< Levitiko 13 >

1 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi lakuAroni isithi:
2 “Munthu akakhala ndi chithupsa, kapena mʼbuko, kapena chikanga pa thupi lake chimene chitha kusanduka nthenda ya khate, abwere naye munthuyo kwa Aaroni wansembe kapena kwa mmodzi mwa ana ake amene ndi ansembe.
Umuntu, nxa kukhona esikhumbeni senyama yakhe ithumba loba uqweqwe loba ibala elikhanyayo, njalo esikhumbeni senyama yakhe kube njengesifo sobulephero, khona ezalethwa kuAroni umpristi kumbe kwenye yamadodana akhe angabapristi.
3 Tsono wansembe ayangʼanitsitse nthendayo pa khungupo, ndipo ngati ubweya wa pamalo pamene pali nthendapo wasanduka woyera, komanso kuti nthendayo yazama mʼkati kupitirira khungu, ndiye kuti nthendayo ndi khate. Wansembe akamuonetsetsa alengeze kuti ndi wodetsedwa.
Umpristi uzakhangela-ke isifo esikhumbeni senyama; uba uboya esifweni sebuphenduke baba mhlophe, lokubonakala kwesifo sekutshone kulesikhumba senyama yakhe, kuyisifo sobulephero. Umpristi esemkhangele uzakutsho ukuthi ungcolile.
4 Ngati chikanga cha pa khungulo chikuoneka choyera, ndipo kuya kwake sikukuonekera kuti kwapitirira khungu ndi ubweya wake pamalopo sunasanduke woyera, wansembe amuyike wodwalayo padera kwa masiku asanu ndi awiri.
Kodwa uba ibala elikhanyayo esikhumbeni senyama yakhe limhlophe, lokubonakala kwalo kungatshoni kulesikhumba, loboya balo bungaphendukanga baba mhlophe, umpristi uzamvalela olesifo insuku eziyisikhombisa.
5 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso bwino wodwalayo. Ndipo ngati waona kuti nthendayo sinasinthe ndipo sinafalikire pa khungu, amuyikenso wodwalayo padera kwa masiku ena asanu ndi awiri.
Umpristi uzamkhangela-ke ngosuku lwesikhombisa; uba, khangela, isifo sisemi emehlweni akhe, isifo singaqhelanga esikhumbeni, umpristi uzamvalela ezinye insuku eziyisikhombisa.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembeyo amuonenso bwino munthuyo, ndipo ngati nthendayo yazima ndi kusafalikira pa khungu, wansembe amutchule munthuyo kuti ndi woyera. Umenewo unali mʼbuko chabe. Choncho munthuyo achape zovala zake ndipo adzakhala woyera.
Umpristi uzabuya-ke amkhangele ngosuku lwesikhombisa; uba, khangela, isifo sifiphele, lesifo singaqhelanga esikhumbeni, umpristi uzakutsho ukuthi uhlambulukile; luqweqwe. Njalo uzahlamba izembatho zakhe, ahlambuluke.
7 Koma ngati mʼbukowo ufalikira pakhungu atakadzionetsa kale kwa wansembe ndipo wansembeyo nʼkulengeza kuti munthuyo ndi woyeretsedwa, ndiye kuti apitenso kukadzionetsa kwa wansembeyo.
Kodwa uba uqweqwe luqhela kakhulu esikhumbeni emva kokubonakaliswa kwakhe kumpristi ngokuhlanjululwa kwakhe, uzabonakaliswa kumpristi futhi.
8 Wansembe amuonetsetsenso munthuyo, ndipo ngati mʼbukowo wafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa ndi kuti nthendayo ndi khate.
Uba umpristi ebona ukuthi, khangela, uqweqwe luyaqhela esikhumbeni, umpristi uzakutsho ukuthi ungcolile; kuyibulephero.
9 “Ngati munthu aliyense ali ndi nthenda ya pakhungu yoyipitsa thupi, wodwalayo abwere naye kwa wansembe.
