< Mlaliki 1 >
1 Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
Ord av predikeren, sønn av David, konge i Jerusalem.
2 “Zopandapake! Zopandapake!” atero Mlaliki. “Zopandapake kotheratu! Zopandapake.”
Bare tomhet, sier predikeren, bare idelig tomhet! Alt er tomhet.
3 Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
Hvad vinning har mennesket av alt sitt strev, som han møier sig med under solen?
4 Mibado imabwera ndipo mibado imapita, koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
Slekt går, og slekt kommer, men jorden står evindelig.
5 Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
Og solen går op, og solen går ned, og den haster tilbake til det sted hvor den går op.
6 Mphepo imawombera cha kummwera ndi kukhotera cha kumpoto; imawomba mozungulirazungulira, kumangobwererabwerera komwe yachokera.
Vinden går mot syd og vender sig mot nord; den vender og vender sig om under sin gang og begynner så atter sitt kretsløp.
7 Mitsinje yonse imakathira ku nyanja, koma nyanjayo sidzaza; kumene madziwo amachokera, amabwereranso komweko.
Alle bekker løper ut i havet, men havet blir ikke fullt; til det sted som bekkene går til, dit går de alltid igjen.
8 Zinthu zonse ndi zotopetsa, kutopetsa kwake ndi kosaneneka. Maso satopa ndi kuona kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
Alle ting strever utrettelig, ingen kan utsi det; øiet blir ikke mett av å se, og øret blir ikke fullt av å høre.
9 Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso, zomwe zinachitika kale zidzachitikanso. Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
Det som har vært, er det som skal bli, og det som har hendt, er det som skal hende, og det er intet nytt under solen.
10 Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti, “Taona! Ichi ndiye chatsopano?” Chinalipo kale, kalekale; chinalipo ife kulibe.
Er det noget hvorom en vilde si: Se, dette er nytt - så har det vært til for lenge siden, i fremfarne tider som var før oss.
11 Anthu akale sakumbukiridwa, ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu sadzakumbukiridwa ndi iwo amene adzabwere pambuyo pawo.
Det er ingen som minnes dem som har levd før, og heller ikke vil de som siden skal komme, leve i minnet hos dem som kommer efter.
12 Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
Jeg, predikeren, var konge over Israel i Jerusalem,
13 Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
og jeg vendte min hu til å ransake og utgranske med visdom alt det som hender under himmelen; det er en ond plage, som Gud har gitt menneskenes barn å plage sig med.
14 Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
Jeg sa alle de gjerninger som gjøres under solen, og se, alt sammen var tomhet og jag efter vind.
15 Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa; chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
Det som er kroket, kan ikke bli rett, og det som mangler, kan ingen regne med.
16 Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
Jeg talte med mig selv i mitt indre og sa: Se, jeg har vunnet mig større og rikere visdom enn alle som har rådet over Jerusalem før mig, og mitt hjerte har skuet megen visdom og kunnskap.
17 Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
Og jeg vendte min hu til å kjenne visdommen og kjenne dårskap og uforstand, men jeg skjønte at også dette var jag efter vind.
18 Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.
For hvor det er megen visdom, der er det megen gremmelse, og den som øker kunnskap, øker smerte.