< Miyambo 6 >
1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
My sonne, if thou be surety for thy neighbour, and hast striken hands with the stranger,
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
Thou art snared with the wordes of thy mouth: thou art euen taken with the woordes of thine owne mouth.
3 Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
Doe this nowe, my sonne, and deliuer thy selfe: seeing thou art come into the hande of thy neighbour, goe, and humble thy selfe, and sollicite thy friends.
4 Usagone tulo, usawodzere.
Giue no sleepe to thine eyes, nor slumber to thine eyelids.
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
Deliuer thy selfe as a doe from the hande of the hunter, and as a birde from the hande of the fouler.
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
Goe to the pismire, O sluggarde: beholde her waies, and be wise.
7 Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
For shee hauing no guide, gouernour, nor ruler,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
Prepareth her meat in the sommer, and gathereth her foode in haruest.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
Howe long wilt thou sleepe, O sluggarde? when wilt thou arise out of thy sleepe?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
Yet a litle sleepe, a litle slumber, a litle folding of the hands to sleepe.
11 umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
Therefore thy pouertie commeth as one that trauaileth by the way, and thy necessitie like an armed man.
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
The vnthriftie man and the wicked man walketh with a froward mouth.
13 amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
He maketh a signe with his eyes: he signifieth with his feete: he instructeth with his fingers.
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
Lewde things are in his heart: he imagineth euill at all times, and raiseth vp contentions.
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
Therefore shall his destruction come speedily: hee shall be destroyed suddenly without recouerie.
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
These sixe things doeth the Lord hate: yea, his soule abhorreth seuen:
17 maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
The hautie eyes, a lying tongue, and the hands that shed innocent blood,
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
An heart that imagineth wicked enterprises, feete that be swift in running to mischiefe,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
A false witnesse that speaketh lyes, and him that rayseth vp contentions among brethren.
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
My sonne, keepe thy fathers commandement, and forsake not thy mothers instruction.
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
Binde them alway vpon thine heart, and tye them about thy necke.
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
It shall leade thee, when thou walkest: it shall watch for thee, when thou sleepest, and when thou wakest, it shall talke with thee.
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
For the commandement is a lanterne, and instruction a light: and corrections for instruction are the way of life,
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
To keepe thee from the wicked woman, and from ye flatterie of ye tongue of a strange woman.
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
Desire not her beautie in thine heart, neither let her take thee with her eye lids.
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
For because of the whorish woman a man is brought to a morsell of bread, and a woman wil hunt for the precious life of a man.
27 Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
Can a man take fire in his bosome, and his clothes not be burnt?
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
Or can a man go vpon coales, and his feete not be burnt?
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
So he that goeth in to his neighbours wife, shall not be innocent, whosoeuer toucheth her.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
Men do not despise a thiefe, when he stealeth, to satisfie his soule, because he is hungrie.
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
But if he be founde, he shall restore seuen folde, or he shall giue all the substance of his house.
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
But he that committeth adulterie with a woman, he is destitute of vnderstanding: he that doeth it, destroyeth his owne soule.
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
He shall finde a wounde and dishonour, and his reproch shall neuer be put away.
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
For ielousie is the rage of a man: therefore he will not spare in the day of vengeance.
35 Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
He cannot beare the sight of any raunsome: neither will he consent, though thou augment the giftes.