< Nahumu 1 >

1 Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
Detta är tungen öfver Nineve, och Nahums Propheties bok af Elkos.
2 Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
Gud är nitisk, och Herren är en hämnare; ja, en hämnare är Herren, och grym. Herren är en hämnare uppå sina fiendar, och den der sina ovänner intet förgäter.
3 Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
Herren är tålig, och af stora magt, och låter intet ostraffadt blifva. Han är Herren, hvilkens vägar äro uti väder och storm, och tjockt moln under hans fötter;
4 Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
Den som näpser hafvet, och förtorkar det, och uttorkar alla floder; Basan och Carmel försmäkta, och hvad som blomstras på Libanons berg, det måste försmäkta för honom.
5 Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
Bergen bäfva för honom, och högarna förgås; jorden darrar för honom; dertill jordenes krets, och alle de som bo der uppå.
6 Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
Ho kan blifva ståndandes för hans vrede? Och ho kan blifva för hans grymhet? Hans vrede brinner såsom en eld, och hällebergen remna för honom.
7 Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
Herren är mild, och ett fäste uti nödenes tid; och känner dem som trösta uppå honom.
8 koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
När floden löper öfver, så gör han en ända med henne; men sina fiendar förföljer han med mörker.
9 Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
Hvad är då det, som I tagen eder före emot Herran? Han låter del dock intet af varda; ty bedröfvelsen skall icke vara evinnerliga.
10 Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
Ty lika som när törne, de ännu om hvartannat växa, och bästa musten hafva, varda uppbränd såsom hel torr strå;
11 Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
Alltså varder det skalkarådet, som af dig kommer, ondt tänkandes emot Herran.
12 Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
Detta säger Herren: De komme så tillrustade och mägtige som de vilja, så skola de likväl omkullhuggne varda, och gå sin kos; ty jag vill ödmjuka dig, men dock icke platt förderfva dig;
13 Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
Utan vill då kasta hans ok, som du drager, ifrå dig och slita din band sönder.
14 Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
Men emot dig hafver Herren budit, att ingen dins namns säd mer blifva skall. Uti dins guds huse vill jag förgöra dig; jag skall gifva dig ena graf ibland afgudar och beläte, och du måste till skam varda.
15 Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.
Si, på bergen komma ens god bådskaps fötter, den der god tiden de bär: Håll dina högtider, Juda, och betala din löfte; ty skalken skall icke mer komma öfver dig; det är platt ute med honom.

< Nahumu 1 >