< Levitiko 11 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi lakuAroni isithi kibo:
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Nyama zomwe mukhoza kudya mwa nyama zonse za dziko lapansi ndi izi:
Tshonini ebantwaneni bakoIsrayeli lithi: Lezi zinyamazana elingazidla kuzo zonke inyamazana ezisemhlabeni.
3 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
Konke okwehlukanisa isondo lokwehlukanisa isondo kabili lokwetshisayo phakathi kwenyamazana, lokhu lizakudla.
4 “‘Koma pali nyama zina zimene zimabzikula kokha kapena ndi zogawikana zipondero zimene simukuyenera kudya. Nyama zimenezi ndi ngamira, ngakhale imabzikula ilibe zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
Kodwa lezi kaliyikuzidla kulezo ezetshisayo kumbe kulezo ezehlukanisa isondo: Ikamela, ngoba liyetshisa, kodwa kalehlukanisi amasondo; lingcolile kini.
5 Ina ndi mbira, ngakhale imabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
Lembila, ngoba iyetshisa, kodwa kayehlukanisi isondo; ingcolile kini.
6 Inanso ndi kalulu, ngakhale amabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi wodetsedwa, musadye.
Lomvundla, ngoba uyetshisa, kodwa kawehlukanisi isondo; ungcolile kini.
7 Nkhumba simabzikula ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
Lengulube, ngoba iyehlukanisa isondo lokwehlukanisa isondo kube kubili kodwa kayetshisi; ingcolile kini.
8 Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa chifukwa ndi yodetsedwa.
Lingadli okwenyama yazo, lingathinti isidumbu sazo; zingcolile kini.
9 “‘Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi a mʼnyanja ndi a mʼmitsinje mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
Lezi lingazidla kuzo zonke ezisemanzini: Zonke ezilempiko lamaxolo, emanzini, enlwandle lemifuleni, lezo lingazidla.
10 Koma zamoyo zonse za mʼnyanja kapena za mʼmitsinje zimene zilibe minga ya pa msana ndi mamba, kaya ndi tizirombo tonse ta mʼmadzi ndi zamoyo zonse zopezeka mʼmenemo ndi zodetsedwa kwa inu.
Kodwa zonke ezingelampiko lamaxolo enlwandle lemifuleni, phakathi kwazo zonke ezibhinqika emanzini laphakathi kwaso sonke isidalwa esiphilayo esisemanzini, ziyisinengiso kini.
11 Pakuti zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu, nyama yake musadye, ndipo zikafa zikhalebe zodetsedwa kwa inu.
Yebo, zizakuba yisinengiso kini; lingadli okwenyama yazo; kodwa lizanengwa yisidumbu sazo.
12 Chamoyo chilichonse cha mʼmadzi chimene chilibe minga ya pa msana kapena mamba ndi chodetsedwa kwa inu.
Konke okungelampiko lamaxolo emanzini, kuyisinengiso kini.
13 “‘Mbalame zimene simukuyenera kudya chifukwa ndi zodetsedwa ndi izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
Lezi-ke lizanengwa yizo phakathi kwezinyoni; kaziyikudliwa, ziyisinengiso; ukhozi lelinqe lengqungqulu edla inhlanzi,
14 nankapakapa, akamtema a mitundu yonse,
lomzwazwa, lohelwane ngohlobo lwalo,
15 akhungubwi a mitundu yonse,
lonke iwabayi ngohlobo lwalo,
16 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo ndi mtundu uliwonse wa akabawi
lesikhova, lomandukulo, lenkanku, lokhozi ngohlobo lwalo,
17 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
lesikhova esincinyane, letshayamanzi, lesikhova esikhulu,
18 tsekwe, vuwo, dembo,
lesikhova esimhlophe, lewunkwe, lelinqe elikhulu,
19 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
lengabuzane, ihemu ngohlobo lwalo, lemvenduna, lolulwane.
20 “‘Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa.
Zonke izibungu ezilempiko ezihamba ngezine ziyisinengiso kini.
21 Komabe mwa zowuluka zokhala ndi miyendo inayi zimene mukhoza kudya ndi zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira.
Kodwa lezi lizazidla ezibungwini ezilempiko ezihamba ngezine ezilemilenze ephezu kwenyawo zazo ezeqa ngayo emhlabeni;
22 Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse.
lezi lingadla kuzo: Isikhonyane ngohlobo lwaso, lonyelele ngohlobo lwakhe, lediye ngohlobo lwalo, lentethe ngohlobo lwayo.
