< Miyambo 5 >

1 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
Moj sin, prisluhni moji modrosti in svoje uho pripogni k mojemu razumevanju,
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
da boš lahko upošteval preudarnost in da bodo tvoje ustnice lahko obvarovale spoznanje.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
Kajti ustnice tuje ženske kapljajo kakor satovje in njena usta so bolj prilizljiva kakor olje,
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
toda njen konec je grenek kakor pelin, oster kakor dvorezen meč.
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
Njena stopala gredo dol k smrti, njeni koraki se prijemljejo pekla. (Sheol h7585)
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
Da ne bi preudarjal steze življenja, njene poti so premične, da jih ti ne moreš spoznati.
7 Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
Zato mi torej prisluhnite, oh vi otroci in ne odidite od besed mojih ust.
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
Svojo pot odstrani daleč od nje in ne pridi blizu vrat njene hiše,
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
da ne bi svoje časti dal drugim in svojih let krutemu,
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
da ne bi bili tujci nasičeni s tvojim premoženjem in bi bili tvoji napori v hiši tujca
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
in boš končno žaloval, ko bo tvoje meso in tvoje telo iztrošeno
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
in rečeš: »Kako sem sovražil poučevanje in je moje srce preziralo opomin
13 Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
in nisem ubogal glasu svojih učiteljev niti svojega ušesa nagnil k tem, ki so me poučevali!
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
Bil sem skoraj v vsem zlu v sredi skupnosti in zbora.«
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
Pij vode iz svojega lastnega vodnega zbiralnika in tekoče vode iz svojega lastnega izvira.
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
Naj bodo tvoji studenci razpršeni naokoli in reke vodá po ulicah.
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
Naj bodo samo tvoji lastni in ne s teboj [tudi] tujčevi.
18 Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
Naj bo tvoj studenec blagoslovljen in razveseljuj se z ženo svoje mladosti.
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
Ona naj bo kakor ljubeča košuta in prijetna srna. Naj te njene prsi zadovoljijo ob vseh časih in vedno bodi očaran z njeno ljubeznijo.
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
Zakaj hočeš biti ti, moj sin, očaran s tujo žensko in objemati naročje tujke?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
Kajti človekove poti so pred Gospodovimi očmi in on preudarja vsa njegova ravnanja.
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
Njegove lastne krivičnosti bodo zlobnega vzele k sebi in držan bo z vrvmi svojih grehov.
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
Umrl bo brez poučevanja in v veličini svoje neumnosti bo zašel na stranpot.

< Miyambo 5 >