Isifo sobulephero, uba sisemuntwini, uzalethwa kumpristi.
10 Wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati ali ndi chithupsa chamaonekedwe woyera pa khungupo chimene chasandutsa ubweya wa pamalopo kukhala woyera, ndipo ngati pali zilonda pa chotupacho,
Njalo umpristi uzabona, khangela-ke, kukhona ithumba elimhlophe esikhumbeni, seliphendule uboya baba mhlophe, futhi kulenyama entsha ephilayo ethunjeni,
11 limenelo ndi khate lachikhalire la pa khungu, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Asamutsekere munthu woteroyo pakuti ndi wodetsedwa kale.
kuyibulephero obudala esikhumbeni senyama yakhe; umpristi uzakutsho-ke ukuthi ungcolile, angamvaleli ngoba engcolile.
12 “Ndipo ngati, mʼkuona kwa wansembe, khate lija lafalikira pa khungu lonse moti lamugwira thupi lonse kuyambira kumutu mpaka kumapazi,
Uba-ke ubulephero buqhela kakhulu esikhumbeni, lobulephero bugubuzela isikhumba sonke salowo olesifo, kusukela ekhanda lakhe kuze kufike lenyaweni zakhe, njengokubona konke kwamehlo ompristi,
13 wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati khatero lagwira thupi lake lonse, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Popeza kuti thupi lonse lasanduka loyera, munthuyo ndi woyeretsedwa.
umpristi uzabona, khangela-ke, ubulephero bugubuzele inyama yonke yakhe, uzakutsho ukuthi olesifo uhlambulukile; konke kuphendukile kwaba mhlophe; uhlambulukile.
14 Koma pa tsiku limene zilonda zidzaoneka pa iye, munthuyo adzakhala wodetsedwa.
Kodwa mhla kubonakala kuye inyama ebomvu, uzakuba ngongcolileyo.
15 Wansembe aonetsetse zilondazo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zilondazo ndi zodetsedwa ndipo ili ndi khate.
Lapho umpristi esebone inyama ebomvu, uzakutsho ukuthi ungcolile; inyama ebomvu ingcolile, iyibulephero.
16 Koma zilondazo zikasinthika ndi kusanduka zoyera, munthuyo ayenera kupita kwa wansembe.
Kumbe uba inyama ebomvu ibuye iphenduke ibe mhlophe, uzakuya kumpristi.
17 Wansembe amuonetsetse ndipo ngati zilondazo zasanduka zoyera, wansembe amutchule wodwalayo kuti ndi woyera ndipo adzakhala woyera ndithu.
Lapho umpristi esembonile ukuthi, khangela, isifo sesiphenduke saba mhlophe, umpristi uzakutsho ukuthi uhlambulukile olesifo; uhlambulukile.
18 “Ngati pa khungu la munthu wodwalayo pali chithupsa chimene chinapola kale,
Inyama layo, nxa kukhona kuyo, esikhumbeni sayo, ithumba, selipholile,
19 ndipo pamalo pamene panali chithupsacho pakatuluka chotupa choyera kapena banga loyera mofiirira, munthuyo ayenera kukadzionetsa kwa wansembe.
lendaweni yethumba kube lokuvuvuka okumhlophe kumbe ibala elikhanyayo elimhlophe libomvana, kuzatshengiswa umpristi.
20 Wansembe aonetsetse bwino ndipo ngati chikuoneka kuti chazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka woyera, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Imeneyo ndi nthenda ya khate imene yatuluka mʼchithupsacho.
Uba umpristi ezabona ukuthi, khangela, ukubonakala kwakho kutshone kulesikhumba, loboya bakho sebuphenduke baba mhlophe, umpristi uzakutsho ukuthi ungcolile; kuyisifo sobulephero, siphume ethunjeni.