23 Koma za mapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inayi muzitenge kukhala zodetsedwa kwa inu.
Kodwa zonke izibungu ezilempiko, ezilenyawo ezine, ziyisinengiso kini.
24 “‘Zimenezi zidzakudetsani. Aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Langalezi lizangcoliswa; wonke othinta isidumbu sazo uzakuba ngongcolileyo kuze kuhlwe.
25 Aliyense wonyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Njalo wonke ophakamisa okwesidumbu sazo uzahlamba izembatho zakhe, abe ngongcolileyo kuze kuhlwe.
26 “‘Nyama iliyonse imene ili ndi ziboda zogawikana koma mapazi ake wosagawikana, kapena imene sibzikula muyiyese yodetsedwa kwa inu ndipo munthu aliyense akakhudza nyama yakufayo, adzakhala wodetsedwa.
Yonke inyamazana eyehlukanisa isondo, kodwa ingehlukanisi isondo kabili, njalo ingetshisi, ingcolile kini; wonke oyithintayo uzangcola.
27 Mwa nyama zonse zoyenda ndi miyendo inayi, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo kuphazi muzitenge kukhala zodetsedwa ndipo aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Konke-ke okuhamba ngezidladla zakho, phakathi kwazo zonke inyamazana ezihamba ngezine, zingcolile kini; wonke othinta isidumbu sazo uzangcola kuze kuhlwe.
28 Aliyense wonyamula nyamazi zitafa ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu.
Lothwala isidumbu sazo uzahlamba izembatho zakhe, abe ngongcolileyo kuze kuhlwe; zingcolile kini.
29 “‘Mwa nyama zokwawa, zimene zili zodetsedwa kwa inu ndi izi: likongwe, mbewa, msambulu za mitundu yonse,
Futhi lezi zizakuba ngezingcolileyo kini, phakathi kwezihuquzelayo ezihuquzelayo emhlabeni; ubuchakide, legundwane, legwababa ngohlobo lwalo,
30 gondwa, mngʼazi, buluzi, dududu ndi nanzikambe.
lontulo, lembulumakhasana, lombankwa, lesiqhuza, lonwabu.
31 Mwa nyama zonse zoyenda pansi, zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu. Munthu aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Lezi zingcolile kini phakathi kwazo zonke ezihuquzelayo; wonke ozithintayo sezifile uzakuba ngongcolileyo kuze kuhlwe.
32 Iliyonse mwa nyama zimenezi ikafa ndi kugwera pa chiwiya chilichonse, kaya chimagwira ntchito yotani, kaya ndi chopangidwa ndi mtengo, kaya ndi cha nsalu, kaya ndi cha chikopa kapena chiguduli chiwiyacho chidzakhala chodetsedwa. Muchiviyike mʼmadzi chiwiyacho komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo, ndipo kenaka chidzakhala choyeretsedwa.
Konke-ke ewela phezu kwakho enye yazo isifile kuzakuba ngokungcolileyo, lokwasiphi isitsha sesihlahla, loba isembatho, loba isikhumba, loba isaka, lasiphi isitsha okusetshenzwa ngaso; kuzafakwa emanzini, njalo kuzakuba ngokungcolileyo kuze kuhlwe; khona kuzahlambuluka.
33 Tsono nyama ina iliyonse mwa zimenezi ikagwera mʼmbiya ya dothi, ndiye kuti chilichonse cha mʼmbiyamo chidzakhala chodetsedwa, ndipo muyenera kuswa mbiyayo.
Layo yonke imbiza yebumba ewela phakathi kwayo enye yazo, konke okukiyo kuzakuba ngokungcolileyo, njalo lizayibulala.
34 Chakudya chilichonse chimene mungadye chikakhala kuti chathiridwa mʼmbiyamo, ndiye kuti chakudyacho chidzakhala chodetsedwa, ndipo madzi akumwa wochokera mʼmbiya zotere ndi wodetsedwa.
Ekudleni konke okudliwayo afike kukho amanzi kuzakuba ngokungcolileyo; lakuphi okunathwayo okunganathwa phakathi kwaloba yiyiphi imbiza enjalo kuzakuba ngokungcolileyo.
35 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufa chikagwera pa chinthu chilichonse kaya pa uvuni, kapena pa mʼphika, ndiye kuti zinthuzo zidzakhala zodetsedwa, ndipo ziphwanyidwe popeza ndi zodetsedwa.
