mains qui ont versé du sang innocent,
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
un cœur qui conçoit de mauvais plans, des pieds qui sont prompts à courir au mal,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
un faux témoin qui profère des mensonges, et celui qui sème la discorde entre les frères.
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
Mon fils, garde le commandement de ton père, et n'abandonnez pas l'enseignement de votre mère.
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
Lie-les continuellement sur ton cœur. Attachez-les autour de votre cou.
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
Quand tu marcheras, il te conduira. Quand vous dormirez, il veillera sur vous. Quand vous vous réveillerez, il parlera avec vous.
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
Car le commandement est une lampe, et la loi est légère. Les reproches d'instruction sont le chemin de la vie,
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
pour vous préserver de la femme immorale, de la flatterie de la langue de l'épouse volage.
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
Ne convoite pas sa beauté dans ton cœur, ni la laisser vous captiver avec ses paupières.
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
Car une prostituée vous réduit à un morceau de pain. La femme adultère chasse votre précieuse vie.
27 Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
Un homme peut-il ramasser du feu sur ses genoux, et que ses vêtements ne soient pas brûlés?
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
Ou peut-on marcher sur des charbons ardents, et ses pieds ne seront pas brûlés?
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
Il en est de même pour celui qui va vers la femme de son prochain. Quiconque la touche ne restera pas impuni.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
Les hommes ne méprisent pas un voleur. s'il vole pour se satisfaire quand il a faim,
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
mais s'il est retrouvé, il restituera sept fois. Il donnera toutes les richesses de sa maison.
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
Celui qui commet un adultère avec une femme est dépourvu d'intelligence. Celui qui le fait détruit sa propre âme.
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
Il recevra des blessures et le déshonneur. Son opprobre ne sera pas effacé.
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
Car la jalousie excite la fureur du mari. Il n'épargnera pas au jour de la vengeance.
35 Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
Il ne tiendra compte d'aucune rançon, il ne sera pas non plus satisfait, même si vous lui faites de nombreux cadeaux.

< Miyambo 6 >