21 Koma ngati wansembe waonetsetsa napeza kuti palibe ubweya woyera ndipo chithupsacho sichinazame, koma chazimirira, wansembeyo amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
Kodwa uba umpristi ezakubona ukuthi, khangela, kakulaboya obumhlophe kukho, lokuthi kakutshonanga kulesikhumba, kodwa kufiphele, umpristi uzamvalela insuku eziyisikhombisa.
22 Ngati nthendayo ikufalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limeneli ndi khate.
Uba-ke kuqhela kakhulu esikhumbeni, umpristi atsho ukuthi ungcolile, kuyisifo.
23 Koma bangalo likakhala malo amodzi, wosafalikira, chimenecho ndi chipsera cha chithupsacho, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera.
Kodwa uba ibala elikhanyayo limi endaweni yalo, lingaqheli, kuyisibavu sethumba; umpristi uzakutsho-ke ukuthi uhlambulukile.
24 “Munthu akakhala ndi bala lamoto pa khungu lake, ndipo chilonda cha balalo chikasanduka banga loyera mofiirira kapena loyera,
Kumbe inyama, uba kukhona esikhumbeni sayo umtshiso womlilo, lokuphola komtshiso kulibala elikhanyayo elimhlophe libomvana kumbe limhlophe.
25 wansembe aonetsetse bangalo, ndipo ngati ubweya wa pa bangapo usanduka woyera, ndipo balalo lioneka kuti ndi lozama, limenelo ndi khate lomwe latuluka pa balalo. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate la pa khungu.
Lapho umpristi eselibonile ukuthi, khangela, uboya bebala elikhanyayo buphenduke baba mhlophe, lokubonakala kwalo litshone kulesikhumba, kuyibulephero, buqhamuke emtshisweni; ngakho umpristi uzakutsho ukuthi ungcolile; kuyisifo sobulephero.
26 Koma ngati wansembe waonetsetsa balalo ndipo palibe ubweya woyera, ndipo ngati balalo silinazame ndi kuti lazirala, wansembe amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
Kodwa uba umpristi eselibona ukuthi, khangela, kakulaboya obumhlophe ebaleni elikhanyayo, lokuthi kalitshonanga kulesikhumba, kodwa lifiphele, umpristi uzamvalela insuku eziyisikhombisa.
27 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso wodwalayo, ndipo ngati bangalo lafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate.
Langosuku lwesikhombisa umpristi uzambona; uba liqhele kakhulu esikhumbeni, umpristi uzakutsho ukuthi ungcolile; kuyisifo sobulephero.
28 Koma ngati bangalo likhala pa malo amodzi wosafalikira pa khungu, ndipo lazimirira, limenelo ndi thuza la bala lamoto, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Chimenecho ndi chipsera chamoto.
Kodwa uba ibala elikhanyayo limi endaweni yalo, lingaqhelanga esikhumbeni, kodwa lifiphele, kuyikuvuvuka komtshiso; umpristi atsho-ke ukuthi uhlambulukile, ngoba kuyisibavu somtshiso.
29 “Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi nthenda kumutu kapena ku chibwano,
Njalo nxa owesilisa loba owesifazana elesifo ekhanda loba endevini,
30 wansembe aonetsetse balalo ndipo likaoneka kuti lazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka wachikasu ndi wonyololoka, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zimenezo ndi mfundu zonyerenyetsa, khate lakumutu kapena ku chibwano.
lapho umpristi esebonile isifo ukuthi, khangela, ukubonakala kwaso kutshonile kulesikhumba, njalo kulezinwele ezilithanga ezinciphileyo, umpristi uzakutsho ukuthi ungcolile; kuluqweqwe; kuyibulephero bekhanda loba obendevu.
31 Koma wansembe akaonetsetsa mfundu zonyerenyetsazo, ndipo zikaoneka kuti sizinazame ndi kuti palibe ubweya wakuda, wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku asanu ndi awiri.
