< Mateyu 24 >
1 Yesu anatuluka mʼNyumba ya Mulungu ndipo akuchoka ophunzira ake anadza kwa Iye ndi kumuonetsa mamangidwe a Nyumbayo.
anantaraṁ yīśu ryadā mandirād bahi rgacchati, tadānīṁ śiṣyāstaṁ mandiranirmmāṇaṁ darśayitumāgatāḥ|
2 Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuona zinthu zonsezi? Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti palibe mwala pano umene udzasiyidwe pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
tato yīśustānuvāca, yūyaṁ kimetāni na paśyatha? yuṣmānahaṁ satyaṁ vadāmi, etannicayanasya pāṣāṇaikamapyanyapāṣāṇepari na sthāsyati sarvvāṇi bhūmisāt kāriṣyante|
3 Pamene Yesu anakhala pansi pa phiri la Olivi, ophunzira ake anabwera kwa Iye mwamseri nati, “Tiwuzeni, kodi izi zidzachitika liti, ndipo chizindikiro cha kubwera kwanu ndi zizindikiro za kutha kwa dziko zidzakhala chiyani?” (aiōn )
anantaraṁ tasmin jaitunaparvvatopari samupaviṣṭe śiṣyāstasya samīpamāgatya guptaṁ papracchuḥ, etā ghaṭanāḥ kadā bhaviṣyanti? bhavata āgamanasya yugāntasya ca kiṁ lakṣma? tadasmān vadatu| (aiōn )
4 Yesu anayankha kuti, “Onetsetsani kuti wina asakunyengeni.
tadānīṁ yīśustānavocat, avadhadvvaṁ, kopi yuṣmān na bhramayet|
5 Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati, ‘Ndine Khristu,’ ndipo adzanyenga ambiri.
bahavo mama nāma gṛhlanta āgamiṣyanti, khrīṣṭo'hameveti vācaṁ vadanto bahūn bhramayiṣyanti|
6 Mudzamva za nkhondo ndi mbiri za nkhondo, koma onetsetsani kuti musadzidzimuke nazo. Zotere ziyenera kuchitika, koma chimaliziro sichinafike.
yūyañca saṁgrāmasya raṇasya cāḍambaraṁ śroṣyatha, avadhadvvaṁ tena cañcalā mā bhavata, etānyavaśyaṁ ghaṭiṣyante, kintu tadā yugānto nahi|
7 Mtundu ndi mtundu udzawukirana, ndipo ufumu ndi ufumu udzawukirana. Kudzakhala njala ndi zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana.
aparaṁ deśasya vipakṣo deśo rājyasya vipakṣo rājyaṁ bhaviṣyati, sthāne sthāne ca durbhikṣaṁ mahāmārī bhūkampaśca bhaviṣyanti,
8 Zonsezi ndi chiyambi chabe cha zowawa.
etāni duḥkhopakramāḥ|
9 “Pamenepo adzakuperekani kuti mukazunzidwe ndi kuphedwa, ndipo mitundu yonse idzakudani chifukwa cha Ine.
tadānīṁ lokā duḥkhaṁ bhojayituṁ yuṣmān parakareṣu samarpayiṣyanti haniṣyanti ca, tathā mama nāmakāraṇād yūyaṁ sarvvadeśīyamanujānāṁ samīpe ghṛṇārhā bhaviṣyatha|
10 Pa nthawi imeneyo ambiri adzasiya chikhulupiriro ndipo adzadana ndi kuperekana wina ndi mnzake,
bahuṣu vighnaṁ prāptavatsu parasparam ṛtīyāṁ kṛtavatsu ca eko'paraṁ parakareṣu samarpayiṣyati|
11 ndipo aneneri onama ambiri adzaoneka ndi kunyenga anthu ambiri.
tathā bahavo mṛṣābhaviṣyadvādina upasthāya bahūn bhramayiṣyanti|
12 Chifukwa cha kuchuluka kwa zoyipa, chikondi cha ambiri chidzazirala,
duṣkarmmaṇāṁ bāhulyāñca bahūnāṁ prema śītalaṁ bhaviṣyati|
13 koma wopirira kufikira chimaliziro adzapulumuka.
