< Mlaliki 1 >

1 Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
Besede Pridigarja, Davidovega sina, kralja v Jeruzalemu.
2 “Zopandapake! Zopandapake!” atero Mlaliki. “Zopandapake kotheratu! Zopandapake.”
»Ničevost ničevosti, « pravi Pridigar, »ničevost ničevosti; vse je ničevost.«
3 Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
Kakšno korist ima človek od vsega svojega truda, ki se ga loteva pod soncem?
4 Mibado imabwera ndipo mibado imapita, koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
En rod mineva in drug rod prihaja, toda zemlja ostaja na veke.
5 Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
Tudi sonce vzhaja in sonce gre dol in hiti k svojemu kraju, kjer vstaja.
6 Mphepo imawombera cha kummwera ndi kukhotera cha kumpoto; imawomba mozungulirazungulira, kumangobwererabwerera komwe yachokera.
Veter gre proti jugu in se obrača k severu, nenehno se vrti naokoli in veter se ponovno vrača, glede na svoje kroge.
7 Mitsinje yonse imakathira ku nyanja, koma nyanjayo sidzaza; kumene madziwo amachokera, amabwereranso komweko.
Vse reke tečejo v morje, vendar morje ni polno; na kraj, od koder reke prihajajo, tja se ponovno vrnejo.
8 Zinthu zonse ndi zotopetsa, kutopetsa kwake ndi kosaneneka. Maso satopa ndi kuona kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
Vse stvari so polne truda, človek tega ne more izreči. Oko ni nasičeno z gledanjem niti uho nasičeno s poslušanjem.
9 Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso, zomwe zinachitika kale zidzachitikanso. Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
Stvar, ki je bila, to je ta, ki bo in to, kar je storjeno, je to, kar bo storjeno, in pod soncem ni nobene nove stvari.
10 Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti, “Taona! Ichi ndiye chatsopano?” Chinalipo kale, kalekale; chinalipo ife kulibe.
Ali je katerakoli stvar, o čemer bi bilo lahko rečeno: »Glej, to je novo? To je bilo že od starih časov, ki so bili pred nami.«
11 Anthu akale sakumbukiridwa, ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu sadzakumbukiridwa ndi iwo amene adzabwere pambuyo pawo.
Ni spominjanja o prejšnjih stvareh niti ne bo kakršnegakoli spominjanja o stvareh, ki pridejo s tistimi, ki bodo prišle potem.
12 Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
Jaz, Pridigar, sem bil kralj nad Izraelom v Jeruzalemu.
13 Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
Izročil sem svoje srce, da išče in preiskuje z modrostjo glede vseh stvari, ki so storjene pod nebom. To bolečo muko je Bog izročil človeškim sinovom, da bi bili vežbani s tem.
14 Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
Videl sem vsa dela, ki so storjena pod soncem in glej, vse je ničevost in draženje duha.
15 Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa; chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
To, kar je skrivljeno, ne more biti izravnano; in to, kar je pomanjkljivo, ne more biti prešteto.
16 Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
Posvetoval sem se s svojim lastnim srcem, rekoč: »Glej! Prišel sem k velikemu premoženju in prejel sem več modrosti kakor vsi tisti, ki so bili pred menoj v Jeruzalemu. Da, moje srce je imelo sijajno izkušnjo modrosti in spoznanja.
17 Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
Izročil sem svoje srce, da spoznam modrost in da spoznam norost in neumnost. Zaznal sem, da je tudi to draženje duha.
18 Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.
Kajti v mnogi modrosti je mnogo žalosti in kdor povečuje spoznanje, povečuje bridkost.«

< Mlaliki 1 >