< Nehemiya 8 >

1 Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
Тада се скупи сав народ једнодушно на улицу која је пред вратима воденим, и рекоше Јездри књижевнику да донесе књигу закона Мојсијевог који даде Господ Израиљу.
2 Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
И донесе Јездра свештеник закон пред збор, у коме беху људи и жене и сви који могаху разумети, првог дана седмог месеца.
3 Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
И чита је на улици која је пред вратима воденим од јутра до подне пред људима и женама и оним који могаху разумети, и уши свему народу беху обраћене ка књизи законској.
4 Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
А Јездра књижевник стајаше на месту повисоку, које беху начинили од дрвета за то; и до њега стајаше Мататија и Сема и Анаја и Урија и Хелкија и Масија с десне стране, а с леве Федаја и Мисаило и Малахија и Асум и Асвадана, Захарија и Месулам.
5 Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
И отвори Јездра књигу на видику свем народу, јер беше више свега народа, и кад је отвори, уста сав народ.
6 Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
И Јездра благослови Господа Бога великог, а сав народ одговори: Амин, амин, подигнувши руке своје, па се савише и поклонише се Господу лицем до земље.
7 Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
А Исус и Ваније и Сервевија, Јамин, Акув, Саветај, Одија, Масија, Келита, Азарија, Јозавад, Анан, Фелаја и други Левити поучаваху народ закону, и народ стајаше на месту.
8 Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
И читаху књигу, закон Божји, разговетно и разлагаху смисао, те се разумеваше шта се читаше.
9 Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
Потом Немија, који је Тирсата, и свештеник Јездра књижевник и Левити који научаваху народ, рекоше свему народу: Овај је дан свет Господу Богу вашем; не тужите ни плачите. Јер плакаше сав народ слушајући шта говори закон.
10 Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
И рече им: Идите и једите претило и пијте слатко и шаљите делове онима који немају ништа зготовљено, јер је овај дан свет Господу нашем. Зато не будите жалосни, јер је радост Господња ваша сила.
11 Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
И Левити утишаше народ говорећи: Ћутите, јер је овај дан свет, и не будите жалосни.
12 Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
И отиде сав народ да једе и пије и да шаље делове, и веселише се веома што разумеше речи које им се казаше.
13 Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
А сутрадан скупише се главари домова отачких из свега народа, свештеници и Левити, к Јездри књижевнику да уче шта закон говори.
14 Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
И нађоше написано у закону да је Господ заповедио преко Мојсија да синови Израиљеви бораве у сеницама на празник седмог месеца.
15 Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
И објавише и прогласише по свим градовима својим и у Јерусалиму говорећи: Идите у гору, и донесите грање маслиново и грање од дивље маслине и грање миртово и палмово и грање од шумнатих дрвета, да начините сенице, како је написано.
16 Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
И народ изиђе и донесе и начини сенице сваки на свом крову и у свом трему и у тремовима дома Божјег и на улици код врата водених и на улици код врата Јефремових.
17 Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
И тако начини сенице сав збор, што се беше вратио из ропства, и борављаху под сеницама. А од времена Исуса, сина Навиног, до тог дана не чинише тако синови Израиљеви. И би весеље веома велико.
18 Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.
И читаше се књига закона Божјег сваки дан, од првог дана до последњег; и празноваше празник седам дана, а осми дан би сабор, како је уређено.

< Nehemiya 8 >