< Miyambo 8 >
1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Não clama porventura a sabedoria, e a intelligencia não dá a sua voz?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
No cume das alturas, junto ao caminho, nas encruzilhadas das veredas se põe.
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
Da banda das portas da cidade, á entrada da cidade, e á entrada das portas está gritando.
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
A vós, ó homens, clamo; e a minha voz se dirige aos filhos dos homens.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
Entendei, ó simplices, a prudencia: e vós, loucos, entendei do coração.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Ouvi, porque fallarei coisas excellentes: os meus labios se abrirão para a equidade.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
Porque a minha bocca proferirá a verdade, e os meus labios abominam a impiedade.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
Em justiça estão todas as palavras da minha bocca: não ha n'ellas nenhuma coisa tortuosa nem perversa.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
Todas ellas são rectas para o que bem as entende, e justas para os que acham o conhecimento.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Acceitae a minha correcção, e não a prata: e o conhecimento, mais do que o oiro fino escolhido.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
Porque melhor é a sabedoria do que os rubins; e tudo o que mais se deseja não se pode comparar com ella.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
Eu, a sabedoria, habito com a prudencia, e acho a sciencia dos conselhos.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
O temor do Senhor é aborrecer o mal: a soberba, e a arrogancia, e o mau caminho, e a bocca perversa, aborreço.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
Meu é o conselho e verdadeira sabedoria: eu sou o entendimento, minha é a fortaleza.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
Por mim reinam os reis e os principes ordenam justiça.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
Por mim dominam os dominadores, e principes, todos os juizes da terra.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
Eu amo aos que me amam, e os que de madrugada me buscam me acharão.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
Riquezas e honra estão comigo; como tambem opulencia duravel e justiça.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
Melhor é o meu fructo do que o fino oiro e do que o oiro refinado, e as minhas novidades do que a prata escolhida.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
Faço andar pelo caminho da justiça, no meio das veredas do juizo.
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
Para que faça herdar bens permanentes aos que me amam, e eu encha os seus thesouros.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
O Senhor me possuiu no principio de seus caminhos, desde então, e antes de suas obras.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
Desde a eternidade fui ungida, desde o principio, antes do começo da terra.
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
Quando ainda não havia abysmos, fui gerada, quando ainda não havia fontes carregadas d'aguas.
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
Antes que os montes se houvessem assentado, antes dos outeiros, eu era gerada.
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
Ainda não tinha feito a terra, nem os campos, nem o principio dos mais miudos do mundo.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
Quando preparava os céus, ahi estava eu, quando compassava ao redor a face do abysmo,
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
Quando affirmava as nuvens de cima, quando fortificava as fontes do abysmo,
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
Quando punha ao mar o seu termo, para que as aguas não trespassassem o seu mando, quando compunha os fundamentos da terra.
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
Então eu estava com elle por alumno: e eu era cada dia as suas delicias, folgando perante elle em todo o tempo;
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
Folgando no seu mundo habitavel, e achando as minhas delicias com os filhos dos homens.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Agora, pois, filhos, ouvime, porque bemaventurados serão os que guardarem os meus caminhos.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Ouvi a correcção, e sêde sabios, e não a rejeiteis.
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Bemaventurado o homem que me dá ouvidos, velando ás minhas portas cada dia, esperando ás hombreiras das minhas entradas.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
Porque o que me achar achará a vida, e alcançará favor do Senhor.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
Mas o que peccar contra mim violentará a sua propria alma: todos os que me aborrecem amam a morte.