< Yoswa 10 >

1 Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
Pripetilo se je torej, ko je jeruzalemski kralj Adoní Cedek slišal, kako je Józue zavzel Aj in ga popolnoma uničil; kakor je storil Jerihi in njenemu kralju, tako je storil Aju in njegovemu kralju; in kako so prebivalci Gibeóna sklenili mir z Izraelom in so bili med njimi;
2 Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
da so se silno bali, ker je bil Gibeón veliko mesto, kakor eno izmed kraljevskih mest in ker je bil večji kakor Aj in vsi njihovi možje so bili mogočni.
3 Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
Zato je jeruzalemski kralj Adoní Cedek poslal k Hohámu, kralju v Hebrónu in Pirámu, kralju v Jarmútu in Jafíju, kralju v Lahíšu in Debírju, kralju v Eglónu, rekoč:
4 Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
»Pridite gor k meni in mi pomagajte, da bomo lahko udarili Gibeón, kajti ta je sklenil mir z Józuetom in z Izraelovimi otroki.«
5 Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
Zato se je pet kraljev izmed Amoréjcev, kralj iz Jeruzalema, kralj iz Hebróna, kralj iz Jarmúta, kralj iz Lahíša in kralj iz Eglóna, zbralo skupaj in odšlo gor, oni in vse njihove vojske in se utaborili pred Gibeónom in začeli vojno zoper njega.
6 Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
Možje iz Gibeóna so poslali k Józuetu, v tabor pri Gilgálu, rekoč: »Ne odtegni svoje roke od svojih služabnikov. Hitro pridi gor k nam in nas reši in nam pomagaj, kajti vsi kralji Amoréjcev, ki prebivajo po gorah, so skupaj zbrani zoper nas.«
7 Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
Tako se je Józue vzpel iz Gilgála, on in vse bojno ljudstvo z njim in vsi močni junaški možje.
8 Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
Gospod je rekel Józuetu: »Ne boj se jih, kajti izročil sem jih v tvojo roko. Niti mož izmed njih ne bo obstal pred teboj.«
9 Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
Józue je torej nenadoma prišel k njim in vso noč so hodili gor od Gilgála.
10 Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
Gospod jih je porazil pred Izraelom ter jih pri Gibeónu usmrtil z velikim pobojem in jih zasledoval na poti, ki gre gor do Bet Horóna in jih udarjal do Azéke in proti Makédi.
11 Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
Ko so bežali izpred Izraela in so bili pri spuščanju dol k Bet Horónu, se je pripetilo, da je Gospod z neba nanje metal velike kamne do Azéke in so umrli. Bilo jih je več, ki so umrli od kamnite toče, kakor tistih, ki so jih Izraelovi otroci usmrtili z mečem.
12 Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
Potem je Józue spregovoril Gospodu na dan, ko je pred Izraelovimi otroki Gospod izročil Amoréjce in rekel pred očmi Izraela: »Sonce, ti stoj mirno nad Gibeónom in ti luna v dolini Ajalón.«
13 Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
Sonce je stalo mirno in luna je obstala, dokler se ljudstvo ni maščevalo nad svojimi sovražniki. Mar ni to zapisano v Jasherjevi knjigi? Tako je sonce mirno stalo na sredi neba in približno cel dan ni pohitelo, da bi zašlo.
14 Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
Pred tem niti za tem ni bilo takšnega dne, da bi Gospod prisluhnil glasu moža, kajti Gospod se je bojeval za Izrael.
15 Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
Józue se je vrnil in ves Izrael z njim, k taboru pri Gilgálu.
16 Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
Toda teh pet kraljev je pobegnilo in se skrilo v votlini pri Makédi.
17 Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
To je bilo povedano Józuetu, rekoč: »Pet kraljev je najdenih skritih v votlini pri Makédi.«
18 Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
Józue je rekel: »Na odprtino votline zavalite velike kamne in poleg postavite može, da jih varujejo.
19 Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
Ne stojte, temveč sledite za svojimi sovražniki in udarite najbolj zadnje izmed njih. Ne trpite, da vstopijo v svoja mesta, kajti Gospod, vaš Bog, jih je izročil v vašo roko.«
20 Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
Pripetilo se je, ko so Józue in Izraelovi otroci z zelo velikim pokolom, dokler niso bili použiti, naredili konec njihovemu pobijanju, da je preostanek, ki je preostal izmed njih, vstopil v utrjena mesta.
21 Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
In vse ljudstvo se je v miru vrnilo k taboru, k Józuetu, pri Makédi. Nihče ni svojega jezika premaknil zoper kateregakoli izmed Izraelovih otrok.