kintu yaḥ kaścit śeṣaṁ yāvad dhairyyamāśrayate, saeva paritrāyiṣyate|
14 Ndipo uthenga wa ufumu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi ngati umboni kwa mitundu yonse, ndipo pomwepo chimaliziro chidzafika.”
aparaṁ sarvvadeśīyalokān pratimākṣī bhavituṁ rājasya śubhasamācāraḥ sarvvajagati pracāriṣyate, etādṛśi sati yugānta upasthāsyati|
15 “Tsono mukadzaona chinthu chonyansa chosakaza chitayima pamalo oyera chimene anayankhula mneneri Danieli, owerengayo azindikire.
ato yat sarvvanāśakṛdghṛṇārhaṁ vastu dāniyelbhaviṣyadvadinā proktaṁ tad yadā puṇyasthāne sthāpitaṁ drakṣyatha, (yaḥ paṭhati, sa budhyatāṁ)
16 Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire ku mapiri.
tadānīṁ ye yihūdīyadeśe tiṣṭhanti, te parvvateṣu palāyantāṁ|
17 Yemwe ali pa denga la nyumba yake asatsike kukatulutsa chinthu chilichonse mʼnyumba.
yaḥ kaścid gṛhapṛṣṭhe tiṣṭhati, sa gṛhāt kimapi vastvānetum adhe nāvarohet|
18 Yemwe ali ku munda asapite kukatenga mkanjo wake.
yaśca kṣetre tiṣṭhati, sopi vastramānetuṁ parāvṛtya na yāyāt|
19 Kudzakhala koopsa kwambiri masiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi kwa oyamwitsa!
tadānīṁ garbhiṇīstanyapāyayitrīṇāṁ durgati rbhaviṣyati|
20 Pempherani kuti kuthawa kwanu kusadzachitike nthawi yozizira kapena pa Sabata.
ato yaṣmākaṁ palāyanaṁ śītakāle viśrāmavāre vā yanna bhavet, tadarthaṁ prārthayadhvam|
21 Popeza kudzakhala masautso aakulu, omwe safanana ndi ena ali onse chiyambireni cha dziko lapansi mpaka lero lino ndipo sadzafanananso ndi ena.
ā jagadārambhād etatkālaparyyanantaṁ yādṛśaḥ kadāpi nābhavat na ca bhaviṣyati tādṛśo mahākleśastadānīm upasthāsyati|
22 Ngati masiku amenewo sakanafupikitsidwa, palibe mmodzi akanapulumuka, koma chifukwa cha osankhidwawo masiku amenewo adzafupikitsidwa.
tasya kleśasya samayo yadi hsvo na kriyeta, tarhi kasyāpi prāṇino rakṣaṇaṁ bhavituṁ na śaknuyāt, kintu manonītamanujānāṁ kṛte sa kālo hsvīkariṣyate|
23 Pa nthawi imeneyo ngati wina adzati kwa inu, ‘Onani, Khristu ali pano!’ Kapena, ‘Uyo ali ukoyo!’ Musakhulupirire.
aparañca paśyata, khrīṣṭo'tra vidyate, vā tatra vidyate, tadānīṁ yadī kaścid yuṣmāna iti vākyaṁ vadati, tathāpi tat na pratīt|
24 Chifukwa akhristu onama ndi aneneri onama adzaoneka ndipo adzachita zizindikiro zazikulu ndi zodabwitsa kuti akanyenge ngakhale osankhidwawo ngati kukanakhala kotheka kutero.
yato bhāktakhrīṣṭā bhāktabhaviṣyadvādinaśca upasthāya yāni mahanti lakṣmāṇi citrakarmmāṇi ca prakāśayiṣyanti, tai ryadi sambhavet tarhi manonītamānavā api bhrāmiṣyante|
25 Onani, ndakuwuzani izi nthawi isanafike.
paśyata, ghaṭanātaḥ pūrvvaṁ yuṣmān vārttām avādiṣam|
26 “Ndiye ngati wina akuwuzani inu kuti, ‘Uyo ali ku chipululu,’ inu musapiteko; kapena akati, ‘Uyu ali kuno mʼchipinda chamʼkati,’ musakhulupirire.
