< Miyambo 17 >

1 Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
Melhor é um bocado secco, e com elle a tranquillidade, do que a casa cheia de victimas, com contenda.
2 Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
O servo prudente dominará sobre o filho que faz envergonhar; e entre os irmãos repartirá a herança.
3 Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
O crisol é para a prata, e o forno para o oiro; mas o Senhor prova os corações.
4 Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
O malfazejo attenta para o labio iniquo: o mentiroso inclina os ouvidos á lingua maligna.
5 Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
O que escarnece do pobre insulta ao que o creou: o que se alegra da calamidade não ficará innocente.
6 Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
Corôa dos velhos são os filhos dos filhos; e a gloria dos filhos são seus paes.
7 Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
Não convem ao tolo o labio excellente: quanto menos ao principe o labio mentiroso.
8 Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
Pedra preciosa é o presente aos olhos dos que o recebem; para onde quer que se volver, servirá de proveito.
9 Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
O que encobre a transgressão busca a amizade, mas o que renova a coisa, separa os maiores amigos.
10 Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
Mais profundamente entra a reprehensão no prudente, do que cem açoites no tolo.
11 Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
Na verdade o rebelde não busca senão o mal, mas mensageiro cruel se enviará contra elle.
12 Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
Encontre-se com o homem a ursa roubada dos filhos; mas não o louco na sua estulticia.
13 Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
Quanto áquelle que torna mal por bem, não se apartará o mal da sua casa.
14 Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
Como o que solta as aguas, é o principio da contenda, pelo que, antes que sejas envolto, deixa a porfia.
15 Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
O que justifica ao impio, e condemna ao justo, ambos são abominaveis ao Senhor, tanto um como o outro.
16 Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
De que serviria o preço na mão do tolo para comprar a sabedoria, visto que não tem entendimento?
17 Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
Em todo o tempo ama o amigo; e para a angustia nasce o irmão.
18 Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
O homem falto d'entendimento dá a mão, ficando por fiador diante do seu companheiro.
19 Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
O que ama a contenda ama a transgressão; o que alça a sua porta busca a ruina.
20 Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
O perverso de coração nunca achará o bem; e o que tem a lingua dobre virá a cair no mal
21 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
O que gera a um tolo para a sua tristeza o faz; e o pae do insensato não se alegrará.
22 Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
O coração alegre serve de bom remedio, mas o espirito abatido virá a seccar os ossos.
23 Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
O impio tomará o presente do seio, para perverter as veredas da justiça.
24 Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
No rosto do entendido se vê a sabedoria, porém os olhos do louco estão nas extremidades da terra.
25 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
O filho insensato é tristeza para seu pae, e amargura para a que o pariu.
26 Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
Não é bom tambem pôr pena ao justo, nem que firam os principes ao que obra justamente.
27 Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
Retem as suas palavras o que possue o conhecimento, e o homem d'entendimento é de precioso espirito.
28 Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.
Até o tolo, quando se cala, será reputado por sabio; e o que cerrar os seus labios por entendido.

< Miyambo 17 >