< Miyambo 1 >
1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Ordsprog av Salomo, Davids sønn, Israels konge.
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
Av dem kan en lære visdom og tukt og å skjønne forstandige ord;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
av dem kan en motta tukt til klokskap og lære rettferdighet og rett og rettvishet;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
de kan gi de enfoldige klokskap, de unge kunnskap og tenksomhet.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Den vise skal høre på dem og gå frem i lærdom, og den forstandige vinne evne til å leve rett.
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Av dem kan en lære å forstå ordsprog og billedtale, vismenns ord og deres gåter.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Å frykte Herren er begynnelsen til kunnskap; visdom og tukt foraktes av dårer.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Hør, min sønn, på din fars tilrettevisning og forlat ikke din mors lære!
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
For de er en fager krans for ditt hode og kjeder om din hals.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Min sønn! Når syndere lokker dig, da samtykk ikke!
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
Når de sier: Kom med oss! Vi vil lure efter blod, sette feller for de uskyldige uten grunn;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
vi vil sluke dem levende som dødsriket, med hud og hår, likesom det sluker dem som farer ned i graven; (Sheol )
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
vi vil finne alle slags kostelig gods, fylle våre hus med rov;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
du skal få kaste lodd om det med oss, vi skal alle ha samme pung -
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
slå da ikke følge med dem, min sønn, hold din fot borte fra deres sti!
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
For deres føtter haster til det onde, og de er snare til å utøse blod;
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
til ingen nytte blir garnet utspent så alle fuglene ser det;
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
de lurer efter sitt eget blod, de setter feller for sig selv.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Så går det hver den som søker urettferdig vinning; den tar livet av sine egne herrer.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Visdommen roper høit på gaten, den lar sin røst høre på torvene;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
på hjørnet av larmfylte gater roper den, ved portinngangene, rundt omkring i byen taler den og sier:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Hvor lenge vil I uforstandige elske uforstand og spotterne ha lyst til spott og dårene hate kunnskap?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Vend om og gi akt på min tilrettevisning! Da vil jeg la min ånd velle frem for eder, jeg vil kunngjøre eder mine ord.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Fordi jeg ropte, og I ikke vilde høre, fordi jeg rakte ut min hånd, og ingen gav akt,
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
fordi I forsmådde alle mine råd og ikke vilde vite av min tilrettevisning,
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
så vil også jeg le når ulykken rammer eder, jeg vil spotte når det kommer som I reddes for,
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
når det I reddes for, kommer som et uvær, og eders ulykke farer frem som en stormvind, når trengsel og nød kommer over eder.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Da skal de kalle på mig, men jeg svarer ikke; de skal søke mig, men ikke finne mig.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Fordi de hatet kunnskap og ikke vilde frykte Herren,
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
fordi de ikke vilde vite av mitt råd og foraktet all min tilrettevisning,
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
derfor skal de ete frukten av sine gjerninger, og av sine onde råd skal de mettes.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
For de uforstandiges selvrådighet dreper dem, og dårenes trygghet ødelegger dem;
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
men den som hører på mig, skal bo trygt og leve i ro uten frykt for ulykke.