< Nahumu 1 >
1 Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
Oracle sur Ninive. Livre de la Vision de Nahum d’Elqosch.
2 Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
C’est un Dieu jaloux et vengeur que Yahweh; vengeur est Yahweh et connaissant le courroux; Yahweh se venge de ses adversaires, et garde rancune à ses ennemis.
3 Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
Yahweh est patient et grand en force, et il n’accorde pas l’impunité. Yahweh marche dans la tempête et dans l’ouragan, et la nuée est la poussière de ses pieds.
4 Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
Il menace la mer et il la dessèche, et il fait tarir tous les fleuves. Basan et le Carmel sont flétris, flétrie est la végétation du Liban.
5 Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
Les montagnes tremblent devant lui, et les collines se fondent; la terre se soulève devant sa face, le monde et tous ceux qui l’habitent.
6 Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
Devant sa fureur qui subsistera, qui tiendra contre l’ardeur de sa colère? Son courroux se répand comme le feu, et les rochers se brisent devant lui.
7 Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
Yahweh est bon; il est un refuge au jour de la détresse, et il connaît ceux qui se confient en lui.
8 koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
Par un flot débordant il détruira entièrement ce lieu, et il poursuivra ses ennemis jusque dans les ténèbres.
9 Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
Quelles sont vos pensées sur Yahweh? Il consommera la ruine; la détresse ne surgira pas deux fois.
10 Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
Car, entrelacés comme des épines, et comme ivres de leur vin, ils seront consumés comme de la paille toute sèche.
11 Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
De toi est sorti celui qui médite le mal contre Yahweh, celui qui forme des desseins criminels.
12 Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
Ainsi parte Yahweh: Bien qu’ils soient intacts et nombreux, ils seront moissonnés et disparaîtront. Je t’ai humiliée et je ne t’humilierai plus.
13 Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
Et maintenant, ô Juda, je briserai son joug de dessus toi, et je romprai tes liens.
14 Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
Quant à toi, voici ce qu’a ordonné Yahweh: Il n’y aura plus de postérité de ton nom; je détruirai de la maison de ton Dieu les images taillées et celles de fonte; je prépare ton sépulcre, parce que tu as été léger.
15 Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.
Voici sur les montagnes les pieds d’un messager de bonnes nouvelles, qui annonce la paix. Célèbre tes fêtes, ô Juda, accomplis tes vœux! Car il ne passera plus chez toi; le méchant est entièrement détruit.