< Luka 1 >

1 Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
Puisque plusieurs ont entrepris de mettre en ordre le récit des événements qui se sont accomplis parmi nous,
2 monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
comme nous l'ont transmis ceux qui, dès le début, ont été témoins oculaires et serviteurs de la parole,
3 Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
il m'a semblé bon, ayant dès le début suivi exactement le cours de toutes choses, de t'écrire avec ordre, très excellent Théophile,
4 kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
afin que tu saches avec certitude les choses dans lesquelles tu as été instruit.
5 Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
Il y avait, du temps d'Hérode, roi de Judée, un prêtre nommé Zacharie, de la division sacerdotale d'Abija. Il avait une femme parmi les filles d'Aaron, et son nom était Élisabeth.
6 Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
Ils étaient tous deux justes devant Dieu, marchant sans reproche dans tous les commandements et ordonnances du Seigneur.
7 Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
Mais ils n'eurent pas d'enfant, car Élisabeth était stérile, et ils étaient tous deux avancés en âge.
8 Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
Or, tandis qu'il exerçait la fonction de prêtre devant Dieu selon l'ordre de sa division,
9 Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
selon la coutume de la fonction de prêtre, son lot était d'entrer dans le temple du Seigneur et d'y brûler des parfums.
10 Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
Toute la multitude du peuple priait dehors à l'heure de l'encens.
11 Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
Un ange du Seigneur lui apparut, se tenant à droite de l'autel des parfums.
12 Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
Zacharie fut troublé en le voyant, et la peur le saisit.
13 Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
Mais l'ange lui dit: « Ne crains pas, Zacharie, car ta demande a été exaucée. Ta femme, Élisabeth, t'enfantera un fils, et tu lui donneras le nom de Jean.
14 Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
Tu auras de la joie et de l'allégresse, et beaucoup se réjouiront de sa naissance.
15 chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
Car il sera grand aux yeux du Seigneur, et il ne boira ni vin ni boisson forte. Il sera rempli de l'Esprit Saint, dès le sein de sa mère.
16 Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
Il ramènera beaucoup de fils d'Israël à l'Éternel, leur Dieu.
17 Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
Il le précédera avec l'esprit et la puissance d'Élie, pour ramener le cœur des pères vers les enfants, et les désobéissants à la sagesse des justes, afin de préparer un peuple à l'Éternel. »
18 Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
Zacharie dit à l'ange: « Comment puis-je en être sûr? Car je suis un vieil homme, et ma femme est bien avancée en âge. »
19 Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
L'ange lui répondit: « Je suis Gabriel, qui se tient dans la présence de Dieu. J'ai été envoyé pour te parler et t'annoncer cette bonne nouvelle.
20 Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
Voici, tu te tairas et tu ne pourras pas parler jusqu'au jour où ces choses arriveront, parce que tu n'as pas cru à mes paroles, qui s'accompliront en leur temps. »
21 Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
Le peuple attendait Zacharie et s'étonnait qu'il tarde à entrer dans le temple.
22 Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
Lorsqu'il sortit, il ne put leur parler. Ils comprirent qu'il avait eu une vision dans le temple. Il continua à leur faire des signes, et il resta muet.
23 Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
Lorsque les jours de son service furent accomplis, il s'en alla dans sa maison.
24 Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
Après ces jours-là, Élisabeth, sa femme, devint enceinte, et elle se cacha pendant cinq mois, en disant:
25 Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
« C'est ainsi que le Seigneur m'a fait pendant les jours où il m'a regardée, pour ôter mon opprobre parmi les hommes. »
26 Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
Au sixième mois, l'ange Gabriel fut envoyé par Dieu dans une ville de Galilée, nommée Nazareth,
27 kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
auprès d'une vierge promise en mariage à un homme du nom de Joseph, de la maison de David. Le nom de la vierge était Marie.
28 Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
Après être entré, l'ange lui dit: « Réjouis-toi, toi qui es si favorisée! Le Seigneur est avec toi. Tu es bénie entre toutes les femmes! »
29 Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
Mais quand elle le vit, elle fut très troublée par cette parole, et elle réfléchit à la manière dont elle pouvait être saluée.
30 Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
L'ange lui dit: « Ne crains pas, Marie, car tu as trouvé grâce devant Dieu.
31 Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
Voici que tu concevras dans ton sein et tu donneras naissance à un fils, et tu lui donneras le nom de Jésus.
32 Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
Il sera grand et on l'appellera le Fils du Très-Haut. Le Seigneur Dieu lui donnera le trône de son père David,
33 ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
et il régnera sur la maison de Jacob pour toujours. Il n'y aura pas de fin à son règne. » (aiōn g165)
34 Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
Marie dit à l'ange: « Comment cela se peut-il, puisque je suis vierge? »
35 Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
L'ange lui répondit: « L'Esprit Saint viendra sur toi, et la puissance du Très-Haut te couvrira de son ombre. C'est pourquoi aussi le saint qui naîtra de toi sera appelé Fils de Dieu.
