< Mateyu 14 >
1 Pa nthawi imeneyo Mfumu Herode anamva za mbiri ya Yesu.
tadānīṁ rājā herod yīśo ryaśaḥ śrutvā nijadāseyān jagād,
2 Ndipo iye anati kwa antchito ake, “Uyu ndi Yohane Mʼbatizi; iye wauka kwa akufa! Ichi ndi chifukwa chake mphamvu zodabwitsa zikugwira ntchito mwa iye.”
eṣa majjayitā yohan, pramitebhayastasyotthānāt tenetthamadbhutaṁ karmma prakāśyate|
3 Pakuti Herode anamugwira Yohane ndi kumumanga ndipo anamuyika mʼndende chifukwa cha Herodia mkazi wa mʼbale wake Filipo.
purā herod nijabhrātu: philipo jāyāyā herodīyāyā anurodhād yohanaṁ dhārayitvā baddhā kārāyāṁ sthāpitavān|
4 Chifukwa Yohane anakhala akunena kwa iye kuti, “Sichololedwa kwa inu kutenga mkaziyo.”
yato yohan uktavān, etsayāḥ saṁgraho bhavato nocitaḥ|
5 Herode anafuna kupha Yohane koma iye anaopa anthu chifukwa anamuyesa iye mneneri.
tasmāt nṛpatistaṁ hantumicchannapi lokebhyo vibhayāñcakāra; yataḥ sarvve yohanaṁ bhaviṣyadvādinaṁ menire|
6 Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwa Herode, mwana wamkazi wa Herodia anavina pamaso pa anthu ndipo anasangalatsa kwambiri.
kintu herodo janmāhīyamaha upasthite herodīyāyā duhitā teṣāṁ samakṣaṁ nṛtitvā herodamaprīṇyat|
7 Kotero Herode analonjeza ndi lumbiro kumupatsa chilichonse chimene mwanayo angamupemphe.
tasmāt bhūpatiḥ śapathaṁ kurvvan iti pratyajñāsīt, tvayā yad yācyate, tadevāhaṁ dāsyāmi|
8 Ndipo atamupangira amayi ake anati, “Mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
sā kumārī svīyamātuḥ śikṣāṁ labdhā babhāṣe, majjayituryohana uttamāṅgaṁ bhājane samānīya mahyaṁ viśrāṇaya|
9 Mfumuyo inamva chisoni koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo amene anali pa phwando lake analamulira kuti chofuna chake chipatsidwe;
tato rājā śuśoca, kintu bhojanāyopaviśatāṁ saṅgināṁ svakṛtaśapathasya cānurodhāt tat pradātuma ādideśa|
10 ndipo anakadula mutu wa Yohane mʼndende.
paścāt kārāṁ prati naraṁ prahitya yohana uttamāṅgaṁ chittvā
11 Mutu wake anawubweretsa mʼmbale ndi kumupatsa mtsikanayo amene anawutengera kwa amayi ake.
tat bhājana ānāyya tasyai kumāryyai vyaśrāṇayat, tataḥ sā svajananyāḥ samīpaṁ tannināya|
12 Ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo wake ndi kukawuyika mʼmanda. Pomwepo iwo anapita kukamuwuza Yesu.
paścāt yohanaḥ śiṣyā āgatya kāyaṁ nītvā śmaśāne sthāpayāmāsustato yīśoḥ sannidhiṁ vrajitvā tadvārttāṁ babhāṣire|
13 Yesu atamva zimene zinachitika, anachoka pa bwato mwachinsinsi kupita kumalo a yekha. Magulu a anthu atamva izi anamutsatira Iye poyenda pansi kuchokera ku mizinda.
anantaraṁ yīśuriti niśabhya nāvā nirjanasthānam ekākī gatavān, paścāt mānavāstat śrutvā nānānagarebhya āgatya padaistatpaścād īyuḥ|
14 Yesu atafika ku mtunda, ndi kuona gulu lalikulu la anthu, Iye anamva nawo chifundo ndipo anachiritsa odwala awo.
tadānīṁ yīśu rbahirāgatya mahāntaṁ jananivahaṁ nirīkṣya teṣu kāruṇikaḥ man teṣāṁ pīḍitajanān nirāmayān cakāra|
15 Kutayamba mdima, ophunzira anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kutchire ndipo kwayamba kale kuda. Awuzeni anthu azipita kuti afike ku midzi ndi kukadzigulira zakudya.”
tataḥ paraṁ sandhyāyāṁ śiṣyāstadantikamāgatya kathayāñcakruḥ, idaṁ nirjanasthānaṁ velāpyavasannā; tasmāt manujān svasvagrāmaṁ gantuṁ svārthaṁ bhakṣyāṇi kretuñca bhavān tān visṛjatu|
16 Yesu anawayankha kuti, “Sikofunika kuti azipita. Inuyo muwapatse kanthu kuti adye.”
kintu yīśustānavādīt, teṣāṁ gamane prayojanaṁ nāsti, yūyameva tān bhojayata|
17 Iwo anayankha kuti, “Tili ndi malofu asanu okha a buledi ndi nsomba ziwiri.”
tadā te pratyavadan, asmākamatra pūpapañcakaṁ mīnadvayañcāste|
18 Koma Iye anati, “Bweretsani kwa Ine.”
tadānīṁ tenoktaṁ tāni madantikamānayata|
19 Analamula anthu kuti akhale pansi pa udzu ndipo anatenga buledi musanu ndi nsomba ziwiri nayangʼana kumwamba, nayamika nagawa bulediyo. Kenaka anapereka bulediyo kwa ophunzira ake ndipo ophunzirawo anagawira anthu.