ataḥ paśyata, sa prāntare vidyata iti vākye kenacit kathitepi bahi rmā gacchata, vā paśyata, sontaḥpure vidyate, etadvākya uktepi mā pratīta|
27 Monga momwe mphenzi ingʼanima kuchokera kummawa kupita kumadzulo, momwemonso kudzakhala kubwera kwa Mwana wa Munthu.
yato yathā vidyut pūrvvadiśo nirgatya paścimadiśaṁ yāvat prakāśate, tathā mānuṣaputrasyāpyāgamanaṁ bhaviṣyati|
28 Kulikonse kuli chinthu cha kufa, makwangwala adzasonkhanako.
yatra śavastiṣṭhati, tatreva gṛdhrā milanti|
29 “Akadzangotha mavuto a masiku amenewo, “‘dzuwa lidzadetsedwa, ndipo mwezi sudzawala; nyenyezi zidzagwa kuchokera kumwamba, ndipo mphamvu za mmwamba zidzagwedezeka.’
aparaṁ tasya kleśasamayasyāvyavahitaparatra sūryyasya tejo lopsyate, candramā jyosnāṁ na kariṣyati, nabhaso nakṣatrāṇi patiṣyanti, gagaṇīyā grahāśca vicaliṣyanti|
30 “Pa nthawi imeneyo chizindikiro cha Mwana wa Munthu chidzaoneka mlengalenga, ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzalira. Idzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
tadānīm ākāśamadhye manujasutasya lakṣma darśiṣyate, tato nijaparākrameṇa mahātejasā ca meghārūḍhaṁ manujasutaṁ nabhasāgacchantaṁ vilokya pṛthivyāḥ sarvvavaṁśīyā vilapiṣyanti|
31 Ndipo adzatuma angelo ake, ndi kulira kwa lipenga kwakukulu, nadzasonkhanitsa osankhidwa ake kuchokera ku mphepo zinayi, ndi kuchokera kumathero a thambo kufika mbali ina.
tadānīṁ sa mahāśabdāyamānatūryyā vādakān nijadūtān praheṣyati, te vyomna ekasīmāto'parasīmāṁ yāvat caturdiśastasya manonītajanān ānīya melayiṣyanti|
32 “Tsopano kuchokera ku mtengo wamkuyu phunzirani ichi: Pamene uyamba kuphukira, masamba ake akatuluka, mumadziwa kuti dzinja layandikira.
uḍumbarapādapasya dṛṣṭāntaṁ śikṣadhvaṁ; yadā tasya navīnāḥ śākhā jāyante, pallavādiśca nirgacchati, tadā nidāghakālaḥ savidho bhavatīti yūyaṁ jānītha;
33 Momwemonso, pamene mudzaona zinthu zonsezi mudzadziwe kuti ali pafupi pa khomo penipeni.
tadvad etā ghaṭanā dṛṣṭvā sa samayo dvāra upāsthād iti jānīta|
34 Zoonadi, ndikuwuzani kuti mʼbado uwu sudzatha mpaka zinthu zonse zitachitika.
yuṣmānahaṁ tathyaṁ vadāmi, idānīntanajanānāṁ gamanāt pūrvvameva tāni sarvvāṇi ghaṭiṣyante|
35 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
nabhomedinyo rluptayorapi mama vāk kadāpi na lopsyate|
36 “Palibe amene adziwa za tsikulo kapena nthawi, angakhale angelo akumwamba, angakhale Mwana, koma Atate okha.
