< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
Salomo mmebusɛm: Ɔba nyansafo ma nʼagya ani gye, na ɔba kwasea brɛ ne na awerɛhow.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Ɔkwan bɔne so ahonya nni bo, nanso trenee gye onipa fi owu mu.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
Awurade remma ɔkɔm nne ɔtreneeni na omumɔyɛfo de, ɔka nʼadepa gu.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
Nsa a ɛnyɛ adwuma ma onipa di hia, nanso nsiyɛfo nsa de ahonya ba.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
Nea ɔboaboa nnɔbae ano wɔ ahuhurubere no yɛ ɔba nyansafo na nea ɔda wɔ twabere mu no yɛ ɔba nimguaseni.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Atreneefo hyɛ nhyira kyɛw na akakabensɛm ayɛ omumɔyɛfo anom ma.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
Ɔtreneeni nkae yɛ nhyira, na omumɔyɛfo din bɛporɔw.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
Koma mu nyansafo tie ɔhyɛ nsɛm, na ɔkwasea kasafo hwe ase.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Ɔnokwafo nantew dwoodwoo, na nea ɔfa akwan kɔntɔnkye so no ho bɛda adi.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
Nea ɔde nitan bu nʼani no de ɔhaw ba, na ɔkwasea kasafo hwe ase.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
Ɔtreneeni anom yɛ nkwa asuti, na akakabensɛm ayɛ omumɔyɛfo anom ma.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Ɔtan kanyan mpaapaemu, nanso ɔdɔ kata mfomso nyinaa so.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
Wohu nyansa wɔ nhumufo anom, na abaa fata nea onni adwene akyi.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
Anyansafo kora nimdeɛ, nanso ɔkwasea ano frɛfrɛ ɔsɛe.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
Adefo ahonya yɛ wɔn kuropɔn a wɔabɔ ho ban, nanso ahiafo hia yɛ wɔn asehwe.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
Atreneefo akatua de nkwa brɛ wɔn, na nea amumɔyɛfo nya no de asotwe brɛ wɔn.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
Nea otie ntetew pa no kyerɛ nkwa kwan, na nea ɔpo nteɛso no di afoforo anim yera kwan.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
Nea ɔkata nitan so no yɛ ɔtorofo, na nea odi nseku no yɛ ɔkwasea.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
Mfomso mpa ɔkasa bebree mu, na nea ɔkora ne tɛkrɛma no yɛ onyansafo.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
Ɔtreneeni tɛkrɛma yɛ dwetɛ ankasa nanso omumɔyɛfo koma nni bo.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
Atreneefo ano ma bebree aduan, na atemmu a nkwaseafo nni nti wowuwu.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
Awurade nhyira de ahonya ba, na ɔmfa ɔbrɛ mmata ne nya ho.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
Bɔneyɛ yɛ anigyede ma ɔkwasea, nanso nea ɔwɔ nimdeɛ anigye wɔ nyansa mu.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
Nea amumɔyɛfo suro no bɛba wɔn so; na nea atreneefo pɛ no, wɔde bɛma wɔn.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
Sɛ ahum no betwa mu a, amumɔyɛfo yera, nanso atreneefo gyina hɔ pintinn afebɔɔ.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
Sɛnea nsa keka ɛse, na wusiw kɔ aniwa no, saa ara na ɔkwadwofo yɛ ma wɔn a wɔsoma no.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
Awurade suro ma nkwa tenten, nanso wotwa amumɔyɛfo nkwa so.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
Atreneefo anidaso de ahotɔ ba, nanso amumɔyɛfo anidaso nkosi hwee.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
Awurade kwan yɛ guankɔbea ma ɔtreneeni, nanso ɛyɛ ɔsɛe ma wɔn a wɔyɛ bɔne.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
Wɔrentɔre atreneefo ase da, nanso amumɔyɛfo renka asase no so.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
Nyansa fi ɔtreneeni anom ba nanso tɛkrɛma a ɛdaadaa no, wobetwa akyene.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
Ɔtreneeni ano nim ade a ɛfata na omumɔyɛfo ano nim nea ɛyɛ nnaadaasɛm nko ara.

< Miyambo 10 >