anantaraṁ sa manujān yavasoparyyupaveṣṭum ājñāpayāmāsa; apara tat pūpapañcakaṁ mīnadvayañca gṛhlan svargaṁ prati nirīkṣyeśvarīyaguṇān anūdya bhaṁktvā śiṣyebhyo dattavān, śiṣyāśca lokebhyo daduḥ|
20 Onse anadya nakhuta ndipo ophunzira anatola zotsalira ndi kudzaza madengu khumi ndi awiri.
tataḥ sarvve bhuktvā paritṛptavantaḥ, tatastadavaśiṣṭabhakṣyaiḥ pūrṇān dvādaśaḍalakān gṛhītavantaḥ|
21 Chiwerengero cha amene anadya kupatulako amayi ndi ana chinali pafupifupi amuna 5,000.
te bhoktāraḥ strīrbālakāṁśca vihāya prāyeṇa pañca sahasrāṇi pumāṁsa āsan|
22 Nthawi yomweyo anawawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita kutsidya lina pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita kwawo.
tadanantaraṁ yīśu rlokānāṁ visarjanakāle śiṣyān taraṇimāroḍhuṁ svāgre pāraṁ yātuñca gāḍhamādiṣṭavān|
23 Atatha kuwawuza kuti azipita kwawo, Iye anakwera ku phiri yekha kukapemphera. Pamene kumada anali kumeneko yekha.
tato lokeṣu visṛṣṭeṣu sa vivikte prārthayituṁ girimekaṁ gatvā sandhyāṁ yāvat tatraikākī sthitavān|
24 Pamenepo nʼkuti bwato litapita patali pangʼono kuchokera ku mtunda ndipo linavutika ndi mafunde chifukwa mphepo inkawomba mokumana nalo.
kintu tadānīṁ sammukhavātatvāt saritpate rmadhye taraṅgaistaraṇirdolāyamānābhavat|
25 Pa ora lachinayi usiku, Yesu anabwera kwa iwo akuyendabe pa nyanja.
tadā sa yāminyāścaturthaprahare padbhyāṁ vrajan teṣāmantikaṁ gatavān|
26 Ophunzira atamuona akuyenda pa nyanja, anaopa nati, “Ndi mzukwa!” Ndipo analira chifukwa cha mantha.
kintu śiṣyāstaṁ sāgaropari vrajantaṁ vilokya samudvignā jagaduḥ, eṣa bhūta iti śaṅkamānā uccaiḥ śabdāyāñcakrire ca|
27 Koma Yesu nthawi yomweyo anawawuza kuti, “Limbani mtima! Ndine, musaope.”
tadaiva yīśustānavadat, susthirā bhavata, mā bhaiṣṭa, eṣo'ham|
28 Petro anayankha nati, “Ambuye ngati ndinu, mundiwuze ndibwere kuli inuko pa madzipo.”
tataḥ pitara ityuktavān, he prabho, yadi bhavāneva, tarhi māṁ bhavatsamīpaṁ yātumājñāpayatu|
29 Iye anati, “Bwera.” Pamenepo Petro anatuluka mʼbwato ndipo anayenda pa madzi kupita kwa Yesu.
tataḥ tenādiṣṭaḥ pitarastaraṇito'varuhya yīśerantikaṁ prāptuṁ toyopari vavrāja|
30 Koma ataona mphepo, iye anachita mantha ndipo anayamba kumira, nafuwula nati, “Ambuye ndipulumutseni!”
kintu pracaṇḍaṁ pavanaṁ vilokya bhayāt toye maṁktum ārebhe, tasmād uccaiḥ śabdāyamānaḥ kathitavān, he prabho, māmavatu|
31 Ndipo mofulumira Yesu anatambasula dzanja lake namugwira iye, nati, “Iwe wachikhulupiriro chochepa, bwanji unakayika?”
yīśustatkṣaṇāt karaṁ prasāryya taṁ dharan uktavān, ha stokapratyayin tvaṁ kutaḥ samaśethāḥ?
32 Ndipo atalowa mʼbwato mphepo inaleka.
anantaraṁ tayostaraṇimārūḍhayoḥ pavano nivavṛte|
33 Pamenepo amene anali mʼbwato anamulambira Iye, nati, “Zoonadi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu.”
tadānīṁ ye taraṇyāmāsan, ta āgatya taṁ praṇabhya kathitavantaḥ, yathārthastvameveśvarasutaḥ|
34 Atawoloka, anafika ku Genesareti.
anantaraṁ pāraṁ prāpya te gineṣarannāmakaṁ nagaramupatasthuḥ,
35 Anthu akumeneko atamuzindikira Yesu, iwo anatumiza mawu kwa onse ozungulira deralo. Anthu anabwera ndi odwala awo onse kwa Iye.
tadā tatratyā janā yīśuṁ paricīya taddeśsya caturdiśo vārttāṁ prahitya yatra yāvantaḥ pīḍitā āsan, tāvataeva tadantikamānayāmāsuḥ|
36 Ndipo anamupempha alole kuti akhudze mphonje ya mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachiritsidwa.
aparaṁ tadīyavasanasya granthimātraṁ spraṣṭuṁ vinīya yāvanto janāstat sparśaṁ cakrire, te sarvvaeva nirāmayā babhūvuḥ|