aparaṁ mama tātaṁ vinā mānuṣaḥ svargastho dūto vā kopi taddinaṁ taddaṇḍañca na jñāpayati|
37 Monga momwe zinalili nthawi ya Nowa, momwemonso zidzatero pobwera kwa Mwana wa Munthu.
aparaṁ nohe vidyamāne yādṛśamabhavat tādṛśaṁ manujasutasyāgamanakālepi bhaviṣyati|
38 Pakuti masiku amenewo chisanafike chigumula, anthu amadya ndi kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa, mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo;
phalato jalāplāvanāt pūrvvaṁ yaddinaṁ yāvat nohaḥ potaṁ nārohat, tāvatkālaṁ yathā manuṣyā bhojane pāne vivahane vivāhane ca pravṛttā āsan;
39 ndipo sanadziwe za chimene chikanachitika mpaka pamene chigumula chinafika ndi kuwamiza onse. Umu ndi mmene zidzakhalira pobwera kwa Mwana wa Munthu.
aparam āplāvitoyamāgatya yāvat sakalamanujān plāvayitvā nānayat, tāvat te yathā na vidāmāsuḥ, tathā manujasutāgamanepi bhaviṣyati|
40 Amuna awiri adzakhala mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
tadā kṣetrasthitayordvayoreko dhāriṣyate, aparastyājiṣyate|
41 Amayi awiri adzakhala akusinja pa mtondo; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
tathā peṣaṇyā piṁṣatyorubhayo ryoṣitorekā dhāriṣyate'parā tyājiṣyate|
42 “Chifukwa chake yangʼanirani, popeza simudziwa tsiku lanji limene Ambuye anu adzabwera.
yuṣmākaṁ prabhuḥ kasmin daṇḍa āgamiṣyati, tad yuṣmābhi rnāvagamyate, tasmāt jāgrataḥ santastiṣṭhata|
43 Koma zindikirani ichi: Ngati mwini nyumba akanadziwa nthawi yanji ya usiku imene mbala imabwera, sakanagona ndipo sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
kutra yāme stena āgamiṣyatīti ced gṛhastho jñātum aśakṣyat, tarhi jāgaritvā taṁ sandhiṁ karttitum avārayiṣyat tad jānīta|
44 Inunso tsono muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa nthawi imene inu simukumuyembekezera.
yuṣmābhiravadhīyatāṁ, yato yuṣmābhi ryatra na budhyate, tatraiva daṇḍe manujasuta āyāsyati|
45 “Kodi wantchito wokhulupirika ndi wanzeru amene ambuye ake anamuyika kukhala woyangʼanira antchito a mʼnyumba kuti awapatse chakudya chawo pa nthawi yake ndani?
prabhu rnijaparivārān yathākālaṁ bhojayituṁ yaṁ dāsam adhyakṣīkṛtya sthāpayati, tādṛśo viśvāsyo dhīmān dāsaḥ kaḥ?
46 Chidzakhala chabwino kwa wantchitoyo ngati mbuye wake pofika adzamupeza akuchita zimenezi.
prabhurāgatya yaṁ dāsaṁ tathācarantaṁ vīkṣate, saeva dhanyaḥ|
47 Zoonadi, ndikuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
yuṣmānahaṁ satyaṁ vadāmi, sa taṁ nijasarvvasvasyādhipaṁ kariṣyati|
48 Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo ndi woyipa, nati kwa iye yekha, ‘Mbuye wanga akuchedwa kubwera,’
kintu prabhurāgantuṁ vilambata iti manasi cintayitvā yo duṣṭo dāso
49 nayamba kumenya antchito anzake, nadya ndi kumwa ndi zidakwa.
'paradāsān praharttuṁ mattānāṁ saṅge bhoktuṁ pātuñca pravarttate,
50 Mbuye wa wantchitoyo adzabwera pa tsiku limene iye samamuyembekezera ndi pa nthawi imene iye sakuyidziwa.
sa dāso yadā nāpekṣate, yañca daṇḍaṁ na jānāti, tatkālaeva tatprabhurupasthāsyati|
51 Adzamulanga koopsa ndipo adzamuyika kokhala anthu achiphamaso, kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
tadā taṁ daṇḍayitvā yatra sthāne rodanaṁ dantagharṣaṇañcāsāte, tatra kapaṭibhiḥ sākaṁ taddaśāṁ nirūpayiṣyati|