36 Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
Voici qu'Élisabeth, ta parente, a conçu un fils dans sa vieillesse, et c'est le sixième mois de celle qu'on appelait stérile.
37 Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
Car rien de ce qui est dit par Dieu n'est impossible. »
38 Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
Marie dit: « Voici la servante du Seigneur; qu'il me soit fait selon ta parole. » Puis l'ange s'éloigna d'elle.
39 Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
En ces jours-là, Marie se leva et se rendit en hâte dans la montagne, dans une ville de Juda,
40 kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
elle entra dans la maison de Zacharie et salua Elisabeth.
41 Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
Lorsqu'Elisabeth entendit la salutation de Marie, l'enfant tressaillit dans son sein, et Elisabeth fut remplie du Saint-Esprit.
42 Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
Elle cria d'une voix forte et dit: « Tu es bénie entre toutes les femmes, et le fruit de tes entrailles est béni!
43 Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
Pourquoi suis-je si favorisée, pour que la mère de mon Seigneur vienne à moi?
44 Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
Car voici, quand la voix de ta salutation est parvenue à mes oreilles, le bébé a bondi de joie dans mon sein!
45 Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
Heureuse celle qui a cru, car les choses qui lui ont été dites de la part du Seigneur s'accompliront! »
46 Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
Marie a dit, « Mon âme magnifie le Seigneur.
47 Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
Mon esprit s'est réjoui en Dieu mon Sauveur,
48 pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
car il a regardé l'humble condition de son serviteur. Car voici qu'à partir de maintenant, toutes les générations me diront béni.
49 pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
Car celui qui est puissant a fait de grandes choses pour moi. Saint est son nom.
50 Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
Sa miséricorde s'étend de génération en génération sur ceux qui le craignent.
51 Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
Il a montré de la force avec son bras. Il a dispersé les orgueilleux dans l'imagination de leur cœur.
52 Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
Il a fait tomber les princes de leurs trônes, et a élevé les humbles.
53 Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
Il a rassasié de bonnes choses les affamés. Il a renvoyé les riches à vide.
54 Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
Il a secouru Israël, son serviteur, pour qu'il se souvienne de la miséricorde,
55 Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
comme il a parlé à nos pères, à Abraham et à sa descendance pour toujours. » (aiōn g165)
56 Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
Marie resta avec elle environ trois mois, puis elle retourna dans sa maison.
57 Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
Le temps où Élisabeth devait accoucher s'accomplit, et elle donna naissance à un fils.
58 Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
Ses voisins et ses proches apprirent que le Seigneur avait magnifié sa miséricorde envers elle, et ils se réjouirent avec elle.
59 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
Le huitième jour, on vint pour circoncire l'enfant, et l'on voulut l'appeler Zacharie, du nom de son père.
60 koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
Sa mère répondit: « Non, mais on l'appellera Jean. »
61 Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
Ils lui dirent: « Il n'y a personne parmi tes proches qui soit appelé de ce nom. »
62 Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
Ils firent des signes à son père, pour savoir comment il voulait qu'on l'appelle.
63 Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
Il demanda une tablette et écrivit: « Son nom est Jean. » Ils étaient tous émerveillés.
64 Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
Aussitôt sa bouche s'ouvrit et sa langue se délia, et il parla en bénissant Dieu.
65 Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
La crainte s'empara de tous les habitants des environs, et l'on parlait de toutes ces paroles dans toute la montagne de Judée.
66 Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
Tous ceux qui les entendaient les fixaient dans leur cœur, en disant: « Que sera donc cet enfant? » La main du Seigneur était avec lui.
67 Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
Son père Zacharie fut rempli du Saint-Esprit, et il prophétisa, disant,
68 “Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
« Béni soit le Seigneur, le Dieu d'Israël, car il a visité et racheté son peuple;
69 Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
et il nous a suscité une corne de salut dans la maison de son serviteur David.
70 (Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
(comme il l'a dit par la bouche de ses saints prophètes qui existent depuis des temps immémoriaux), (aiōn g165)
71 chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
le salut de nos ennemis et de la main de tous ceux qui nous haïssent;
72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
pour faire preuve de clémence envers nos pères, pour se souvenir de sa sainte alliance,
73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
le serment qu'il a fait à Abraham, notre père,
74 kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
de nous accorder que, délivrés de la main de nos ennemis, doivent le servir sans crainte,
75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
dans la sainteté et la droiture devant lui tous les jours de notre vie.
76 “Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
Et toi, mon enfant, tu seras appelé prophète du Très-Haut; car tu iras devant la face du Seigneur pour préparer ses voies,
77 kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
pour donner la connaissance du salut à son peuple par la rémission de ses péchés,
78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
à cause de la tendre miséricorde de notre Dieu, par lequel l'aube d'en haut nous visitera,
79 kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
pour éclairer ceux qui sont assis dans les ténèbres et l'ombre de la mort; pour guider nos pieds sur le chemin de la paix. »
80 Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.
L'enfant grandissait et devenait fort en esprit, et il était dans le désert jusqu'au jour de son apparition publique en Israël.

< Luka 1 >