< Miyambo 17 >

1 Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
Melior est buccella sicca cum gaudio, quam domus plena victimis cum iurgio.
2 Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
Servus sapiens dominabitur filiis stultis, et inter fratres hereditatem dividet.
3 Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
Sicut igne probatur argentum, et aurum camino: ita corda probat Dominus.
4 Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
Malus obedit linguae iniquae: et fallax obtemperat labiis mendacibus.
5 Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
Qui despicit pauperem, exprobrat factori eius: et qui ruina laetatur alterius, non erit impunitus.
6 Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
Corona senum filii filiorum: et gloria filiorum patres eorum.
7 Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
Non decent stultum verba composita: nec principem labium mentiens.
8 Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
Gemma gratissima, expectatio praestolantis: quocumque se vertit, prudenter intelligit.
9 Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
Qui celat delictum, quaerit amicitias: qui altero sermone repetit, separat foederatos.
10 Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
Plus proficit correptio apud prudentem, quam centum plagae apud stultum.
11 Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
Semper iurgia quaerit malus: angelus autem crudelis mittetur contra eum.
12 Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
Expedit magis ursae occurrere raptis foetibus, quam fatuo confidenti in stultitia sua.
13 Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
Qui reddit mala pro bonis, non recedet malum de domo eius.
14 Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
Qui dimittit aquam, caput est iurgiorum: et antequam patiatur contumeliam, iudicium deserit.
15 Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
Qui iustificat impium, et qui condemnat iustum, abominabilis est uterque apud Deum.
16 Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
Quid prodest stulto habere divitias, cum sapientiam emere non possit? Qui altum facit domum suam, quaerit ruinam: et qui evitat discere, incidet in mala.
17 Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
Omni tempore diligit qui amicus est: et frater in angustiis comprobatur.
18 Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
Stultus homo plaudet manibus cum spoponderit pro amico suo.
19 Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
Qui meditatur discordias, diligit rixas: et qui exaltat os suum, quaerit ruinam.
20 Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
Qui perversi cordis est, non inveniet bonum: et qui vertit linguam, incidet in malum.
21 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
Natus est stultus in ignominiam suam: sed nec pater in fatuo laetabitur.
22 Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
Animus gaudens aetatem floridam facit: spiritus tristis exiccat ossa.
23 Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
Munera de sinu impius accipit, ut pervertat semitas iudicii.
24 Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
In facie prudentis lucet sapientia: oculi stultorum in finibus terrae.
25 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
Ira patris, filius stultus: et dolor matris quae genuit eum.
26 Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
Non est bonum, damnum inferre iusto: nec percutere principem, qui recta iudicat.
27 Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
Qui moderatur sermones suos, doctus et prudens est: et pretiosi spiritus vir eruditus.
28 Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.
Stultus quoque si tacuerit, sapiens reputabitur: et si compresserit labia sua, intelligens.

< Miyambo 17 >