< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
The Lord spoke to Moses in the Tent of Meeting while they were in the Sinai desert. This was on the first day of the second month of the second year after the Israelites had left Egypt. He told him,
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
“Census all the Israelites according to their tribe and family. Count every man and keep a record of each individual's name.
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
Those aged twenty or older who can do military service are to be registered by you and Aaron in their Israelite army divisions.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
A representative from each tribe, the head of a family, must be there with you.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
These are the names of the men who will work with you: From the tribe of Reuben, Elizur, son of Shedeur;
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
from the tribe of Simeon, Shelumiel, son of Zurishaddai;
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
from the tribe of Judah, Nahshon, son of Amminadab;
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
from the tribe of Issachar, Nethanel, son of Zuar;
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
from the tribe of Zebulun, Eliab, son of Helon;
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
from the sons of Joseph: from the tribe of Ephraim, Elishama, son of Ammihud, and from the tribe of Manasseh, Gamaliel, son of Pedahzur;
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
from the tribe of Benjamin, Abidan, son of Gideoni;
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
from the tribe of Dan, Ahiezer, son of Ammishaddai;
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
from the tribe of Asher, Pagiel, son of Ocran;
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
from the tribe of Gad, Eliasaph, son of Deuel;
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
and from the tribe of Naphtali, Ahira, son of Enan.”
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
These were the men chosen from the Israelite community. They were the leaders of their fathers' tribes; the heads of the families of Israel.
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
Moses and Aaron summoned these men who had been selected by name.
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
They had all the Israelites gather together on the first day of the second month, and recorded the people's genealogy according to their tribe and family, and counted up the names of all those aged twenty or older,
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
as the Lord had told Moses to do. Moses conducted this census in the Sinai desert.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Reuben, (he was Israel's firstborn son), men aged twenty or over, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
from the tribe of Reuben totaled 46,500.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Simeon, men aged twenty or over, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
from the tribe of Simeon totaled 59,300.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Gad, men aged twenty or over, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
from the tribe of Gad totaled 45,650.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Judah, men aged twenty or older, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
from the tribe of Judah, totaled 74,600.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Issachar, men aged twenty or older, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
from the tribe of Issachar, totaled 54,400.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Zebulun, men aged twenty or older, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
from the tribe of Zebulun, totaled 57,400.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Joseph: the descendants of Ephraim, men aged twenty or older, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
from the tribe of Ephraim, totaled 40,500.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
And the descendants of Manasseh, men aged twenty or older, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
from the tribe of Manasseh, totaled 32,200.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Benjamin, men aged twenty or older, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
from the tribe of Benjamin, totaled 35,400.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Dan, men aged twenty or older, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
from the tribe of Dan, totaled 62,700.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Asher, men aged twenty or older, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
from the tribe of Asher, totaled 41,500.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
The descendants of Naphtali, men aged twenty or older, were recorded by name according to the genealogical records of their tribe and families. All those registered who could serve in the army
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
from the tribe of Naphtali, totaled 53,400.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
These were the totals of the men counted and registered by Moses and Aaron, with the help of the twelve leaders of Israel, who each represented their family.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
In this way all the Israelite men aged twenty or older who were able to serve in Israel's army were registered according to their families.
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
The sum total of those registered was 603,550.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
However, the Levites were not registered with the others according to their tribe and families.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
This was because the Lord had told Moses,
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
“Don't register the tribe of Levi; don't count them in the census with the other Israelites.
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
Put the Levites in charge of the Tabernacle and of the Testimony, as well as all its furniture and everything it contains. They are the ones responsible for carrying the Tabernacle and all its items. They are to care for it, and to make their camp around it.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
When it's time to move the Tabernacle, the Levites shall take it down, and when it's time to make camp, the Levites shall put it up. Any outsider who goes near it must be put to death.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
The Israelites are to make camp according to their tribal divisions, each person in their own camp under their own flag.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
But the Levites are to set up their camp around the Tabernacle of the Testimony to stop anyone making me angry with the Israelites. The Levites are responsible for looking after the Tabernacle of the Testimony.”
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
The Israelites did everything that the Lord ordered Moses that they should do.

< Numeri 1 >