< Nahumu 1 >

1 Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
Пророцтво на Ніневію. Книга видіння елкошейця Наума.
2 Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
„Палки́й Бог, і мсти́вий Госпо́дь, Господь мстивий та лютий, — Господь мстивий до тих, хто Його ненавидить, і пам'ятає про кривду Своїх ворогів.
3 Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
Господь довготерпели́вий і великої поту́ги, та очистити винного — Він не очистить. Господь — у бурі та в ви́хрі доро́га Його, а хмара — від стіп Його ку́рява.
4 Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
Як загні́вається Він на море, то сушить його, і всі рі́ки висушує, в'яне Баша́н та Карме́л, і в'яне та квітка Ліва́ну.
5 Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
Гори тремтять перед Ним, а підгі́рки топні́ють, перед обличчям Його трясеться земля та вселе́нна, та всі її ме́шканці.
6 Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
Хто встоїть перед гнівом Його́, і хто стане у по́лум'ї люті Його? Його шал виливається, мов той огонь, і розпада́ються скелі від Нього!
7 Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
Добрий Господь, пристано́вище Він у день у́тиску, і знає Він тих, хто на Нього наді́ється!
8 koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
Але в зливі нава́льній Він зробить кінця́ між Його заколо́тниками, і ворогів зажене́ у темно́ту.
9 Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
Що ви ду́маєте проти Господа? Бо Він зробить кінця́, — не поста́не два ра́зи наси́льство.
10 Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
Бо вони переплу́тані, наче той те́рен, і повпива́лись, немов би вином, — вони будуть пожерті зовсі́м, мов солома суха!
11 Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
З тебе вийшов заду́муючий проти Господа лихо, радник нікче́мний.
12 Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
Так говорить Госпо́дь: Хоч були б найсильніші і дуже числе́нні, та пости́нані будуть вони, та й мину́ться! І хоч Я тебе мучив, та мучити більше тебе вже не бу́ду!
13 Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
А тепер Я злама́ю ярмо́ його, яке на тобі, і пу́та твої позрива́ю.
14 Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
І накаже на тебе, Ашшу́ре, Господь: Більш не буде вже сі́ятися з твого йме́ння! З дому бога твого́ Я бовва́на та і́дола ви́тну, зроблю́ тобі гро́ба із них, бо ти став легкова́жений.
15 Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.
Ось на горах ноги́ благові́сника, що звіщає про мир: Святкуй, Юдо, свята свої, виконуй прися́ги свої, бо більше не буде нікче́мний ходи́ти по тобі, — він ви́тятий ввесь!

< Nahumu 1 >