< Nahumu 1 >
1 Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
Břímě Ninive: Kniha vidění Nahuma Elkošského.
2 Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
Hospodin jest Bůh horlivý a mstitel, mstitel jestiť Hospodin, a zůřivý. Hospodin uvodí pomstu na protivníky své, a drží hněv proti nepřátelům svým.
3 Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
Hospodin dlouhočekající jest a velikomocný, však nikoli neospravedlňuje vinného. U vichru a bouři jest cesta Hospodinova, a oblak jest prach noh jeho.
4 Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
Když domlouvá moři, vysušuje je, i všecky řeky vysušuje; chřadne Bázan i Karmel, i květ Libánský chřadne.
5 Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
Hory se třesou před ním, a pahrbkové se rozplývají, země pak hoří před tváří jeho, i okršlek zemský a všickni, kteříž přebývají na něm.
6 Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
Před rozhněváním jeho kdo ostojí? A kdo se postaví proti prchlivosti hněvu jeho? Prchlivost jeho vylévá se jako oheň, a skály vyvracejí se před ním.
7 Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
Dobrýť jest Hospodin, silou jest v den ssoužení, a zná ty, kdož v něho doufají.
8 koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
Protož povodní prudkou konec učiní místu jeho, a nepřátely Boží stihati budou temnosti.
9 Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
Co myslíte proti Hospodinu? Onť konec učiní, nezdvihne druhé rány.
10 Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
Nebo rovně jako trní spleteni jsouce, a jako vínem opojeni, jako strniště suché docela sehlceni budou.
11 Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
Z tebeť vyšel ten, kterýž myslí proti Hospodinu zlé, rádce nešlechetný.
12 Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
Takto dí Hospodin: Byť se byli pokojně měli, byliť by tak v rozšíření zůstali aneb by toliko přemrštěni byli; i bylo by to pominulo, a netrápil bych jich více, tak jako jsem trápil.
13 Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
Nyní pak polámi jho jeho, aby neleželo na tobě, a to, čímž jsi svázán, roztrhám.
14 Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
Nebo přikázaní vydal proti tobě Hospodin, nebudeť rozsíváno ze jména tvého více; z domu Boha tvého vyhladím rytinu i slitinu, a když zlehčen budeš, způsobímť hrob.
15 Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.
Aj hle na horách těchto nohy potěšené věci zvěstujícího, ohlašujícího pokoj. Slaviž, o Judo, slavnosti své, plň sliby své. Neboť nepokusí se více ani mimo tebe choditi nešlechetný, docelať jest vyhlazen.