Konke-ke okuwela kukho okwesidumbu sazo kuzakuba ngokungcolileyo; iziko loba isitofu, kuzaphohlozwa, kungcolile, futhi kuzakuba ngokungcolileyo kini.
36 Koma kasupe kapena chitsime chamadzi chidzakhala choyeretsedwa ngakhale kuti chilichonse chokhudza nyama yakufayo chidzakhala chodetsedwa. Zimenezi muzitenge kukhala zodetsedwa.
Kodwa umthombo loba umgodi aqoqene khona amanzi uzakuba ngohlambulukileyo; kodwa okuthinta izidumbu zazo kuzakuba ngokungcolileyo.
37 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufayo chikagwera pa mbewu zimene akuti adzale, mbewu zimenezo zidzakhalabe zabwino.
Njalo uba okwesidumbu sazo kuwela phezu kwenhlanyelo ehlanyelwayo ezahlanyelwa, ihlambulukile;
38 Koma mbewuzo zikakhala zonyowa ndi madzi, ndipo chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo chikagwera pa mbewuzo, mbewuzo zikhale zodetsedwa kwa inu.
kodwa uba okwamanzi kufakwa enhlanyelweni, lokwesidumbu sazo kuwela phezu kwayo, ingcolile kini.
39 “‘Ngati nyama imene mumaloledwa kudya yafa yokha, ndiye kuti aliyense wokhudza nyama yakufayo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Uba kusifa-ke enyamazaneni eyikudla kini, othinta isidumbu sayo uzakuba ngongcolileyo kuze kuhlwe.
40 Aliyense amene adyako nyama yakufayo achape zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Aliyense amene wanyamula nyama yakufayo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
Lodla okwesidumbu sayo uzahlamba izembatho zakhe, abe ngongcolileyo kuze kuhlwe; lothwala isidumbu sayo uzawatsha izembatho zakhe, abe ngongcolileyo kuze kuhlwe.
41 “‘Chinthu chilichonse chokwawa pansi ndi chonyansa, simuyenera kudya.
Lazo zonke ezihuquzelayo ezihuquzela emhlabeni ziyisinengiso; kaziyikudliwa.
42 Musadye chilichonse chokwawa pansi, choyenda chamimba kapena choyenda ndi miyendo inayi kapenanso yambiri popeza ndi chodetsedwa.
Konke okuhamba ngesisu, lakho konke okuhamba ngezine, kuze kube yikho konke okulenyawo ezinengi, phakathi kwazo zonke ezihuquzelayo ezihuquzela emhlabeni kaliyikukudla, ngoba kuyisinengiso.
43 Musadzisandutse nokha odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. Musadziyipitse nazo, kuti mukhale odetsedwa.
Lingazenzi linengeke langakuphi okuhuquzelayo kuhuquzela, lingazingcolisi ngakho ukuthi lingcoliswe yikho.
44 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, choncho dziyeretseni kuti mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera. Musadzisandutse odetsedwa ndi chokwawa chilichonse.
Ngoba ngiyiNkosi uNkulunkulu wenu. Ngakho zingcweliseni, libe ngcwele, ngoba ngingcwele. Lingazingcolisi langakuphi okuhuquzelayo okuhuquzela emhlabeni.
45 Ine ndine Yehova amene ndinakutulutsani ku Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Tsono mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera.
Ngoba ngiyiNkosi eyalenyusa lisuka elizweni leGibhithe ukuthi ngibe nguNkulunkulu wenu. Ngakho banini ngcwele, ngoba ngingcwele.
46 “‘Amenewa ndi malamulo onena za nyama, mbalame, chamoyo chilichonse choyenda mʼmadzi ndiponso chamoyo chilichonse chokwawa.
Lo ngumlayo wezinyamazana lezinyoni, laso sonke isidalwa esiphilayo esibhinqika emanzini lakuso sonke isidalwa esihuquzela emhlabeni,
47 Muzisiyanitsa pakati pa chodetsedwa ndi choyeretsedwa, komanso pakati pa zomwe mutha kudya ndi zomwe simuyenera kudya.’”
ukwehlukanisa phakathi kokungcolileyo lokuhlambulukileyo, laphakathi kokuphilayo okungadliwa lokuphilayo okungadliwayo.

< Levitiko 11 >