Uba-ke umpristi esebone isifo soqweqwe ukuthi, khangela, ukubonakala kwaso kasitshonanga kulesikhumba, lokuthi kakulanwele ezimnyama kuso, umpristi uzamvalela olesifo soqweqwe insuku eziyisikhombisa.
32 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo, ndipo ngati sizinafalikire ndipo palibe ubweya wachikasu pamalopo ndiponso sizinazame,
Langosuku lwesikhombisa umpristi uzabona isifo; uba, khangela, uqweqwe lungaqhelanga, futhi kungekho kuso inwele ezilithanga, lokubonakala koqweqwe kungatshonanga kulesikhumba,
33 wodwalayo ametedwe, koma pamene pali mfunduyo pasametedwe. Wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
uzaziphuca, kodwa uqweqwe angaluphuci, lompristi uzamvalela oloqweqwe ezinye insuku eziyisikhombisa.
34 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo ndipo ngati sizinafalikire pa khungu ndi kuti sizinazame, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Tsono achape zovala zake, ndipo adzakhala woyera.
Langosuku lwesikhombisa umpristi uzabona uqweqwe; uba, khangela, uqweqwe lungaqhelanga esikhumbeni, futhi ukubonakala kwalo kungatshonanga kulesikhumba, umpristi uzakutsho ukuthi uhlambulukile, njalo uzahlamba izembatho zakhe, ahlambuluke.
35 Koma mfundu zonyerenyetsazo zikafalikira pa khungu, wansembe atalengeza kuti ndi woyera,
Kodwa uba uqweqwe luqhela kakhulu esikhumbeni emva kokuhlanjululwa kwakhe,
36 wansembe amuonetsetsenso wodwalayo ndipo ngati mfunduzo zafalikira pa khungu, iye asalabadirenso zoyangʼana ngati ubweya uli wachikasu. Munthuyo ndi wodetsedwa.
umpristi uzabe esembonile ukuthi, khangela, uqweqwe seluqhelile esikhumbeni, umpristi kangadingi inwele ezilithanga; ungcolile.
37 Koma ngati wansembe waonetsetsa kuti mfunduzo sizinasinthe ndipo ubweya wakuda wamera pa mfundupo, ndiye kuti wodwalayo wachira. Tsono wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa.
Kodwa uba emehlweni akhe uqweqwe lusemi, lenwele ezimnyama sezimilile kulo, uqweqwe selupholile, uhlambulukile; lompristi uzakutsho ukuthi uhlambulukile.
38 “Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi mawanga woyera pa khungu,
Njalo owesilisa loba owesifazana, nxa kukhona esikhumbeni senyama yabo amabala akhanyayo, amabala akhanyayo amhlophe,
39 wansembe aonetsetse mawangawo, ndipo ngati ali otuwa, ndiye kuti ndi mibuko chabe yotuluka pa khungu. Munthuyo ndi woyera.
nxa umpristi ebona ukuthi, khangela, esikhumbeni senyama yabo kulamabala akhanyayo afipheleyo amhlophe, kuyimpunza equbukayo esikhumbeni; uhlambulukile.
40 “Tsitsi la munthu likayoyoka kumutu ndiye kuti ndi dazi limenelo koma munthuyo ndi woyeretsedwa.
Lendoda, uba ikhanda layo lingaselanwele, ulempabanga, uhlambulukile.
41 Ngati tsitsi lake layoyoka chapamphumi ndiye kuti ndi dazi la pa chipumi limenelo koma munthuyo ndi woyera.
Uba-ke ikhanda layo lingaselanwele eceleni lebunzi layo, ulempabanga ebunzini, uhlambulukile.
42 Koma ngati pa dazi la pamutu kapena la pa chipumi pakhala chithupsa choyera mofiirira, ndiye kuti ndi khate limenelo lochokera mu dazi la pamutu lija kapena pa chipumi lija.
