< Yona 2 >

1 Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
And Jonas preiede to the Lord his God fro the fischis wombe,
2 Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
and seide, Y criede to God of my tribulacioun, and he herde me; fro the wombe of helle Y criede, and thou herdist my vois. (Sheol h7585)
3 Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
Thou castidist me doun in to depnesse, in the herte of the see, and the flood cumpasside me; alle thi swolowis and thi wawis passiden on me.
4 Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
And Y seide, Y am cast awei fro siyt of thin iyen; netheles eftsoone Y schal see thin hooli temple.
5 Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
Watris cumpassiden me `til to my soule, depnesse enuyrownede me, the see hilide myn heed.
6 Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
Y wente doun to the vtmeste places of hillis, the barris of erthe closiden me togidere, in to withouten ende; and thou, my Lord God, schalt reise vp my lijf fro corrupcioun.
7 “Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
Whanne my soule was angwisched in me, Y bithouyte on the Lord, that my preier come to thee, to thin hooli temple.
8 “Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
Thei that kepen vanytees, forsaken his merci idili.
9 Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
But Y in vois of heriyng schal offre to thee; what euer thingis Y vowide, Y schal yelde to the Lord, for myn helthe.
10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.
And the Lord seide to the fisch, and it castide out Jonas `in to the drie lond.

< Yona 2 >