22 Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
Potem je Józue rekel: »Odprite odprtino votline in teh pet kraljev privedite k meni, ven iz votline.«
23 Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
Storili so tako in iz votline so k njemu privedli teh pet kraljev, kralja iz Jeruzalema, kralja iz Hebróna, kralja iz Jarmúta, kralja iz Lahíša in kralja iz Eglóna.
24 Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
Ko so te kralje privedli k Józuetu, se je pripetilo, da je Józue dal poklicati vse Izraelove može in rekel poveljnikom bojevnikov, ki so odšli z njim: »Pridite bliže, položite svoja stopala na vratove teh kraljev.« Približali so se in svoja stopala položili na njihove vratove.
25 Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
Józue jim je rekel: »Ne bojte se niti ne bodite zaprepadeni, bodite močni in odločnega poguma, kajti tako bo Gospod storil vsem vašim sovražnikom, zoper katere se borite.«
26 Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
Potem jih je Józue udaril, jih usmrtil in jih obesil na pet dreves; in do večera so viseli na drevesih.
27 Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
Ob času zahajanja sonca pa se je pripetilo, da je Józue zapovedal in so jih sneli iz dreves in jih vrgli v votlino, v kateri so bili skriti in na ustje votline so položili velike kamne, ki ostajajo do točno tega dne.
28 Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
Ta dan je Józue zavzel Makédo in jo udaril z ostrino meča in njenega kralja je popolnoma uničil, njih in vse duše, ki so bile tam. Nikogar ni pustil ostati. Kralju v Makédi pa je storil, kakor je storil kralju v Jerihi.
29 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
Potem je Józue in ves Izrael z njim, prešel od Makéde v Libno in se boril zoper Libno.
30 Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
Tudi njo je Gospod izročil in njenega kralja, v Izraelovo roko. Udaril jo je z ostrino meča in vse duše, ki so bile v njej. Nikogar ni pustil preostati v njej, toda njenemu kralju je storil, kakor je storil kralju Jerihe.
31 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
Józue in ves Izrael z njim, je prešel od Libne do Lahíša in se utaboril zoper njega in se boril zoper njega.
32 Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
Gospod je Lahíš izročil v Izraelovo roko, ki so ga zavzeli na drugi dan in ga udaril z ostrino meča in vse duše, ki so bile tam, glede na vse, kar je storil Libni.
33 Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
Potem je prišel gor Horám, kralj v Gezerju, da pomaga Lahíšu, in Józue je udaril njega in njegovo ljudstvo, dokler nikogar ni pustil preostati.
34 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
Iz Lahíša je Józue prešel do Eglóna in ves Izrael z njim in utaborili so se zoper njega in se borili zoper njega.
35 Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
Zavzeli so ga na ta dan in ga udarili z ostrino meča in vse duše, ki so bile tam, je ta dan popolnoma uničil, glede na vse, kar je storil Lahíšu.
36 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
Józue in ves Izrael z njim, je odšel gor od Eglóna, do Hebróna in so se borili zoper njega,
37 Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
ga zavzeli in udarili z ostrino meča in njihovega kralja in vsa njihova mesta in vse duše, ki so bile v njem. Nikogar ni pustil preostati, glede na vse, kar je storil Eglónu, temveč ga je popolnoma uničil in vse duše, ki so bile v njem.
38 Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
Józue se je vrnil in ves Izrael z njim, do Debírja in se boril zoper njega
39 Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
in ga zavzel in njegovega kralja in vsa njegova mesta. Udarili so jih z ostrino meča in popolnoma uničili vse duše, ki so bile v njem. Nikogar ni pustil preostati. Kakor je storil Hebrónu, tako je storil Debírju in njegovemu kralju, kakor je storil tudi Libni in njenemu kralju.
40 Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
Tako je Józue udaril vso hribovito deželo, južno [deželo], [deželo] dolin, izvirov in vse njihove kralje. Ničesar ni pustil preostati, temveč je popolnoma uničil vse, kar je dihalo, kakor je zapovedal Gospod, Izraelov Bog.
41 Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
Józue jih je udarjal od Kadeš Barnée, celo do Gaze in vso Gošensko pokrajino, celo do Gibeóna.
42 Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
Vse te kralje in njihove dežele je Józue zavzel naenkrat, ker se je Gospod, Izraelov Bog, boril za Izrael.
43 Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.
In Józue se je vrnil in ves Izrael z njim, v tabor h Gilgálu.

< Yoswa 10 >