< Marko 1 >
1 Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu,
The beginning of the gospel of Jesus Christ, the Son of God.
2 monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya: “Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu,”
Even as it is written in Isaiah the prophet, Behold, I send my messenger before thy face, Who shall prepare thy way;
3 “Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
The voice of one crying in the wilderness, Make ye ready the way of the Lord, Make his paths straight;
4 Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo.
John came, who baptized in the wilderness and preached the baptism of repentance unto remission of sins.
5 Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani.
And there went out unto him all the country of Judaea, and all they of Jerusalem; and they were baptized of him in the river Jordan, confessing their sins.
6 Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo.
And John was clothed with camel’s hair, and [had] a leathern girdle about his loins, and did eat locusts and wild honey.
7 Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake.
And he preached, saying, There cometh after me he that is mightier than I, the latchet of whose shoes I am not worthy to stoop down and unloose.
8 Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”
I baptized you with water; but he shall baptize you with the Holy Ghost.
9 Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
And it came to pass in those days, that Jesus came from Nazareth of Galilee, and was baptized of John in the Jordan.
10 Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda.
And straightway coming up out of the water, he saw the heavens rent asunder, and the Spirit as a dove descending upon him:
11 Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”
And a voice came out of the heavens, Thou art my beloved Son, in thee I am well pleased.
12 Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu,
And straightway the Spirit driveth him forth into the wilderness.
13 ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.
And he was in the wilderness forty days tempted of Satan; and he was with the wild beasts; and the angels ministered unto him.
14 Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati,
Now after that John was delivered up, Jesus came into Galilee, preaching the gospel of God,
15 “Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”
and saying, The time is fulfilled, and the kingdom of God is at hand: repent ye, and believe in the gospel.
16 Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi.
And passing along by the sea of Galilee, he saw Simon and Andrew the brother of Simon casting a net in the sea: for they were fishers.
17 Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
And Jesus said unto them, Come ye after me, and I will make you to become fishers of men.
18 Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.
And straightway they left the nets, and followed him.
19 Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo.
And going on a little further, he saw James the [son] of Zebedee, and John his brother, who also were in the boat mending the nets.
20 Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.
And straightway he called them: and they left their father Zebedee in the boat with the hired servants, and went after him.
21 Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa.
And they go into Capernaum; and straightway on the sabbath day he entered into the synagogue and taught.
22 Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo.
And they were astonished at his teaching: for he taught them as having authority, and not as the scribes.
23 Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti,
And straightway there was in their synagogue a man with an unclean spirit; and he cried out,
24 “Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
saying, What have we to do with thee, thou Jesus of Nazareth? art thou come to destroy us? I know thee who thou art, the Holy One of God.
25 Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!”
And Jesus rebuked him, saying, Hold thy peace, and come out of him.
26 Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.
And the unclean spirit, tearing him and crying with a loud voice, came out of him.
27 Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.”
And they were all amazed, insomuch that they questioned among themselves, saying, What is this? a new teaching! with authority he commandeth even the unclean spirits, and they obey him.
28 Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.
And the report of him went out straightway everywhere into all the region of Galilee round about.
29 Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya.
And straightway, when they were come out of the synagogue, they came into the house of Simon and Andrew, with James and John.
30 Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye.
Now Simon’s wife’s mother lay sick of a fever; and straightway they tell him of her:
31 Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.
and he came and took her by the hand, and raised her up; and the fever left her, and she ministered unto them.
32 Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda.
And at even, when the sun did set, they brought unto him all that were sick, and them that were possessed with devils.
33 Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo,
And all the city was gathered together at the door.
34 Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.
And he healed many that were sick with divers diseases, and cast out many devils; and he suffered not the devils to speak, because they knew him.
35 Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera.
And in the morning, a great while before day, he rose up and went out, and departed into a desert place, and there prayed.
36 Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye,
And Simon and they that were with him followed after him;
37 ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”
and they found him, and say unto him, All are seeking thee.
38 Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.”
And he saith unto them, Let us go elsewhere into the next towns, that I may preach there also; for to this end came I forth.
39 Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.
And he went into their synagogues throughout all Galilee, preaching and casting out devils.
40 Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
And there cometh to him a leper, beseeching him, and kneeling down to him, and saying unto him, If thou wilt, thou canst make me clean.
41 Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!”
And being moved with compassion, he stretched forth his hand, and touched him, and saith unto him, I will; be thou made clean.
42 Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.
And straightway the leprosy departed from him, and he was made clean.
43 Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti,
And he strictly charged him, and straightway sent him out,
44 “Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.”
and saith unto him, See thou say nothing to any man: but go thy way, shew thyself to the priest, and offer for thy cleansing the things which Moses commanded, for a testimony unto them.
45 Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.
But he went out, and began to publish it much, and to spread abroad the matter, insomuch that Jesus could no more openly enter into a city, but was without in desert places: and they came to him from every quarter.