< Luka 18 >

1 Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
And he spake a parable unto them to the end that they ought always to pray, and not to faint;
2 Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
saying, There was in a city a judge, which feared not God, and regarded not man:
3 Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
and there was a widow in that city; and she came oft unto him, saying, Avenge me of mine adversary.
4 “Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
And he would not for a while: but afterward he said within himself, Though I fear not God, nor regard man;
5 koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
yet because this widow troubleth me, I will avenge her, lest she wear me out by her continual coming.
6 Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
And the Lord said, Hear what the unrighteous judge saith.
7 Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
And shall not God avenge his elect, which cry to him day and night, and he is longsuffering over them?
8 Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
I say unto you, that he will avenge them speedily. Howbeit when the Son of man cometh, shall he find faith on the earth?
9 Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
And he spake also this parable unto certain which trusted in themselves that they were righteous, and set all others at nought:
10 “Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
Two men went up into the temple to pray; the one a Pharisee, and the other a publican.
11 Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
The Pharisee stood and prayed thus with himself, God, I thank thee, that I am not as the rest of men, extortioners, unjust, adulterers, or even as this publican.
12 Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
I fast twice in the week; I give tithes of all that I get.
13 “Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
But the publican, standing afar off, would not lift up so much as his eyes unto heaven, but smote his breast, saying, God, be merciful to me a sinner.
14 “Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
I say unto you, This man went down to his house justified rather than the other: for every one that exalteth himself shall be humbled; but he that humbleth himself shall be exalted.
15 Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
And they brought unto him also their babes, that he should touch them: but when the disciples saw it, they rebuked them.
16 Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
But Jesus called them unto him, saying, Suffer the little children to come unto me, and forbid them not: for of such is the kingdom of God.
17 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
Verily I say unto you, Whosoever shall not receive the kingdom of God as a little child, he shall in no wise enter therein.
18 Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
And a certain ruler asked him, saying, Good Master, what shall I do to inherit eternal life? (aiōnios g166)
19 Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
And Jesus said unto him, Why callest thou me good? none is good, save one, [even] God.
20 Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
Thou knowest the commandments, Do not commit adultery, Do not kill, Do not steal, Do not bear false witness, Honour thy father and mother.
21 Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
And he said, All these things have I observed from my youth up.
22 Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
And when Jesus heard it, he said unto him, One thing thou lackest yet: sell all that thou hast, and distribute unto the poor, and thou shalt have treasure in heaven: and come, follow me.
23 Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
But when he heard these things, he became exceeding sorrowful; for he was very rich.
24 Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
And Jesus seeing him said, How hardly shall they that have riches enter into the kingdom of God!
25 Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
For it is easier for a camel to enter in through a needle’s eye, than for a rich man to enter into the kingdom of God.
26 Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
And they that heard it said, Then who can be saved?
27 Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
But he said, The things which are impossible with men are possible with God.
28 Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
And Peter said, Lo, we have left our own, and followed thee.
29 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
And he said unto them, Verily I say unto you, There is no man that hath left house, or wife, or brethren, or parents, or children, for the kingdom of God’s sake,
30 adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
who shall not receive manifold more in this time, and in the world to come eternal life. (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
And he took unto him the twelve, and said unto them, Behold, we go up to Jerusalem, and all the things that are written by the prophets shall be accomplished unto the Son of man.
32 Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
For he shall be delivered up unto the Gentiles, and shall be mocked, and shamefully entreated, and spit upon:
33 adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
and they shall scourge and kill him: and the third day he shall rise again.
34 Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
And they understood none of these things; and this saying was hid from them, and they perceived not the things that were said.
35 Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
And it came to pass, as he drew nigh unto Jericho, a certain blind man sat by the way side begging:
36 anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
and hearing a multitude going by, he inquired what this meant.
37 Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
And they told him, that Jesus of Nazareth passeth by.
38 Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
And he cried, saying, Jesus, thou son of David, have mercy on me.
39 Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
And they that went before rebuked him, that he should hold his peace: but he cried out the more a great deal, Thou son of David, have mercy on me.
40 Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
And Jesus stood, and commanded him to be brought unto him: and when he was come near, he asked him,
41 “Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
What wilt thou that I should do unto thee? And he said, Lord, that I may receive my sight.
42 Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
And Jesus said unto him, Receive thy sight: thy faith hath made thee whole.
43 Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.
And immediately he received his sight, and followed him, glorifying God: and all the people, when they saw it, gave praise unto God.

< Luka 18 >