< Marko 11 >

1 Atayandikira ku Yerusalemu, anafika ku Betifage ndi Betaniya ku phiri la Olivi. Yesu anatuma awiri a ophunzira ake
Lorsqu'ils approchèrent de Jérusalem, de Bethsphage et de Béthanie, au mont des Oliviers, il envoya deux de ses disciples
2 nati kwa iwo, “Pitani ku mudzi uli patsogolo panu, ndipo mukamakalowa, mukapeza mwana wabulu atamangiriridwa pamenepo, amene wina aliyense sanakwerepo. Kamumasuleni ndi kubwera naye kuno.
et leur dit: « Allez au village qui est en face de vous. Dès que vous y serez entrés, vous trouverez un jeune âne attaché, sur lequel personne ne s'est assis. Détachez-le et amenez-le.
3 Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Mukuchita zimenezi chifukwa chiyani?’ Kamuwuzeni kuti, ‘Ambuye akumufuna ndipo akamutumiza kuno msanga.’”
Si quelqu'un vous demande: « Pourquoi faites-vous cela? », dites: « Le Seigneur a besoin de lui; et aussitôt il le renverra ici. »
4 Anapita ndipo anakapeza mwana wabulu ali kunja mu msewu waukulu atamumangirira pa chipata. Pamene anamumasula,
Ils s'en allèrent, et trouvèrent un jeune âne attaché à la porte, dehors, en pleine rue, et ils le détachèrent.
5 anthu ena amene anayima pomwepo anafunsa kuti, “Mukuchita chiyani, kumasula mwana wabuluyo?”
Quelques-uns de ceux qui étaient là leur demandèrent: « Que faites-vous, en détachant le jeune âne? »
6 Iwo anayankha monga mmene Yesu anawawuzira, ndipo anthu aja anawalola kuti apite.
Ils leur répondirent exactement comme Jésus l'avait dit, et ils les laissèrent partir.
7 Atafika naye mwana wabulu kwa Yesu, nayika mikanjo yawo pa buluyo, Iye anakwerapo.
Ils amenèrent le jeune âne à Jésus, y jetèrent leurs vêtements, et Jésus s'assit dessus.
8 Anthu ambiri anayala mikanjo yawo pa msewu, pamene ena anayala nthambi zomwe anadula mʼminda.
Beaucoup étendaient leurs vêtements sur le chemin, et d'autres coupaient des branches d'arbres et les répandaient sur la route.
9 Amene anatsogola ndi iwo amene ankatsatira ankafuwula kuti, “Hosana! “Odala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye!”
Ceux qui précédaient et ceux qui suivaient criaient: « Hosanna! Béni soit celui qui vient au nom du Seigneur!
10 “Odala ndi ufumu umene ukubwera wa abambo athu Davide!” “Hosana Mmwambamwamba!”
Béni soit le royaume de notre père David, qui vient au nom du Seigneur! Hosanna au plus haut des cieux! »
11 Yesu analowa mu Yerusalemu napita ku Nyumba ya Mulungu. Anayangʼana zonse, koma popeza kuti nthawi inali itapita, anatuluka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.
Jésus entra dans le temple de Jérusalem. Après avoir tout regardé, le soir étant venu, il se rendit à Béthanie avec les douze.
12 Mmawa mwake pamene amachoka ku Betaniya, Yesu anamva njala.
Le lendemain, quand ils sortirent de Béthanie, il eut faim.
13 Ataonera patali mtengo wamkuyu uli ndi masamba, anapita kuti akaone ngati unali ndi chipatso chilichonse. Atafika, sanapezemo kanthu koma masamba, chifukwa sinali nthawi ya nkhuyu.
Voyant de loin un figuier qui avait des feuilles, il s'approcha pour voir s'il n'y trouverait pas quelque chose. Lorsqu'il l'atteignit, il ne trouva que des feuilles, car ce n'était pas la saison des figues.
14 Ndipo Iye anati kwa mtengo, “Palibe amene adzadyenso chipatso kuchokera kwa iwe.” Ndipo ophunzira ake anamva Iye akunena izi. (aiōn g165)
Jésus lui dit: « Que personne ne mange plus jamais de fruit de toi! » et ses disciples l'entendirent. (aiōn g165)
15 Atafika ku Yerusalemu, Yesu analowa mʼbwalo lakunja la Nyumba ya Mulungu ndipo anayamba kupirikitsa anthu amene amagula ndi kugulitsa mʼmenemo. Anagubuduza matebulo a osintha ndalama ndi mipando ya ogulitsa nkhunda,
Ils arrivèrent à Jérusalem. Jésus entra dans le temple et se mit à jeter dehors ceux qui vendaient et ceux qui achetaient dans le temple; il renversa les tables des changeurs et les sièges de ceux qui vendaient les colombes.
16 ndipo Iye sanalole aliyense kugulitsa malonda mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu.
Il ne permettait à personne de transporter un récipient dans le temple.