Kodwa uba kukhona isifo esimhlophe sibomvana empabangeni kumbe empabangeni esebunzini, kuyibulephero obuqubuka ebumpabangeni bayo kumbe empabangeni esebunzini layo.
43 Tsono wansembe amuonetsetse wodwalayo ndipo ngati chithupsa cha pa dazi lapankhongo kapena pa dazi lapachipumicho ndi choyera mofiirira monga nthenda ya khate imaonekera,
Lapho umpristi esembonile ukuthi, khangela, ukuvuvuka kwesifo kumhlophe kubomvana empabangeni yayo kumbe empabangeni esebunzini layo, njengokubonakala kobulephero esikhumbeni senyama,
44 ndiye kuti munthuyo ali ndi khate, motero ndi wodetsedwa. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa chifukwa cha chithupsa cha pamutu pakepo.
uyindoda elobulephero, ungcolile; umpristi uzakutsho ukuthi ungcolile kakhulu; isifo sayo sisekhanda layo.
45 “Munthu wa khate lotere avale sanza, tsitsi lake alilekerere, aphimbe mlomo wake wapamwamba ndipo azifuwula kuti, ‘Ndine wodetsedwa, ndine wodetsedwa!’
Umlephero, esikuye isifo, izembatho zakhe zizadatshulwa-ke, lekhanda lakhe lembulwe, njalo ambomboze indevu zendebe yakhe yangaphezulu, akhale athi: Ngcolile, ngcolile!
46 Munthu wodwalayo adzakhala wodetsedwa kwa nthawi yonse imene ali ndi nthendayo. Iye ayenera kumakhala payekha kunja kwa msasa.
Zonke insuku isifo sikuye ungcolile; ungcolile, uzahlala yedwa, indawo yakhe yokuhlala izakuba ngaphandle kwenkamba.
47 “Nsalu iliyonse ikakhala ndi nguwi,
Njalo isembatho, nxa isifo sobulephero sikuso, esembathweni soboya bezimvu, loba esembathweni selembu elicolekileyo,
48 kaya ndi chovala chopangidwa ndi nsalu yathonje kapena yaubweya, yoluka ndi thonje kapena ubweya, yachikopa kapena yopangidwa ndi chikopa,
loba ezintanjeni eziqondileyo kumbe ezintanjeni eziqumayo zelembu elicolekileyo kumbe ezoboya bezimvu, loba esikhumbeni, kumbe kukuphi okwenziwe ngesikhumba,
49 ndipo ngati pamalo pamene pachita nguwiyo pali ndi maonekedwe obiriwira kapena ofiirira imeneyo ndi nguwi yoyipitsa chovala ndipo chovalacho chikaonetsedwe kwa wansembe.
futhi isifo siluhlazana loba sibomvana esembathweni loba esikhumbeni loba ezintanjeni eziqondileyo loba ezintanjeni eziqumayo kumbe kuyiphi into yesikhumba; kuyisifo sobulephero, njalo kuzatshengiswa umpristi.
50 Wansembeyo ayionetsetse nguwiyo ndipo chovalacho achiyike padera kwa masiku asanu ndi awiri.
Umpristi uzakhangela-ke isifo, avalele okulesifo insuku eziyisikhombisa.
51 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ayionetsetsenso nguwiyo ndipo ngati nguwiyo yafalikira pa chovalacho, chathonje kapena chaubweya, kapena pa chikopacho, kaya ndi cha ntchito ya mtundu wanji, imeneyo ndi nguwi yoopsa ndipo chovalacho ndi chodetsedwa.
Akhangele isifo ngosuku lwesikhombisa; uba isifo siqhelile esembathweni loba ezintanjeni eziqondileyo loba ezintanjeni eziqumayo loba esikhumbeni, loba kuwuphi umsebenzi owenziwe ngesikhumba; isifo siyibulephero obuvukuzayo; kungcolile.
