< Numeri 36 >
1 Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
Približali so se poglavarji očetov družin Gileádovih otrok, sinú Mahírja, sinú Manáseja, iz družin Jožefovih sinov in spregovorili pred Mojzesom in pred princi, poglavarji očetov Izraelovih otrok
2 Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
in rekli: » Gospod je zapovedal mojemu gospodu, naj Izraelovim otrokom da deželo za dediščino po žrebu in mojemu gospodu je bilo zapovedano od Gospoda, naj da dediščino našega brata Celofháda njegovim hčeram.
3 Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
Če bodo poročene h kateremukoli izmed sinov iz drugih rodov Izraelovih otrok, potem bo njihova dediščina vzeta od dediščine naših očetov in predana bo v dediščino rodu, kamor so sprejete. Tako bo to vzeto od žreba naše dediščine.
4 Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
Ko bo jubilej Izraelovih otrok, potem bo njihova dediščina položena v dediščino rodu kamor so sprejete. Tako bo njihova dediščina odvzeta od dediščine rodu naših očetov.«
5 Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
Mojzes je Izraelovim otrokom zapovedal glede na Gospodovo besedo, rekoč: »Rod Jožefovih sinov je dobro rekel.
6 Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
›To je stvar, ki jo je Gospod zapovedal glede Celofhádovih hčera, rekoč: ›Naj se poroče, s komer mislijo, da je najbolje, samo k družini rodu njihovega očeta se bodo poročile.
7 kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
Tako dediščina Izraelovih otrok ne bo prešla od roda k rodu, kajti vsak izmed Izraelovih otrok se bo držal k dediščini rodu svojih očetov.
8 Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
Vsaka hči, ki ima v lasti dediščino v kateremkoli rodu Izraelovih otrok, bo žena enemu iz družine rodu njenega očeta, da bodo Izraelovi otroci lahko uživali vsak človek dediščino svojih očetov.
9 Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
Niti dediščina ne bo prešla od enega rodu k drugemu rodu, temveč bo vsak izmed rodov Izraelovih otrok sebe držal k svoji lastni dediščini.‹«
10 Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
Celo kakor je Gospod zapovedal Mojzesu, tako so Celofhádove hčere storile,
11 Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
kajti Mahla, Tirca, Hogla, Milka in Noa, Celofhádove hčere, so se poročile k sinovom bratov njihovega očeta
12 Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
in poročene so bile v družine sinov Manáseja, Jožefovega sina in njihova dediščina je ostala v rodu družine njihovega očeta.
13 Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.
To so zapovedi in sodbe, ki jih je Gospod po Mojzesovi roki zapovedal Izraelovim otrokom na moábskih ravninah pri Jordanu, blizu Jerihe.