< Eksodo 1 >
1 Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
The sons of Jacob who went to Egypt with him along with their families were
2 Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
Reuben, Simeon, Levi, Judah,
3 Isakara, Zebuloni, Benjamini;
Issachar, Zebulun, Benjamin,
4 Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
Dan, Naphtali, Gad, and Asher.
5 Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
Altogether there were 70 people [who went with] Jacob. That included his [sons, his grandsons, and two great-grandsons]. [His son] Joseph was already in Egypt.
6 Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
[Eventually] Joseph and his [older and younger] brothers and everyone [else in their family who lived] (in that generation/at that time) died.
7 Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
But Jacob’s descendants kept giving birth to many children [IDM]. The number [of his descendants] kept becoming larger and larger. As a result, there were so many of them that they were everywhere in Egypt (OR, that they [became a threat] to the Egyptians).
8 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
Then [several hundred years later], a new king began to rule [MTY] in Egypt. He did not know [what] Joseph [had done for the people of Egypt long ago].
9 Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
He said to his people, “Look [at what has happened]! The Israeli people have become so numerous and so powerful that they [now might conquer] us!
10 Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
We must find a way to control them! If we do not do that, their population will continue to grow. Then, if enemies [PRS] attack us, they will join with our enemies and fight against us, and they will escape from [our] land.”
11 Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
So [the king and his officials] put supervisors over the Israeli people to cause them to suffer very much by [forcing them] to work very hard. They forced [the Israeli people to] build [two] cities, Pithom and Ramses, in which to store [supplies for the king/government].
12 Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
But the more cruelly they treated the [Israeli people], the bigger the Israeli [population] grew, and they became more numerous all over [the land]. So the Egyptian people began to be afraid of the Israeli people.
13 ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
They forced the Israeli people to work very hard,
14 Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
and by making them slaves, they made their lives miserable. They [forced them] to [build many buildings with] mortar and bricks. [They also forced them to do] other work in the fields. [In making them do all this work, the Egyptian officials treated them] ruthlessly/cruelly.
15 Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
There were two Hebrew (midwives/women who helped the women when they were giving birth). [Hebrew means the same as Israeli.] The names of the women were Shiphrah and Puah. The king of Egypt said to [those two women],
16 “Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
“When you help the Hebrew women when they are giving birth [MTY], if [the baby that is born] is a boy, you must kill it. If [the baby] is a girl, you (may let it live/do not have to kill them).”
17 Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
But the midwives feared/revered God. So they did not do what the king told them to do. They allowed the baby boys to live.
18 Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
So the king summoned the [two] midwives and said to them, “Why are you doing this? Why are you letting the baby boys live?”
19 Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
[One of] the midwives replied to the king, “[You need to realize that] the Hebrew women are not like the Egyptian women. The Hebrew women are very strong/healthy. They give birth [to their babies] before we can get to them [to help them].”
20 Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
So God acted kindly toward the midwives, and the [Hebrew] people became even more numerous and strong.
21 Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
Furthermore, because the midwives feared/revered God, he enabled them also to give birth to children.
22 Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”
Then the king commanded all (the [Egyptian] people/his [advisors]): “You must throw into the Nile [River] every baby boy born that the [Hebrew women] give birth to! But you can allow the baby girls to live.”