< Levitiko 24 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Gospod je spregovoril Mojzesu, rekoč:
2 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale, a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
»Zapovej Izraelovim otrokom, da ti prinesejo čistega olja iz stolčenih oliv za svetlobo, da bi svetilke nenehno gorele.
3 Kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, mʼchihema cha msonkhano, Aaroni azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa, nthawi zonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yonse.
Zunaj zagrinjala pričevanja, v šotorskem svetišču skupnosti, bo Aron to nenehno ukazoval od večera do jutra pred Gospodom. To bo zakon na veke v vaših rodovih.
4 Aaroni ayatse nyale zimene zili pa choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri kuti zikhale zoyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova.
Svetike bo nenehno oskrboval na čistem svečniku pred Gospodom.
5 “Mutenge ufa wosalala ndipo muphike makeke khumi ndi awiri ndipo keke iliyonse ikhale ya ufa wa makilogalamu awiri.
Vzel boš fino moko in iz nje spekel dvanajst kolačev. Dve desetinki bosta v enem kolaču.
6 Muwayike pa tebulo la golide wabwino kwambiri pamaso pa Yehova mʼmizere iwiri. Mzere uliwonse ukhale wa makeke asanu ndi imodzi.
Postavil jih boš v dve vrsti, šest v vrsto, na čisto mizo pred Gospodom.
7 Pa mzere uliwonse muyikepo lubani wafungo lokoma kuti pamodzi ndi bulediyo akhale wachikumbutso cha nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova.
Nad vsako vrsto boš dal čisto kadilo, da bo ta lahko na kruhu za spomin, torej ognjena daritev Gospodu.
8 Sabata ndi sabata nthawi zonse Aaroni aziyika makeke amenewa pamaso pa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti akhale pangano lamuyaya.
Vsak šabat ga bo nenehno postavljal v vrsto pred Gospodom, vzetega od Izraelovih otrok z večno zavezo.
9 Chakudyacho ndi cha Aaroni ndi ana ake ndipo azidyera ku malo wopatulika chifukwa kwa iye chakudyacho ndi chopatulika kwambiri chochokera pa chopereka chopsereza cha Yehova.”
To bo Aronovo in od njegovih sinov in to bodo jedli na svetem prostoru, kajti to mu je najsvetejše od daritev Gospodu, narejenih z ognjem, z večnim zakonom.«
10 Tsiku lina munthu wina wamwamuna amene amayi ake anali Mwisraeli koma abambo ake anali Mwigupto anapita kwa Aisraeli ndipo anakangana ndi Mwisraeli wina ku msasa.
Sin Izraelke, katere oče je bil Egipčan, je odšel ven med Izraelove otroke in ta sin izraelske ženske in mož iz Izraela sta se skupaj prepirala v taboru.
11 Munthu uja ananyoza dzina la Yehova ndi kulitemberera. Choncho anabwera naye kwa Mose. Dzina la amayi ake linali Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani.
Sin Izraelke je izrekal bogokletje proti Gospodovemu imenu in preklinjal. Privedli so ga k Mojzesu. (In ime njegove matere je bilo Šelomíta, hči Dibríja, iz Danovega rodu.)
12 Anamuyika mʼndende mpaka atadziwa bwino chofuna cha Yehova.
Dali so ga pod stražo, da bi jim bil lahko pokazan Gospodov um.
13 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
Gospod je spregovoril Mojzesu, rekoč:
14 “Pita naye kunja kwa msasa munthu wotembererayo. Onse amene anamumva akutemberera asanjike manja awo pamutu pake ndipo gulu lonse la anthu limugende miyala.
»Privedite tistega, ki je klel zunaj tabora, in naj vsi, ki so ga slišali, položijo roke na njegovo glavo in naj ga vsa skupnost kamna.
15 Choncho uza Aisraeli kuti, ‘Aliyense wotemberera Mulungu wake alangidwe.
Izraelovim otrokom boš govoril, rekoč: ›Kdorkoli preklinja svojega Boga, bo nosil svoj greh.
16 Aliyense wonyoza dzina la Yehova, mlendo ngakhale mbadwa, aphedwe. Gulu lonse la anthu limuponye miyala.
Kdor preklinja Gospodovo ime, bo zagotovo usmrčen in zagotovo ga bo vsa skupnost kamnala; tako tujca, kakor tistega, ki je rojen v deželi, ko preklinja Gospodovo ime, bo usmrčen.
17 “‘Ngati munthu wina aliyense achotsa moyo wa munthu mnzake, munthuyo ayenera kuphedwa.
Kdor ubija kateregakoli človeka, bo zagotovo usmrčen.
18 Aliyense wopha chiweto cha mnzake ayenera kulipira china. Moyo kulipa moyo.
Kdor ubije žival, bo to poplačal; žival za žival.
19 Ngati munthu avulaza mnzake, nayenso amuchite zomwe wachitira mnzakeyo:
Če človek povzroči madež na svojem bližnjem; kakor je storil on, tako naj bo to storjeno njemu;
20 kuthyola fupa kulipira kuthyola fupa, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino. Monga momwe anavulazira mnzake, amuvulaze chimodzimodzinso.
zlom za zlom, oko za oko, zob za zob. Kakor je on na človeku povzročil pomanjkljivost, tako naj bo njemu ponovno storjeno.
21 Aliyense wopha chiweto cha mnzake, alipire chiweto china, koma aliyense wopha munthu ayenera kuphedwa.
Kdor ubije žival, bo to povrnil, kdor pa ubije človeka, bo usmrčen.
22 Lamulo la mlendo ndi mbadwa ndi limodzi lomweli. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Imeli boste eno vrsto postave, prav tako za tujca, kakor za nekoga iz svoje lastne dežele, kajti jaz sem Gospod, vaš Bog.‹«
23 Pamenepo Mose anawuza Aisraeli zimenezi, ndipo iwo anatulutsira munthu wotembererayo kunja kwa msasa ndi kumugenda miyala. Aisraeli anachita zimene Yehova analamula Mose.
Mojzes je Izraelovim otrokom spregovoril, da naj tistega, ki je preklet, privedejo ven iz tabora in kamnajo s kamni. In Izraelovi otroci so storili tako, kakor je Gospod zapovedal Mojzesu.

< Levitiko 24 >