< Masalimo 1 >
1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Blessed is the man that doeth not walke in the counsell of the wicked, nor stand in the way of sinners, nor sit in ye seate of the scornefull:
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
But his delite is in the Lawe of the Lord, and in his Lawe doeth he meditate day and night.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
For he shall be like a tree planted by the riuers of waters, that will bring foorth her fruite in due season: whose leafe shall not fade: so whatsoeuer he shall doe, shall prosper.
4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
The wicked are not so, but as the chaffe, which the winde driueth away.
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
Therefore the wicked shall not stande in the iudgement, nor sinners in the assemblie of the righteous.
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
For the Lord knoweth the way of the righteous, and the way of the wicked shall perish.