< Nahumu 1 >
1 Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
Spriedums par Ninivi. Nakuma, tā Elkozieša, parādīšanas grāmata.
2 Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
Bargs Dievs un atriebējs ir Tas Kungs, Tas Kungs ir atriebējs un ļoti bargs, Tas Kungs ir atriebējs Saviem pretiniekiem, un atmaksā Saviem ienaidniekiem.
3 Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
Tas Kungs ir lēnprātīgs un liels spēkā, bet nepamet nesodītu; Tā Kunga ceļš ir viesulī un vētrā, un padebesī ir Viņa kāju pīšļi,
4 Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
Viņš rāj jūru, un tā izsīkst, Viņš izžāvē visas upes; Basana un Karmels vīst, arī Lībanus zaļums nokalst.
5 Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
Kalni Viņa priekšā dreb, un pakalni izkūst, zeme trīc Viņa priekšā un pasaule un visi, kas tur dzīvo.
6 Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
Kas pastāvēs priekš Viņa dusmības, un kas pacelsies Viņa bardzības karstumā? Viņa dusmība ir izgāzta kā uguns, un akmens kalni no Viņa top sašķelti.
7 Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
Tas Kungs ir labs, patvērums bēdu dienā, Viņš pazīst tos, kas uz Viņu paļaujas.
8 koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
Bet ar lielu lieliem plūdiem Viņš iznīcinās viņas(Ninives) vietu, un tumsība vajās Savus(Viņa) ienaidniekus.
9 Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
Ko jūs domājat pret To Kungu? Viņš darīs galu; bēdas divreiz necelsies.
10 Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
Jo lai tie ir sapinušies kā ērkšķi un pilni kā mucas, tie taps pavisam aprīti kā sausi rugāji.
11 Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
No tevis(Ninive) ir izgājis, kas ļaunu domā pret To Kungu, nesās ar negantu padomu.
12 Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
Tā saka Tas Kungs: jebšu tiem labi izdodas, un jebšu viņu ir daudz, taču tie taps nocirsti un būs pagalam. Es tevi(Jūda) gan esmu spaidījis, bet Es tevi vairs nespaidīšu.
13 Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
Bet nu Es viņa jūgu no tevis salauzīšu un saraušu tavas saites,
14 Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
Bet pret tevi Tas Kungs ir pavēlējis, ka no tava vārda vairs nebūs dzimums; no tava dieva nama Es izdeldēšu grieztas un lietas bildes; Es tev rakšu tavu kapu, jo tu esi viegls atrasts.
15 Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.
Redzi, uz kalniem prieka vēstnešu kājas, kas mieru sludina; svētī savus svētkus, ak Jūda, maksā savus solījumus; jo tas negantais pie tevis vairs nenāks, viņš ir pavisam izdeldēts.