< Habakuku 3 >

1 Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.
A Prayer of Habakkuk the Prophet on Behalf of Those Who Are Ignorant.
2 Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu; Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa. Muzichitenso masiku athu ano, masiku athu ano zidziwike; mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
Lord, I heard what has been said about you, and I was afraid. Lord, your work, in the midst of years, revive it. In the midst of years, you will make it known. When you have become angry, you will remember mercy.
3 Mulungu anabwera kuchokera ku Temani, Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani. (Sela) Ulemerero wake unaphimba mlengalenga ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
God will come from the south, and the Holy One from mount Pharan. His glory has covered the heavens, and the earth is full of his praise.
4 Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa; kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake, mʼmene anabisamo mphamvu zake.
His brightness shall be like the light; horns are in his hands. There, his strength has been hidden.
5 Patsogolo pake pankagwa mliri; nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
Death will go forth before his face. And the devil shall depart before his feet.
6 Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi; anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera. Mapiri okhazikika anagumuka ndipo zitunda zakalekale zinatitimira. Njira zake ndi zachikhalire.
He stood, and measured the earth. He looked, and dissolved the Gentiles. And the mountains of ages past have been shattered. The hills of the world became curved by the journeys of his eternity.
7 Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto, mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.
I saw the tents of Ethiopia for their iniquity; the tent-skins of the land of Midian will be thrown into confusion.
8 Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje? Kodi munakalipira timitsinje? Kodi munapsera mtima nyanja pamene munakwera pa akavalo anu ndiponso magaleta anu achipulumutso?
Could you have been angry with the rivers, Lord? Or was your fury within the rivers, or your indignation in the sea? He will ascend upon your horses, and your four-horse chariots are salvation.
9 Munasolola uta wanu mʼchimake, munayitanitsa mivi yambiri. (Sela) Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
Being stirred up, you will take up your bow, the oaths you have spoken to the tribes. You will split apart the Rivers of the earth.
10 mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka. Madzi amphamvu anasefukira; nyanja yozama inakokoma ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.
They saw you, and the mountains grieved. The great body of waters crossed over. The abyss uttered its voice. The pinnacle lifted up its hands.
11 Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga, pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo, pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
The sun and the moon have stood firm in their dwelling place; with the light of your arrows, they shall go forth in the splendor of your flashing spear.
12 Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali, ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
With a roar, you will trample the earth. In your fury, you will cause the nations to be stupefied.
13 Munapita kukalanditsa anthu anu, kukapulumutsa wodzozedwa wanu. Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa, munawononga anthu ake onse. (Sela)
You have gone forth for the salvation of your people, for salvation with your Christ. You struck the head of the house of the impious. You have laid bare his foundation all the way to the neck.
14 Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa, ankasangalala ngati kuti akudzawononga osauka amene akubisala.
You have cursed his scepters, the head of his warriors, those who approached like a whirlwind so as to scatter me. Their exultation was like one who devours the poor in secret.
15 Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu, kuvundula madzi amphamvu.
You made a way in the sea for your horses, in the mud of great waters.
16 Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri, milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo; mafupa anga anaguluka, ndipo mawondo anga anawombana. Komabe ndikuyembekezera mofatsa, tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
I heard, and my stomach became troubled. My lips trembled at the voice. Let decay enter into my bones and gush forth from within me. Then I may rest in the day of tribulation, so that I may ascend to our people well-prepared.
17 Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa, ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa. Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso, ndipo mʼminda musatuluke kanthu. Ngakhale nkhosa ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
For the fig tree will not flower, and there will be no bud on the vines. The labor of the olive tree will be misleading, and the farmland will produce no food. The sheep will be cut off from the sheepfold, and there will be no herd at the manger.
18 komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
But I will rejoice in the Lord; and I will exult in God my Jesus.
19 Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga; amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi, amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.
The Lord God is my strength. And he will set my feet like those of the stag. And he, the victor, will lead me beyond my high places while singing psalms.

< Habakuku 3 >