52 Wansembe atenthe chovala chathonje kapena chaubweya chija, ngakhalenso chinthu chachikopa chija popeza nguwiyo yachidetsa. Nguwiyo ndi yoopsa choncho chinthucho achitenthe.
Ngakho uzatshisa isembatho loba izintambo eziqondileyo loba izintambo eziqumayo zoboya bezimvu loba ezelembu elicolekileyo kumbe loba yiyiphi into yesikhumba okukuyo isifo; ngoba kuyibulephero obuvukuzayo; kuzatshiswa ngomlilo.
53 “Koma ngati wansembe akayangʼanitsitsa nguwiyo apeza kuti sinafalikire pa chovalacho kapena pa chinthu chilichonse chachikopa,
Kodwa uba umpristi ebona ukuthi, khangela, isifo kasiqhelanga esembathweni kumbe ezintanjeni eziqondileyo kumbe ezintanjeni eziqumayo, kumbe loba kuyiphi into yesikhumba,
54 iye alamulire kuti chinthu choyipitsidwacho achichape. Akatero achiyike padera kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
umpristi uzalaya-ke ukuthi bawatshe lokho esikukho isifo, akuvalele ezinye insuku eziyisikhombisa.
55 Chovalacho chitachapidwa, wansembe achionenso ndipo ngati nguwiyo sinasinthe maonekedwe ake, ngakhale kuti sinafalikire, chovalacho ndi chodetsedwa ndithu. Muchitenthe, ngakhale kuti nguwiyo ili kumbuyo kapena kumaso kwa chinthucho.
Kuzakuthi umpristi, sekuwatshiwe, abone isifo ukuthi, khangela, isifo kasiphendukanga ukubonakala kwaso, lesifo kasiqhelanga; kungcolile. Uzakutshisa ngomlilo; kuyikucutheka kohlangothi lwakho lwangemuva loba uhlangothi lwakho lwaphambili.
56 Koma ngati wansembe aonetsetsa nʼkupeza kuti nguwi ija yathimbirira pa chovala chija kapena pa chinthu chachikopa chija atachichapa, ndiye angʼambeko chinthucho pa banga la nguwiyo.
Kodwa uba umpristi ebona ukuthi, khangela, isifo sifiphele emva kokuwatshwa kwaso, uzasidabula esembathweni, loba esikhumbeni, loba ezintanjeni eziqondileyo, kumbe ezintanjeni eziqumayo.
57 Koma ngati nguwiyo iwonekanso pa chovala chathonje kapena chaubweya ndiye kuti nguwiyo ikufalikira. Chilichonse chimene chili ndi nguwi chiyenera kutenthedwa.
Kodwa uba silokhu sibonakala esembathweni loba ezintanjeni eziqondileyo kumbe ezintanjeni eziqumayo kumbe loba kuyiphi into yesikhumba, siyaqhela; uzakutshisa ngomlilo lokho esikukho isifo.
58 Chovala chathonje kapena chaubweya, ngakhale chinthu china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, mukachichapa nguwi yake nʼkuchoka muchichapenso kawiri ndipo chidzakhala choyeretsedwa.”
Kodwa isembatho kumbe izintambo eziqondileyo loba izintambo eziqumayo kumbe loba yiyiphi into yesikhumba okuwatshileyo, uba isifo sisukile kukho, kuzawatshwa okwesibili, kuzahlambuluka-ke.
59 Amenewa ndiwo malamulo a nguwi yokhala pa chovala chaubweya kapena pa chovala chathonje, kapenanso pa chinthu chilichonse chopangidwa ndi chikopa kuti muzitha kulekanitsa choyeretsedwa ndi chodetsedwa.
Lo ngumlayo wesifo sobulephero wesembatho soboya bezimvu kumbe selembu elicolekileyo, loba izintambo eziqondileyo loba izintambo eziqumayo, kumbe loba yiyiphi into yesikhumba, ukutsho ukuthi kuhlambulukile kumbe ukutsho ukuthi kungcolile.

< Levitiko 13 >