17 Ndipo pamene ankawaphunzitsa, Iye anati, “Kodi sikunalembedwe kuti, ‘Nyumba yanga idzatchedwa Nyumba ya mapemphero kwa anthu a mitundu yonse?’ Koma inu mwayisandutsa ‘phanga la achifwamba.’”
Il enseignait, en leur disant: « N' est-il pas écrit: « Ma maison sera appelée maison de prière pour toutes les nations »? Mais vous en avez fait une caverne de voleurs! »
18 Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo anamva izi ndipo anayamba kufuna njira yoti amuphere Iye, pakuti amamuopa, chifukwa gulu lonse la anthu linazizwa ndi chiphunzitso chake.
Les principaux sacrificateurs et les scribes l'entendirent, et ils cherchaient comment le faire périr. Car ils le craignaient, parce que toute la foule était étonnée de son enseignement.
19 Pofika madzulo, iwo anatuluka mu mzindamo.
Le soir venu, il sortit de la ville.
20 Mmamawa, pamene ankayenda, anaona mtengo wamkuyu uja utafota kuyambira ku mizu.
Comme ils passaient par là le matin, ils virent le figuier desséché jusqu'aux racines.
21 Petro anakumbukira nati kwa Yesu, “Aphunzitsi, taonani! Mtengo wamkuyu munawutemberera uja wafota!”
Pierre, se souvenant, lui dit: « Rabbi, regarde! Le figuier que tu as maudit s'est desséché. »
22 Yesu anayankha kuti, “Khalani ndi chikhulupiriro mwa Mulungu.
Jésus leur répondit: « Ayez foi en Dieu.
23 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati wina aliyense angalamule phiri ili kuti, ‘Pita, kadziponye mʼnyanja,’ ndipo wosakayika mu mtima mwake koma kukhulupirira kuti chimene akunena chidzachitika, chidzachitikadi kwa iyeyo.
Car, je vous le dis en vérité, quiconque dira à cette montagne: « Emporte-la et jette-la dans la mer », et ne doutera pas dans son cœur, mais croira que ce qu'il dit arrive, obtiendra ce qu'il dira.
24 Nʼchifukwa chake ndikukuwuzani kuti chilichonse chimene mupempha mʼpemphero, khulupirirani kuti mwalandira, ndipo chidzakhala chanu.
C'est pourquoi je vous dis que tout ce que vous priez et demandez, croyez que vous l'avez reçu, et vous l'aurez.
25 Pamene muyimirira kupemphera, ngati muli ndi chifukwa ndi wina, mukhululukireni, kuti Atate anu akumwamba akukhululukireni machimo anu.”
Chaque fois que vous êtes en prière, pardonnez, si vous avez quelque chose contre quelqu'un, afin que votre Père, qui est dans les cieux, vous pardonne aussi vos transgressions.
26 (Koma ngati simukhululukirana, ngakhale Atate anu akumwamba sadzakhululukira machimo anu).
Mais si vous ne pardonnez pas, votre Père qui est dans les cieux ne pardonnera pas non plus vos transgressions. »
27 Iwo anafikanso ku Yerusalemu, ndipo pamene Yesu amayenda mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
Ils retournèrent à Jérusalem. Comme il se promenait dans le temple, les principaux sacrificateurs, les scribes et les anciens vinrent à lui.
28 Iwo anafunsa kuti, “Mukuchita izi ndi ulamuliro wanji? Ndipo anakupatsani ulamuliro umenewu ndi ndani?”
Ils se mirent à lui dire: « Par quelle autorité fais-tu ces choses? Ou qui t'a donné l'autorité de faire ces choses? »
29 Yesu anayankha kuti, “Ndikufunsani funso limodzi. Mundiyankhe, ndipo ndikuwuzani ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira izi.
Jésus leur dit: « Je vais vous poser une question. Répondez-moi, et je vous dirai par quelle autorité je fais ces choses.
30 Ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena kwa anthu? Ndiwuzeni.”
Le baptême de Jean, est-il venu du ciel ou des hommes? Répondez-moi. »
31 Iwo anakambirana pakati pawo ndipo anati, “Tikati, ‘Wochokera kumwamba,’ atifunsa kuti, ‘Nanga nʼchifukwa chiyani simunamukhulupirire?’
Ils raisonnaient ainsi entre eux: « Si nous disons: Du ciel, il dira: Pourquoi n'avez-vous pas cru en lui?
32 Koma ife tikati, ‘Wochokera kwa anthu.’” (Amaopa anthu, pakuti aliyense amakhulupirira kuti Yohane analidi mneneri).
Si nous disons: Des hommes, ils craignaient le peuple, car tous tenaient Jean pour un vrai prophète.
33 Ndipo anamuyankha Yesu kuti, “Sitikudziwa.” Yesu anati, “Nanenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji ndichitira zimenezi.”
Ils répondirent à Jésus: « Nous ne savons pas. » Jésus leur dit: « Je ne vous dirai pas non plus par quelle autorité je fais ces choses. »

< Marko 11 >