< Marko 6 >
1 Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake.
Then Jesus left that place and went to his hometown, and his disciples followed him.
2 Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa. Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa!
When the Sabbath came, he began to teach in the synagogue, and many who heard him were astonished, saying, “Where did this man get these things? And what is this wisdom that has been given to him, that such miracles are done by his hands?
3 Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.
Is this not the carpenter, the son of Mary, and the brother of James, Joses, Judas, and Simon? Are not his sisters here with us?” And they took offense at him.
4 Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.”
Then Jesus said to them, “A prophet is not without honor except in his hometown, among his relatives, and in his own household.”
5 Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa.
So he could do no miracles there, except that he laid his hands on a few sick people and healed them.
6 Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo. Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa.
And he was amazed at their unbelief. Then Jesus went around among the villages teaching.
7 Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.
He summoned the twelve and began to send them out two by two, giving them authority over unclean spirits.
8 Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama.
He instructed them to take nothing for their journey except a staff—no knapsack, no bread, and no copper money in their belts.
9 Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera.
He told them to wear sandals but not an extra tunic.
10 Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo.
He also said to them, “Whenever you enter a house, stay there until you leave that place.
11 Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”
If anyone will not receive you or listen to you, shake the dust off your feet as you leave that place, as a testimony against them. Truly I say to you, it will be more tolerable for Sodom and Gomorrah on the day of judgment than for that city.”
12 Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima.
So they went out and preached that people should repent.
13 Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.
They also cast out many demons and anointed with oil many who were sick and healed them.
14 Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”
Now King Herod heard about this, for Jesus' name had become known, and he said, “John the Baptist has been raised from the dead, and that is why these mighty powers are at work in him.”
15 Ena anati, “Iye ndi Eliya.” Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”
Others said, “He is Elijah.” And others said, “He is a prophet, like one of the prophets of old.”
16 Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”
But when Herod heard this, he said, “This is John, whom I beheaded; he has been raised from the dead.”
17 Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira.
For Herod himself had sent men to arrest John and chain him in prison on account of Herodias, his brother Philip's wife, whom Herod had married.
18 Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.”
For John had been saying to Herod, “It is not lawful for yoʋ to have yoʋr brother's wife.”
19 Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero,
So Herodias held a grudge against John and wanted to kill him, but she was not able to do so.
20 chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.
For Herod feared John, knowing that he was a righteous and holy man, and he protected him. When Herod listened to John, he would listen to him gladly and do many things.
21 Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya.
But an opportune day came. On his birthday Herod prepared a banquet for his nobles, military commanders, and the prominent men of Galilee.
22 Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo. Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.”
When the daughter of Herodias came in and danced, she pleased Herod and his guests. So the king said to the girl, “Ask me for whatever yoʋ wish, and I will give it to yoʋ.”
23 Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”
He swore to her, “Whatever yoʋ ask me, I will give to yoʋ, up to half my kingdom.”
24 Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?” Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”
So she went out and said to her mother, “What should I ask for?” Her mother said, “The head of John the Baptist.”
25 Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
Immediately the girl came in with haste to the king and made her request, saying, “I want yoʋ to give me at once the head of John the Baptist on a platter.”
26 Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza.
Although the king was very sad, because of his oaths and his guests, he did not want to reject her.
27 Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende,
So the king immediately sent an executioner and commanded that John's head be brought back.
28 nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake.
The executioner then went and beheaded John in the prison, brought his head on a platter, and gave it to the girl. And the girl gave it to her mother.
29 Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.
When John's disciples heard about it, they came and took his body and laid it in a tomb.
30 Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa.
Meanwhile, the apostles gathered around Jesus and told him about all they had done and taught.
31 Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”
Then he said to them, “Come away by yourselves to a desolate place and rest for a little while.” For many people were coming and going, and Jesus and his apostles did not even have an opportunity to eat.
32 Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha.
So they went away to a desolate place in the boat by themselves.
33 Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika.
Now many saw them going away and recognized Jesus. They ran together on foot from all the towns, got there ahead of them, and then gathered around him.
34 Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
When Jesus went ashore and saw a large crowd, he was moved with compassion for them, because they were like sheep without a shepherd. So he began to teach them many things.
35 Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo.
When the hour was already quite late, his disciples came to him and said, “This place is desolate, and the hour is now late.
36 Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
Send the people away so that they can go into the surrounding countryside and villages and buy themselves some bread, for they have nothing to eat.”
37 Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.” Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
But Jesus answered them, “You give them something to eat.” They said to him, “Are we to go and buy two hundred denarii worth of bread and give it to them to eat?”
38 Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.” Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
He said to them, “How many loaves do you have? Go and see.” When they found out, they said, “Five, and two fish.”
39 Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira.
Then he directed them to have all the people sit down in groups on the green grass.
40 Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu.
So they sat down in groups of hundreds and fifties.
41 Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse.
Then he took the five loaves and the two fish, and looking up to heaven, he said the blessing. He broke the loaves and gave them to his disciples to set before the people, and he divided the two fish among them all.
42 Onse anadya ndipo anakhuta,
They all ate and were filled,
43 ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri.
and the disciples picked up twelve baskets full of the broken pieces and of the fish.
44 Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
Now those who had eaten the loaves were five thousand men.
45 Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita.
Immediately Jesus compelled his disciples to get into the boat and go ahead of him to the other side of the sea, to Bethsaida, while he sent the crowd away.
46 Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.
After taking leave of them, he went to the mountain to pray.
47 Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda.
When evening came, the boat was in the middle of the sea, and he was alone on the land.
48 Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira,
He saw the disciples straining as they rowed, for the wind was against them. About the fourth watch of the night he came to them, walking on the sea, and intended to pass them by.
49 koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula,
But when they saw him walking on the sea, they thought it was a ghost and cried out.
50 pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha. Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.”
For they all saw him and were terrified. But Jesus immediately said to them, “Take courage! It is I; do not be afraid.”
51 Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri,
Then he got into the boat with them, and the wind ceased. And they were utterly and completely amazed and in awe;
52 popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.
for they did not understand the significance of what had happened with the loaves, because their hearts were hardened.
53 Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko.
When they had crossed the sea, they came to the land of Gennesaret and moored the boat.
54 Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu.
When they got out of the boat, people immediately recognized Jesus.
55 Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye.
So the people ran around throughout the entire surrounding region and began to carry the sick on mats to wherever they heard he was.
56 Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.
And wherever he went, to villages, cities, or the countryside, they would lay the sick in the marketplaces and beg him to let the sick touch even the fringe of his garment. And all who touched it were healed.