< Mika 7 >

1 Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
Woe to me, for I have become just like one who gleans the clusters of the vintage in autumn. There is no cluster of grapes to consume; my soul desired figs out of season.
2 Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
The holy ones pass away from the land, and there is no one righteous among men. All wait in ambush for blood; a man hunts his brother to death.
3 Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
The evil of their hands, they call good. The leader is demanding, and the judge is yielding, and the great is speaking the desire of his soul, and they have confused it.
4 Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
Whoever is best among them is like a thorny plant, and he who is righteous is like a thorny hedge. The day of your inspection, your visitation, arrives. Now will be their ruination.
5 Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
Do not be willing to believe a friend. And do not be willing to confide in a commander. From her, who sleeps in your bosom, keep the doors of your mouth closed.
6 Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
For the son acts with contempt for the father, and the daughter rises up against her mother, the daughter-in-law against her mother-in-law, and a man’s enemies are those of his own household.
7 Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
But I will look towards the Lord. I will wait for God, my Savior. My God will hear me.
8 Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
You, my enemy, should not rejoice over me because I have fallen. I will rise up, when I sit in darkness. The Lord is my light.
9 Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
I will carry the wrath of the Lord, because I have sinned against him, until he may judge my case and execute judgment for me. He will lead me into the light. I will behold his justice.
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
And my enemy will look, and she will be covered with confusion, she who says to me, “Where is the Lord your God?” My eyes will look upon her. Now she will be trampled underfoot like the mud of the streets.
11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
The day that your walls will be rebuilt, in that day the law will be far away.
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
In that day also, they will come towards you even from Assur, and even to the fortified cities, and from the fortified cities even to the river, and from sea to sea, and from mountain to mountain.
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
And the land will be in desolation, because of its inhabitants and because of the fruit of their intentions.
14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
With your rod, pasture your people, the flock of your inheritance, living alone in the narrow forest, in the midst of Carmel. They will graze in Bashan and Gilead, as in the ancient days.
15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
As in the days of your departure from the land of Egypt, I will reveal miracles to him.
16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
The nations will look, and they will be confounded at the strength of them all. They will place hand over mouth; their ears will be deaf.
17 Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
They will lick the dust like serpents, and, like the creeping things of the earth, they will be disturbed in their houses. They will dread the Lord our God, and they will fear you.
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
What God is like you, who takes away iniquity and passes over the sin of the remnant of your inheritance? No longer will he send forth his fury, because he is willing to be merciful.
19 Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
He will turn back and have mercy on us. He will put away our iniquities, and he will cast all our sins into the depths of the sea.
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.
You will give the truth to Jacob, mercy to Abraham, which you swore to our fathers from the ancient days.

< Mika 7 >