< Miyambo 11 >

1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
Awurade kyi asisi nsania, na nʼani gye nokware nkaribo ho.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
Ahantan ba a, animguase na edi so, nanso ahobrɛase de nyansa ba.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
Teefo nokwaredi kyerɛ wɔn kwan; nanso nkontompofo ano ntanta sɛe wɔn.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Ahonya nka hwee wɔ abufuwhyew da no, nanso trenee gye nkwa fi owu mu.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
Wɔn a wonni bɔne no trenee bɔ kwan tee ma wɔn, nanso amumɔyɛfo amumɔyɛsɛm brɛ wɔn ase.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
Pɛyɛfo treneeyɛ gye wɔn, nanso akɔnnɔ bɔne afiri yi nkontompofo.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
Sɛ omumɔyɛfo wu a, nʼanidaso yera; nea osusuw sɛ obenya afi ne tumi mu nyinaa no yɛ ɔkwa.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
Wogye ɔtreneeni fi amane mu, na ɛba omumɔyɛfo so mmom.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
Nea onsuro Onyame de nʼano sɛe ne yɔnko, nanso ɔtreneeni nam nimdeɛ so fi mu.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
Sɛ atreneefo di yiye a, kuropɔn no di ahurusi; nanso amumɔyɛfo wu a, wɔbɔ ose.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
Pɛyɛfo nhyira ma kuropɔn no kɔ so, nanso amumɔyɛfo ano ma ɛbɔ.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
Onipa a onni adwene no bu ne yɔnko animtiaa, nanso nea ɔwɔ nhumu no to ne tɛkrɛma nnareka.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
Nsekudi sɛe ahotoso, nanso nea wɔwɔ ne mu ahotoso no kora ahintasɛm.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Ɔman a enni akwankyerɛ no bɔ, nanso afotufo dodow ma nkonimdi ba.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
Nea odi akagyinamu ma ɔfoforo no behu amane, na nea ɔmmfa ne nsa nhyɛ awowasi ase no aso mu dwo no.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
Ɔbea a ne yam ye no, wɔde obu ma no, nanso mmarima atirimɔdenfo nya ahode nkutoo.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
Ɔyamyefo ye ma ne ho, na otirimɔdenfo de ɔhaw ba nʼankasa so.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
Omumɔyɛfo nya akatua a ennyina, nanso nea ogu trenee aba no twa aba a edi mu.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
Nea ɔyɛ nokware treneeni no nya nkwa, nanso nea ɔkɔ so yɛ bɔne no kɔ owu mu.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
Awurade kyi nnipa a wɔn koma akyea, na nʼani gye wɔn a wɔn akwan ho nni asɛm no ho.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Gye to mu sɛ, amumɔyɛfo benya wɔn akatua, na atreneefo benya wɔn ti adidi mu.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
Ɔbea hoɔfɛfo a ontumi nsi gyinae no te sɛ sika kaa a ɛhyɛ prako hwene mu.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
Atreneefo apɛde wie yiye, nanso amumɔyɛfo anidaso wie abufuwhyew.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
Obi yɛ adɔe, na onya ne ho bebree; obi nso yɛ pɛpɛe, nanso ehia no.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
Ɔyamyefo bɛkɔ so anya ne ho; na nea ɔma ebinom mee no nso bɛmee.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
Nnipa dome nea ɔde atoko sie, na nhyira ba nea ɔtɔn ne de so.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
Nea ɔhwehwɛ papa akyi kwan no nya anisɔ, na nea ɔhwehwɛ bɔne no, bɔne ba ne so.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
Nea ɔde ne ho to nʼahonyade so no bɛhwe ase, na ɔtreneeni bɛyɛ frɔmfrɔm sɛ ahabammono.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
Nea ɔde ɔhaw bɛto nʼabusua so no bedi mframa ade, na ɔkwasea bɛyɛ onyansafo somfo.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
Ɔtreneeni aba yɛ nkwadua, na nea ogye akra no yɛ onyansafo.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Kyerɛwsɛm no ka se, “Ɛyɛ den sɛ wobegye onipa pa nkwa; na wɔn a wonnye asɛm no nni ne nnebɔneyɛfo no de, dɛn na ɛbɛba wɔn so?”

< Miyambo 11 >