< Levitiko 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh also said to Moses/me,
2 “Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
“Bring Aaron and his sons, and bring their (special clothes/clothes [that they will wear while they do the work of priests)], the oil for anointing them, the bull to be offered to cause them to become forgiven for the sins they have committed, the two rams [to be slaughtered], and the basket containing bread made without yeast.
3 ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
Then gather all the people at the entrance to the Sacred Tent.”
4 Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
Moses/I did what Yahweh told him/me to do, and all the people gathered there.
5 Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
Then Moses/I said to the people, “This is what Yahweh has commanded us to do.”
6 Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
Then he/I brought Aaron and his sons forward and washed them.
7 Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
He/I put the special tunic/shirt on Aaron, tied the sash/waistband around him, put on him the special robe, and put on him the sacred vest/apron. He/I fastened the sacred vest/apron around him, using the skillfully woven sash.
8 Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
He/I put the sacred pouch on his chest and put into it the two stones for him to use to find out what God wants.
9 Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
Then he/I wrapped the turban around Aaron’s head, and fastened on the front of it the gold ornament, the object that showed that he was dedicated to God, like Yahweh had commanded Moses/me.
10 Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
Then Moses/I took the olive oil and anointed the sacred tent and everything in it, and dedicated them [to Yahweh].
11 Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
He/I sprinkled some of the oil on the altar seven times. He/I anointed the altar and all the things used with it, and its huge washbasin and its stand, to dedicate them to Yahweh.
12 Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
He/I poured some of the oil on Aaron’s head and anointed him to dedicate him to Yahweh.
13 Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
Then he/I brought forward Aaron’s sons. He/I put tunics/shirts on them, tied sashes/waistbands around them, and wrapped turbans around their heads, like Yahweh had commanded Moses/me.
14 Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
Then he/I brought the bull for the offering to cause people to be forgiven for the sins that have committed. Then Aaron and his sons put their hands on the bull’s head.
15 Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
Then Moses/I slaughtered the bull, [caught some of its blood in a bowl], and with his/my finger put some of that blood on the projections at the corners of the altar, to purify the altar. He/I poured the rest of the blood at the base of the altar. By doing that, he/I caused it to be a suitable place for burning sacrifices for sin.
16 Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
Moses/I took all the fat that covers the inner parts of the animal, including the liver and kidneys, and burned them on the altar.
17 Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
He/I took the rest of the bull, including the hide and intestines, and burned them outside the camp, like Yahweh had commanded Moses/me.
18 Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
Then he/I brought the ram for the offering that would be completely burned [on the altar], and Aaron and his sons laid their hands on its head.
19 Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
Then Moses/I slaughtered the ram and sprinkled its blood on all sides of the altar.
20 Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
He/I cut the ram into pieces and washed the inner parts and hind legs. Then he/I put the head, the fat, and the other parts of the ram on the altar. As it burned, the aroma of the smoke was pleasing to Yahweh. It was an offering to Yahweh that was burned, as Yahweh had commanded Moses/me.
21 Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
22 Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
Then he/I brought the other ram, the one for consecrating the priests, and Aaron and his sons laid their hands on its head.
23 Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
Moses/I slaughtered that ram, [drained some of its blood in a bowl], and put some of that blood on the lobes of the right ears, the thumbs of the right hands, and the big toes of the right feet of Aaron and his sons [to indicate that what they listened to and what they did and where they went should be directed by Yahweh].
24 Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
25 Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
He/I picked up all the fat of the ram, its fat tail, the fat that covered the inner parts, including the fat that covered the liver and kidneys, and the right thigh of the ram.
26 Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
Then from the basket containing the bread that was made without yeast, the bread which had been dedicated to Yahweh, he/I picked up one loaf of bread [made without olive oil], and one loaf that was [made by mixing the flour] with olive oil, and one wafer. He/I put those on top of the portions of fat, and put them into the hands of Aaron and his sons. Then they lifted them up in the presence of Yahweh [to indicate that it was an offering that belonged to him].
27 Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
28 Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
Then Moses/I took those things from their hands and burned them on the altar. That was the offering that was burned to appoint Aaron and his sons as priests. And the aroma while it burned was pleasing to Yahweh.
29 Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
Moses/I also took the breast of the second ram and lifted it up, as Yahweh had commanded. The breast was Moses’/my share of the ram that was sacrificed to dedicate the priests.
30 Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
Then Moses/I took some of the olive oil for anointing [Aaron and his sons], and some of the blood that was on the altar and sprinkled it on Aaron and his sons and on their clothes. By doing that, he/I consecrated Aaron and his sons and their clothes.
31 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
Then Moses/I said to Aaron and his sons, “Boil the meat [of the second ram] at the entrance of the Sacred Tent, and eat it there with the bread that is in the basket, like I told you to do.
32 Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
Burn up any of the meat and bread that remains.
33 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
The time for you to be set apart as priests will be seven days, so do not leave the entrance of the Sacred Tent for seven days.
34 Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
What we have done today is what Yahweh commanded to cause that you will be forgiven for your sins.
35 Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
You must stay at the entrance of the Sacred Tent for seven days and seven nights and do what Yahweh requires, in order that you will not die [because of disobeying him. I am telling you that] because that is what Yahweh has commanded me to tell you.”
36 Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.
So Aaron and his sons did everything that Yahweh told Moses/me to tell them.

< Levitiko 8 >